< Rute 1 >

1 Mu nthawi imene oweruza ankalamulira Israeli, munali njala mʼdziko, ndipo munthu wina wa ku Betelehemu mʼdziko la Yuda anapita pamodzi ndi mkazi wake ndi ana ake aamuna awiri, kukakhala ku Mowabu kwa nthawi yochepa.
Ngezinsuku kubusa abahluleli, kwaba lendlala elizweni. Ngakho indoda ethile yaseBhethilehema koJuda kanye lomkayo lamadodana abo amabili, basuka bayahlala elizweni lamaMowabi okwesikhatshana.
2 Dzina la munthuyo linali Elimeleki, dzina la mkazi wake linali Naomi, ndipo mayina a ana awo aamuna anali Maaloni ndi Kiliyoni. Iwo anali Aefurati ochokera ku Betelehemu ku Yuda. Ndipo anapita kukakhala ku Mowabu.
Ibizo lalindoda lalingu-Elimeleki, elomkakhe linguNawomi, amadodana akhe amabili ayengoMaheloni loKhiliyoni. Babengama-Efrathi aseBhethilehema koJuda. Baya eMowabi bayahlala khona.
3 Kenaka Elimeleki, mwamuna wake wa Naomi anamwalira ndipo Naomiyo anatsala ndi ana ake aamuna awiri aja.
U-Elimeleki, umkaNawomi wafa, wasesala lamadodana akhe womabili.
4 Iwo anakwatira akazi a Chimowabu; wina dzina lake Oripa ndi wina Rute. Atakhala kumeneko pafupifupi zaka khumi,
Athatha abafazi baseMowabi, omunye wayethiwa ngu-Opha omunye ethiwa nguRuthe. Sebehlale lapho okweminyaka elitshumi,
5 Maloni ndi Kiliyoni anamwaliranso kotero kuti Naomi anatsala yekha wopanda ana ake awiri aja ndi mwamuna wake.
bobabili uMaheloni loKhiliyoni labo bafa, uNawomi wasesala engaselamadodana kanye lomkakhe.
6 Naomi ndi apongozi ake awiri aja ananyamuka kubwerera kwawo kuchokera ku Mowabu popeza anali atamva ali ku Mowabuko kuti Yehova anakomera mtima anthu ake ndi kuwapatsa chakudya.
Wathi esizwa eseMowabi ukuthi uThixo wayesesize abantu bakhe ngokubapha ukudla, uNawomi kanye labomalukazana bakhe balungisela ukubuyela kibo.
7 Naomi pamodzi ndi apongozi ake awiri aja anachoka kumene ankakhala ndi kuyamba ulendo obwerera kwawo ku Yuda.
Wasuka endaweni ayekade ehlala kuyo, labomalukazana bakhe bobabili, wangena indlela eyayizabasa emuva elizweni lamaJuda.
8 Kenaka Naomi anati kwa apongozi ake awiri aja, “Bwererani, aliyense kwa amayi ake. Yehova akukomereni mtima, monga munachita ndi malemu aja ndi ine ndemwe.
UNawomi wasesithi kubomalukazana bakhe bobabili, “Buyelani emuva, ngulowo lalowo aye emzini kanina. Engani uThixo angalenzela umusa onjengalowo elingitshengise wona kanye labomkenu asebedlule.
9 “Yehova akuthandizeni kuti aliyense wa inu apeze pokhala pabwino komanso mwamuna.” Kenaka anawapsompsona koma awiriwo analira mokweza.
Sengathi uThixo angenza ukuba ngulowo lalowo athole inhlalo enhle nxa esendele kwenye indoda.” Wasebanga, basebekhala kakhulu
10 Ndipo anati kwa Naomi, “Ife tipita nawo kwa anthu akwanu.”
bathi kuye, “Sizahamba lawe ebantwini bakini.”
11 Koma Naomi anati, “Bwererani kwanu ana anga. Chifukwa chiyani mukufuna kupita ndi ine? Kodi ine ndingaberekenso ana ena kuti akhale amuna anu?
Kodwa uNawomi wathi, “Buyelani ngekhaya madodakazi ami. Kambe lingabe lihambelani lami? Ngingazala amanye amadodana na angaba ngomkenu?
