< Aroma 9 >

1 Ine ndikunena zoona mwa Khristu. Sindikunama ndipo chikumbumtima changa kudzera mwa Mzimu Woyera chikundichitira umboni.
Christ sung ah thuman ka son hi, leilot ngawl khi hi, keima i sia le pha heak na in Tha Thiangtho sung ah tettipang hi.
2 Ndili ndi chisoni chachikulu ndipo ndikumva kupwetekeka kosalekeza mu mtima mwanga.
Ka thinsung ah vanngit lianpi le a tawntung in khuangai na ka nei hi.
3 Pakuti ndikanafuna ine mwini nditatembereredwa ndi kuchotsedwa mwa Khristu chifukwa cha abale anga, amene ndi a mtundu wanga,
Cilesa deina taw ka suapui te atu in keima tatak sia Christ kung pan in hamsiat ka thuak nuam zaw liang hi:
4 anthu Aisraeli. Iwo anasankhidwa kukhala ana. Mulungu anawapatsa ulemerero, anachita nawo mapangano, kuwapatsa Malamulo, Nyumba yopembedzeramo ndi malonjezano ake.
Amate sia Israel mite hi uh a; amate sia ta suasak na, minthanna, kamciam te, dan piakna, Pathian nasep le kamciam te taw a ki zom te a hihi;
5 Awo ndi makolo athu. Kuchokera kwa iwo mʼthupi ndi kumene kunachokera makolo a Khristu Yesu amene ndi Mulungu wolamulira zinthu zonse, alemekezeke mpaka muyaya! Ameni. (aiōn g165)
Amate sia pu le pa te taw ki zom in, Christ zong cilesa ngeina taw amate sung pan hong theng a hihi, tua Christ sia na theampo tung ah om a, Pathian in a tawntung in thupha pia hi. Amen. (aiōn g165)
6 Sikuti mawu a Mulungu analephera. Pakuti si onse obadwa mwa Israeli amene ndi Israeli.
Pathian thu sia mannung ngawl hi, cinopna hi ngawl hi. Banghangziam cile Israel mi theampo in Israel mi tatak hi siat ngawl hi.
7 Kapena kuti ana ake chifukwa anachokera mwa Abrahamu. Koma zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.
Abraham i suan le pal theampo sia a tate hi siat ngawl hi: ahihang, Isaac bek ah na suanlepal kip tu hi.
8 Kutanthauza kuti, si ana obadwa mʼthupi amene ndi ana a Mulungu koma ndi ana a lonjezano amene amatengedwa kukhala zidzukulu za Abrahamu.
Hi thu sia, cilesa ngeina taw Abraham tate theampo sia Pathian tate hi ngawl hi, ahihang kamciam i tate sia a suan le pal in ceptesak hi.
9 Pakuti Mulungu analonjeza ponena kuti, “Pa nthawi yake ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.”
Banghangziam cile hisia sia kamciam kammal a hihi, hibang hun in kong paikik tu a, Sarah in tapa nei tu hi.
10 Ndipo si pokhapo ayi. Ana awiri a Rebeka aja abambo awo anali mmodzi, kholo lathu Isake.
Hi thu bek hi ngawl hi; ahihang Rebecca zong eite i pa Isaac taw in naupai hi;
11 Komabe, ana amapasawa asanabadwe kapena asanachite chilichonse chabwino kapena choyipa, nʼcholinga choti chifuniro cha Mulungu chosankhiratu munthu aliyense chipitirire,
A tate suak ngawl lai in, a pha le a pha ngawl bangma vawt ngawl lai hi napi, Pathian i ngeal na sia tealsa bangma in a kip thei natu, sep na tungtawn hi ngawl in, amate a sam pa hang a hi zawkna sia;
12 osati chifukwa cha ntchito za munthu koma chifuniro cha Iye mwini, anawuza Rebeka kuti, “Wamkulu adzatumikira wamʼngʼono.”
Rebecca tung ah, a upa in a naupa i na seam tu hi, ci hi.
13 Monga momwe kwalembedwa kuti, “Ine ndinakonda Yakobo, koma ndinamuda Esau.”
Jacob ka it hi, ahihang Esau ka ensan hi, ci at khol hi.
14 Nanga tsono tidzanena chiyani? Kodi Mulungu ndi osalungama? Ayi, ndi pangʼono pomwe!
Tabang hile bang i son thua tu ziam? Pathian sung ah thutan ngawl na om ziam? Om vet ngawl hi.
15 Pakuti Mulungu anawuza Mose kuti, “Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo, ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”
Banghangziam cile Moses tung ah, ka hesuak nop te tung ah hesuakna ka nei tu hi, taciang ka mulkim nop te tung ah mulkim na ka nei tu hi, ci hi.
16 Nʼchifukwa chake, izi sizitengera zokhumba za munthu kapena kuyesetsa koma chifundo cha Mulungu.
Tua ahikom hi thu sia dei thu le taikhiat na thu hang hi ngawl a, hesuakna a kilangsak Pathian hang a hihi.
17 Malemba akuti Mulungu anamuwuza Farao kuti, “Ine ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga, kuti mwa iwe dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.”
Banghangziam cile laithiangtho in Pharaoh tung ah, nangma tung ah ka vangletna ka kilangsak thei natu le ka min sia leitung mun theampo ah ki thangsak tu, ci tupna taw in kong zang hi, ci hi.
