< Aroma 9 >

1 Ine ndikunena zoona mwa Khristu. Sindikunama ndipo chikumbumtima changa kudzera mwa Mzimu Woyera chikundichitira umboni.
Правду кажу в Христї, не обманюю, як сьвідкуе менї (й) совість моя Духом сьвятим,
2 Ndili ndi chisoni chachikulu ndipo ndikumva kupwetekeka kosalekeza mu mtima mwanga.
що великий мені смуток, і без устання болесть серцю моєму.
3 Pakuti ndikanafuna ine mwini nditatembereredwa ndi kuchotsedwa mwa Khristu chifukwa cha abale anga, amene ndi a mtundu wanga,
Бо я сам бажав би бути відлученим від Христа за братів моїх, рідних мені по тїлу;
4 anthu Aisraeli. Iwo anasankhidwa kukhala ana. Mulungu anawapatsa ulemerero, anachita nawo mapangano, kuwapatsa Malamulo, Nyumba yopembedzeramo ndi malonjezano ake.
вони ж Ізраїльтяне, їх усиновленнє, і слава, й завіти, й даваннє закону, й судженнє, і обітування;
5 Awo ndi makolo athu. Kuchokera kwa iwo mʼthupi ndi kumene kunachokera makolo a Khristu Yesu amene ndi Mulungu wolamulira zinthu zonse, alemekezeke mpaka muyaya! Ameni. (aiōn g165)
їх і отці, з них і Христос по тїлу, що над усїм Бог, благословенний по віки. Амінь. (aiōn g165)
6 Sikuti mawu a Mulungu analephera. Pakuti si onse obadwa mwa Israeli amene ndi Israeli.
Не те ж воно, наче б слово Боже не сповнилось; бо не всі ті, що від Ізраїля, сї Ізраїльтяне,
7 Kapena kuti ana ake chifukwa anachokera mwa Abrahamu. Koma zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.
анї всі дїти, тим що вони насіннє Авраамове; нї, в Ісаакові (рече) назветь ся тобі насіннє.
8 Kutanthauza kuti, si ana obadwa mʼthupi amene ndi ana a Mulungu koma ndi ana a lonjezano amene amatengedwa kukhala zidzukulu za Abrahamu.
Се єсть: не дїти тїлесні, се дїти Божі, а дїти обітування полічені в насіннє.
9 Pakuti Mulungu analonjeza ponena kuti, “Pa nthawi yake ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.”
Слово бо обітування таке! Пори сієї прийду, і буде Сарі син.
10 Ndipo si pokhapo ayi. Ana awiri a Rebeka aja abambo awo anali mmodzi, kholo lathu Isake.
Не тільки ж (се); а й Ревека, що почала за одним разом од Ісаака, отця нашого;
11 Komabe, ana amapasawa asanabadwe kapena asanachite chilichonse chabwino kapena choyipa, nʼcholinga choti chifuniro cha Mulungu chosankhiratu munthu aliyense chipitirire,
ще бо не родились, анї зробили нічого доброго або лихого (щоб постанова Божа у вибранню пробувала, не по дїлам, а від Того, хто кличе).
12 osati chifukwa cha ntchito za munthu koma chifuniro cha Iye mwini, anawuza Rebeka kuti, “Wamkulu adzatumikira wamʼngʼono.”
сказано їй, що більший служити ме меншому,
13 Monga momwe kwalembedwa kuti, “Ine ndinakonda Yakobo, koma ndinamuda Esau.”
яко ж писано: Якова злюбив я, а Ісава зненавидів.
14 Nanga tsono tidzanena chiyani? Kodi Mulungu ndi osalungama? Ayi, ndi pangʼono pomwe!
Що ж скажемо? чи вже ж несправедливість у Бога? Нехай не буде.
15 Pakuti Mulungu anawuza Mose kuti, “Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo, ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”
Глаголе бо Мойсейові: Помилую, кого помилую, і змилосерджусь, над ким змилосерджусь.
16 Nʼchifukwa chake, izi sizitengera zokhumba za munthu kapena kuyesetsa koma chifundo cha Mulungu.
Тим же воно нї від того, хто хоче, нї від того, хто біжить, а від милуючого Бога.
17 Malemba akuti Mulungu anamuwuza Farao kuti, “Ine ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga, kuti mwa iwe dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.”
Глаголе бо писаннє й Фараонові: Що на се іменно підняв я тебе, щоб показати на тобі силу мою, і щоб звістилось імя мов по всій землі.
