< Aroma 9 >

1 Ine ndikunena zoona mwa Khristu. Sindikunama ndipo chikumbumtima changa kudzera mwa Mzimu Woyera chikundichitira umboni.
I speak the truth in Christ, I lie not, my conscience bearing me witness in the Holy Ghost,
2 Ndili ndi chisoni chachikulu ndipo ndikumva kupwetekeka kosalekeza mu mtima mwanga.
that there is great sorrow to me and incessant grief to my heart.
3 Pakuti ndikanafuna ine mwini nditatembereredwa ndi kuchotsedwa mwa Khristu chifukwa cha abale anga, amene ndi a mtundu wanga,
For I would pray, that I myself might be an offering from Christ; in behalf of my brethren, my kindred according to the flesh:
4 anthu Aisraeli. Iwo anasankhidwa kukhala ana. Mulungu anawapatsa ulemerero, anachita nawo mapangano, kuwapatsa Malamulo, Nyumba yopembedzeramo ndi malonjezano ake.
who are Israelites, of whom is the adoption of sons, and the glory, and the covenants, and the giving of the law, and the service, and the promises:
5 Awo ndi makolo athu. Kuchokera kwa iwo mʼthupi ndi kumene kunachokera makolo a Khristu Yesu amene ndi Mulungu wolamulira zinthu zonse, alemekezeke mpaka muyaya! Ameni. (aiōn g165)
of whom are the fathers, and of whom is Christ according to the flesh. Who is over all, God blessed forever: amen. (aiōn g165)
6 Sikuti mawu a Mulungu analephera. Pakuti si onse obadwa mwa Israeli amene ndi Israeli.
But not as that the word of God has been a failure. For these are not all Israel who are of Israel;
7 Kapena kuti ana ake chifukwa anachokera mwa Abrahamu. Koma zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.
neither are the children all the seed of Abraham; but in Isaac shall thy seed be called;
8 Kutanthauza kuti, si ana obadwa mʼthupi amene ndi ana a Mulungu koma ndi ana a lonjezano amene amatengedwa kukhala zidzukulu za Abrahamu.
that is the children of the flesh the same are not the children of God; but the children of the promise are counted for the seed.
9 Pakuti Mulungu analonjeza ponena kuti, “Pa nthawi yake ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.”
For this is the word of the promise, About this time I will come, and there shall be a son to Sarah.
10 Ndipo si pokhapo ayi. Ana awiri a Rebeka aja abambo awo anali mmodzi, kholo lathu Isake.
Not only so; but Rebecca also having cohabitation of one, our father Isaac;
11 Komabe, ana amapasawa asanabadwe kapena asanachite chilichonse chabwino kapena choyipa, nʼcholinga choti chifuniro cha Mulungu chosankhiratu munthu aliyense chipitirire,
for the children not having been born, neither having done anything good or evil, in order that the purpose of God might stand according to election not of works, but of him that calleth,
12 osati chifukwa cha ntchito za munthu koma chifuniro cha Iye mwini, anawuza Rebeka kuti, “Wamkulu adzatumikira wamʼngʼono.”
and it was said to her, The elder shall serve the younger:
13 Monga momwe kwalembedwa kuti, “Ine ndinakonda Yakobo, koma ndinamuda Esau.”
as has been written, Jacob have I loved, but Esau have I hated.
14 Nanga tsono tidzanena chiyani? Kodi Mulungu ndi osalungama? Ayi, ndi pangʼono pomwe!
Then what shall we say? Is there unrighteousness with God? It could not be so.
15 Pakuti Mulungu anawuza Mose kuti, “Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo, ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”
For he says to Moses, I will have mercy on whom I do have mercy, and I will commiserate whom I do commiserate.
16 Nʼchifukwa chake, izi sizitengera zokhumba za munthu kapena kuyesetsa koma chifundo cha Mulungu.
Then it is not of him that willeth, nor him that runneth, but of God who shows mercy.
17 Malemba akuti Mulungu anamuwuza Farao kuti, “Ine ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga, kuti mwa iwe dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.”
For the scripture says to Pharaoh, For this very thing have I raised you up, that I may show forth my power in you, and that my name may be proclaimed in all the earth.
18 Choncho Mulungu amachitira chifundo munthu amene akufuna kumuchitira chifundo ndipo amawumitsa mtima munthu amene Iye akufuna kumuwumitsa mtima.