12 Bwererani kwanu ana anga muzipita kwanu. Ine ndakalamba kwambiri kotero kuti sindingakwatiwenso. Ngakhale ndikananena kuti ndili nacho chikhulupiriro, ngakhale ndikanakhala ndi mwamuna usiku uno, ndipo nʼkubala ana aamuna,
Buyelani ngekhaya madodakazi ami. Sengigugile, angingeke ngibe ngisazuza enye indoda. Loba bekungabe kulethemba lokuthi ngende loba bengingaba lendoda ngabona lobubusuku ngizale amadodana,
13 kodi inu mukanadikira kuti akule? Kodi mukanakhalabe osakwatiwa kudikira iwowo? Ayi ana anga. Zimenezi zikundiwawa kwambiri kuposa inu, chifukwa ndi ineyo amene Yehova wafuna kuti ndizunzike.”
lingawamelela aze akhule na? Lingahlala lingendanga lilindele wona na? Hatshi, madodakazi ami. Kubuhlungu kakhulu lokho kimi okwedlula kini ngoba ingalo kaThixo isingihlanekele!”
14 Atamva zimenezi analiranso kwambiri, ndipo Oripa anapsompsona apongozi ake nawatsanzika, koma Rute anakakamirabe.
Bekuzwa lokho bakhala njalo. U-Opha wasesanga uninazala wamvalelisa, kodwa uRuthe wabambelela kuye.
15 Naomi anati “Taona, mʼbale wako wabwerera kwawo kwa anthu ake ndi kwa milungu yake. Bwerera nawenso umulondole mʼbale wako.”
UNawomi wathi, “Khangela, unyanewenu usebuyela kwabakibo kanye labonkulunkulu bakhe. Buyela laye.”
16 Koma Rute anayankha kuti, “Musandikakamize kuti ndikusiyeni kapena kuti ndibwerere osakutsatani. Kumene inu mupite ine ndipita komweko, ndipo kumene mukakhale inenso ndikakhala komweko. Abale anu adzakhala abale anga ndipo Mulungu wanu adzakhala Mulungu wanga.
URuthe waphendula wathi, “Ungangincengi ukuba ngikutshiye loba ukuba ngikufulathele. Lapho oya khona ngizakuya khona, lalapho ozahlala khona ngizahlala khona. Abantu bakini bazakuba ngabakithi loNkulunkulu wakho uzakuba nguNkulunkulu wami.
17 Kumene mukafere inenso ndidzafera komweko ndipo komweko ndikayikidwa mʼmanda. Yehova andichite choyipa chingakule motani, ngati china chingatirekanitse ife kupatula imfa.”
Lapho ozafela khona lami ngizafela khona njalo ngizangcwatshelwa khona. Sengathi uThixo angangihlanekela nxa ngingehlukana lawe ngenxa yolunye ulutho olungesikufa.”
18 Naomi atazindikira kuti Rute watsimikiza kupita naye, analeka kumukakamiza.
Kwathi uNawomi esebonile ukuthi uRuthe uzimisele ukuhamba laye, waseyekela ukumcindezela.
19 Choncho amayi awiriwo anapitiriza ulendo wawo mpaka anakafika ku Betelehemu. Pamene ankafika mu Betelehemu, anthu onse a mʼmudzimo anatekeseka chifukwa cha iwowo ndipo amayi ambiri ankanena kuti, “Kodi uyu nʼkukhala Naomi?”
Basebehamba bobabili baze bayafika eBhethilehema. Bathi befika eBhethilehema, umuzi wonke waba lokuxokozela ngabo, kwathi abesifazane bababaza besithi, “Angabe enguNawomi lo na?”
20 Iye anawawuza kuti, “Musanditchenso Naomi. Muzinditchula ine kuti Mara, chifukwa Wamphamvuzonse wandizunza kwambiri.
Yena wathi kubo, “Lingangibizi ngokuthi nginguNawomi. Wothani nginguMara, ngoba uSomandla wenze impilo yami yaba munyu.
21 Ine ndinapita wolemera, koma Yehova wabwera nane wopanda kanthu. Nanga munditchulirenji Naomi pamene Yehova wandisautsa. Wamphamvuzonse uja wandigwetsera mavuto owawa.”
Ngasuka lapha ngigcwele, kodwa uThixo usengibuyise ngingelalutho. Lingangibizelani ngokuthi nginguNawomi? UThixo ungehlisele uhlupho; uSomandla ungehlisele okubi.”
22 Naomi anabwerera kuchoka ku dziko la Mowabu pamodzi ndi Rute mpongozi wake. Ndipo anafika ku Betelehemu nthawi yoyamba kukolola barele.
Ngakho uNawomi wabuyela ngokunjalo eBhethilehema evela eMowabi. Wafika ephelekezelwa nguRuthe umalukazana wakhe waseMowabi. Bafika ngesikhathi sokuqalisa ukuvuna ibhali.

< Rute 1 >