18 Choncho Mulungu amachitira chifundo munthu amene akufuna kumuchitira chifundo ndipo amawumitsa mtima munthu amene Iye akufuna kumuwumitsa mtima.
Тим ж то, кого хоче, милує, а кого хоче, ожорсточує (окаменює).
19 Tsono mmodzi wa inu nʼkundifunsa kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mulungu amatipeza olakwa? Nanga ndani amene amakana chifuniro chake?”
Скажеш же мені: Чого ж іще й винуватить? хто встояв проти волї Його?
20 Koma ndiwe yani, munthu wamba, woti nʼkutsutsana ndi Mulungu? “Kodi chimene chinawumbidwa nʼkufunsa amene anachiwumba kuti, ‘Kodi unandiwumbiranji motere?’”
Хто ж се ти, чоловіче, що змагаєш ся з Богом? Хиба скаже зроблене тому, хто зробив його: Нащо вробив єси мене так?
21 Kodi wowumba alibe ufulu wowumba kuchokera ku dothi lomwelo mbiya yamtengowapatali ndi ina yamtengo wotsika?
Або не має впасти ганчар над глиною, щоб з того самого місива зробити одну посудину на честь, а другу на нечесть?
22 Koma Mulungu, anafuna kuonetsa mkwiyo wake ndi kuti mphamvu yake idziwike. Iye anapirira modekha mtima kwambiri zochita za anthu omwe anawakwiyirawo amene anayeneradi chiwonongeko.
Коли ж, хотячи Бог показати гнїв свій, і явити силу свою, щадив у великому довготерпінню посуди гнїва, наготовлені на погибель,
23 Iye anachita izi kufuna kuonetsa kulemera kwa ulemerero wake ndi kuti udziwike kwa amene analandira chifundo chake. Iye anawakonzeratu kuti alandire ulemerero wake
і щоб явити богацтво слави своєї на посудах милости, котрих наперед наготовив на славу,
24 ngakhale ifenso amene anatiyitana osati kuchokera kwa Ayuda okha komanso kwa a mitundu ina.
як і над нами, котрих покликав не тільки з Жидів, та й з поган?
25 Monga momwe Mulungu akunenera mʼbuku la Hoseya kuti, “Amene sanali anthu anga ndidzawatcha ‘anthu anga;’ ndipo Ine ndidzatcha ‘wokondedwa wanga’ amene sali wokondedwa wanga,”
Як і в Осії глаголе: Назву немоїх людей людьми моїми, і неполюблену полюбленою.
26 ndipo, “Pamalo omwewo pamene ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti, ‘Ana a Mulungu wamoyo.’”
І буде на місцї, де сказано їм: не мій ви народ, там назвуть ся синами Бога живого.
27 Yesaya anafuwula za Aisraeli kuti, “Ngakhale chiwerengero cha Aisraeli chingakhale ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiye adzapulumuke.
Ісаія ж покликує про Ізраїля: Хочби було число синів Ізраїлевих як пісок морський, останок (тільки) спасеть ся:
28 Pakuti Ambuye adzagamula milandu ya anthu pa dziko lapansi mofulumira ndi kumaliziratu.”
скінчивши бо слово, поскорить ся в правдї; бо скоро слово зробить Господь на землі.
29 Monga momwe Yesaya ananena malo ena kuti, “Ngati Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira zidzukulu, ife tikanawonongeka ngati anthu a ku Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.”
І яко ж прорік Ісаія: Коли б Господь Саваот не зоставив нам насїння, були б ми, як Содома, й уподобились би Гоморі.
30 Kodi nanga tidzati chiyani? Tidzati a mitundu ina amene sanafune chilungamo analandira chilungamo chachikhulupiriro
Що ж скажемо? Що погане, котрі не вганяли за праведностю, настигли праведність, праведність, що од віри;
31 koma Aisraeli, amene anafuna chilungamo cha lamulo sanachilandire.
Ізраїль же, вганяючи за праведностю, не настиг закону праведности.
32 Chifukwa chiyani? Chifukwa iwo sanachifune ndi chikhulupiriro koma ngati mwa ntchito. Iwo anapunthwa pa “Mwala wopunthwitsa.”
Чому? Тому, що (шукали праведности) не од віри, а якби од учинків закону; спіткнулись бо на камінь спотикання.
33 Monga momwe kwalembedwa kuti, “Taonani, Ine ndikuyika mwala mu Ziyoni wopunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Koma amene akhulupirira Iye sadzachititsidwa manyazi.”
Яко ж писано: Ось кладу в Сіонї камінь спотикання і камень поблазнї, а всякий, хто вірув в Него, не осоромить ся.

< Aroma 9 >