18 Choncho Mulungu amachitira chifundo munthu amene akufuna kumuchitira chifundo ndipo amawumitsa mtima munthu amene Iye akufuna kumuwumitsa mtima.
Tua ahikom Pathian in a hesuak nop te tung ah hesuakna nei a, a deisak mite lungtang khauhsak hi.
19 Tsono mmodzi wa inu nʼkundifunsa kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mulungu amatipeza olakwa? Nanga ndani amene amakana chifuniro chake?”
Tabang hile nangma in ka tung ah, banghang in Pathian in maw hong zong lai ziam? hong ci tu ni hi. Banghangziam cile a kua in Pathian deina nial tu ziam?
20 Koma ndiwe yani, munthu wamba, woti nʼkutsutsana ndi Mulungu? “Kodi chimene chinawumbidwa nʼkufunsa amene anachiwumba kuti, ‘Kodi unandiwumbiranji motere?’”
Ahihang, mihing pa awng, Pathian a zo kik tu in nangma sia akua ni ziam? Banghang in hibang in hong vawt ni ziam, ci in a vawtsa nate in a vawtpa tung ah ci tu ziam?
21 Kodi wowumba alibe ufulu wowumba kuchokera ku dothi lomwelo mbiya yamtengowapatali ndi ina yamtengo wotsika?
Tungman lomkhat pan in beal khat sia a zatak huai in vawt tu le, a dang khat sia zatak huai ngawl in vawt tu sia, beal vawt pa in tungman tung ah thu nei hi ngawl ziam?
22 Koma Mulungu, anafuna kuonetsa mkwiyo wake ndi kuti mphamvu yake idziwike. Iye anapirira modekha mtima kwambiri zochita za anthu omwe anawakwiyirawo amene anayeneradi chiwonongeko.
Pathian in a thin-ukna kilangsak nuam a, a thunei na a hesak nuam le, suksiat tu in a vawtsa thin-ukna beal te sia thinsautak in thuak hi:
23 Iye anachita izi kufuna kuonetsa kulemera kwa ulemerero wake ndi kuti udziwike kwa amene analandira chifundo chake. Iye anawakonzeratu kuti alandire ulemerero wake
Taciang minthanna tu in a puakhol sate sia hesuakna beal te tung ah a minthanna i letna hesak tu hi,
24 ngakhale ifenso amene anatiyitana osati kuchokera kwa Ayuda okha komanso kwa a mitundu ina.
Eite na ngawn, a saptuam te i hihi, Judah mite bek hi ngawl in, Gentile mite zong sam hi ngawl ziam?
25 Monga momwe Mulungu akunenera mʼbuku la Hoseya kuti, “Amene sanali anthu anga ndidzawatcha ‘anthu anga;’ ndipo Ine ndidzatcha ‘wokondedwa wanga’ amene sali wokondedwa wanga,”
Hosea laibu sung ah zong, ka mite a hi ngawl te ka mite, ka ci tu hi; taciang ka it ngawl te zong, ka it te, ka ci tu hi.
26 ndipo, “Pamalo omwewo pamene ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti, ‘Ana a Mulungu wamoyo.’”
Tua zawkciang in amate tung ah, note ka mi na hi bua uh hi, ka ci na mun ah; a nungta Pathian tate, ci in amate ka sam tu hi, ci hi.
27 Yesaya anafuwula za Aisraeli kuti, “Ngakhale chiwerengero cha Aisraeli chingakhale ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiye adzapulumuke.
Isaiah in zong Israel mite taw kisai in, Israel tate sia tuipi ah senneal za hinapi, a tanglai te bek ngupna nga tu hi:
28 Pakuti Ambuye adzagamula milandu ya anthu pa dziko lapansi mofulumira ndi kumaliziratu.”
Banghangziam cile Ama in nasep man tu hi, taciang thutang suana taw a tomno in tan tu hi:
29 Monga momwe Yesaya ananena malo ena kuti, “Ngati Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira zidzukulu, ife tikanawonongeka ngati anthu a ku Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.”
Taciang Isaiah in hi thu te i mai ah, ngalkaphon te i Topa in thaici khe ngawl hile, eite sia Sodom le Gomorah bang i hi siat tu hi, ci hi.
30 Kodi nanga tidzati chiyani? Tidzati a mitundu ina amene sanafune chilungamo analandira chilungamo chachikhulupiriro
Tabang hile bang i son tu ziam? Thutang suana a del ngawl Gentile mite in thutang suana phaban hi, tua thu sia upna hang in thutang suana a hihi.
31 koma Aisraeli, amene anafuna chilungamo cha lamulo sanachilandire.
Ahihang thutang suana a del Israel mite in, thutang suana i thukham sia phaban ngawl hi.
32 Chifukwa chiyani? Chifukwa iwo sanachifune ndi chikhulupiriro koma ngati mwa ntchito. Iwo anapunthwa pa “Mwala wopunthwitsa.”
Banghangziam? Amate in upna taw a zong bua uh hi, thukham i sepna te taw a zon uh hang a hihi. Tabang in amate sia lutu theina suang tung ah lutu uh hi;
33 Monga momwe kwalembedwa kuti, “Taonani, Ine ndikuyika mwala mu Ziyoni wopunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Koma amene akhulupirira Iye sadzachititsidwa manyazi.”
En vun, Zion ah lutusak thei suang le lutu na suangtum ka koi hi: taciang akuamapo Ama a um peuma a maizum ngawl tu hi, ci in at khol hi.

< Aroma 9 >