Then therefore he has mercy on whom he will, and whom he will he hardens.
19 Tsono mmodzi wa inu nʼkundifunsa kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mulungu amatipeza olakwa? Nanga ndani amene amakana chifuniro chake?”
Then thou wilt say to me, Why does he yet find fault? For who has resisted his will?
20 Koma ndiwe yani, munthu wamba, woti nʼkutsutsana ndi Mulungu? “Kodi chimene chinawumbidwa nʼkufunsa amene anachiwumba kuti, ‘Kodi unandiwumbiranji motere?’”
O man, who art thou that repliest against God? Whether shall the thing formed say to him that formed it. Why did you make me thus?
21 Kodi wowumba alibe ufulu wowumba kuchokera ku dothi lomwelo mbiya yamtengowapatali ndi ina yamtengo wotsika?
Has not the potter the right of the clay, from the same lump to make one part a vessel unto honor, and another unto dishonor?
22 Koma Mulungu, anafuna kuonetsa mkwiyo wake ndi kuti mphamvu yake idziwike. Iye anapirira modekha mtima kwambiri zochita za anthu omwe anawakwiyirawo amene anayeneradi chiwonongeko.
But if God, wishing to show forth his indignation and make his power known, endured with much longsuffering the vessels of indignation having been perfected unto destruction:
23 Iye anachita izi kufuna kuonetsa kulemera kwa ulemerero wake ndi kuti udziwike kwa amene analandira chifundo chake. Iye anawakonzeratu kuti alandire ulemerero wake
and in order that he might make known the riches of his glory on the vessels of mercy, which he before prepared unto glory?
24 ngakhale ifenso amene anatiyitana osati kuchokera kwa Ayuda okha komanso kwa a mitundu ina.
whom he called, even us, not only of the Jews, but also of the Gentiles:
25 Monga momwe Mulungu akunenera mʼbuku la Hoseya kuti, “Amene sanali anthu anga ndidzawatcha ‘anthu anga;’ ndipo Ine ndidzatcha ‘wokondedwa wanga’ amene sali wokondedwa wanga,”
as he says in Hosea, I will call them my people, who are not my people; and her beloved, who is not beloved:
26 ndipo, “Pamalo omwewo pamene ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti, ‘Ana a Mulungu wamoyo.’”
and it shall come to pass, in the place in which it was said to them, You are not my people, there they shall be called the sons of the living God:
27 Yesaya anafuwula za Aisraeli kuti, “Ngakhale chiwerengero cha Aisraeli chingakhale ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiye adzapulumuke.
but Isaiah cries out in behalf of Israel, Though the number of sons of Israel may be as the sand of the sea, a remnant shall be saved.
28 Pakuti Ambuye adzagamula milandu ya anthu pa dziko lapansi mofulumira ndi kumaliziratu.”
For perfecting the word and cutting it short, will the Lord do a complete work on the earth:
29 Monga momwe Yesaya ananena malo ena kuti, “Ngati Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira zidzukulu, ife tikanawonongeka ngati anthu a ku Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.”
and as Isaiah has before spoken; Unless the Lord of Sabaoth left to us a seed, we would have become as Sodom, and would have been made like unto Gomorrah:
30 Kodi nanga tidzati chiyani? Tidzati a mitundu ina amene sanafune chilungamo analandira chilungamo chachikhulupiriro
Then what shall we say? That the Gentiles, not pursuing righteousness, received righteousness, and the righteousness which is from faith:
31 koma Aisraeli, amene anafuna chilungamo cha lamulo sanachilandire.
but Israel, following after the law, did not attain unto the law of righteousness.
32 Chifukwa chiyani? Chifukwa iwo sanachifune ndi chikhulupiriro koma ngati mwa ntchito. Iwo anapunthwa pa “Mwala wopunthwitsa.”
Why? Because they sought it not from faith, but as it were from works: they stumbled over the stone of stumbling,
33 Monga momwe kwalembedwa kuti, “Taonani, Ine ndikuyika mwala mu Ziyoni wopunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Koma amene akhulupirira Iye sadzachititsidwa manyazi.”
as has been written, Behold, I lay in Zion a stone of stumbling and a rock of offence: and he that believeth on him shall not be ashamed.

< Aroma 9 >