< Aroma 6 >

1 Nanga tinene chiyani? Kodi tipitirire kuchimwa kuti chisomo chichulukebe?
What shall we say then? Shall we continue in sin, that grace may abound?
2 Ayi. Mʼnjira iliyonse! Popeza tinafa ku tchimo, nanga tidzapitirira bwanji kukhalabe mʼmenemo?
God forbid. We who died to sin, how shall we any longer live therein?
3 Kodi simukudziwa kuti tonse amene tinabatizidwa mwa Khristu Yesu tinabatizidwa mu imfa yake?
Or are ye ignorant that all we who were baptized into Christ Jesus were baptized into his death?
4 Chifukwa chake ife tinayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Iye mwa ubatizo. Tinalowa mu imfa ndi cholinga choti monga momwe Khristu anaukitsidwa kwa akufa ndi ulemerero wa Atate, ifenso tikakhale mʼmoyo watsopano.
We were buried therefore with him through baptism into death: that like as Christ was raised from the dead through the glory of the Father, so we also might walk in newness of life.
5 Pakuti ngati ife tinakhala amodzi ndi Iye mu imfa yake, tidzakhalanso ndithu amodzi ndi Iye mu kuuka kwake.
For if we have become united with [him] by the likeness of his death, we shall be also [by the likeness] of his resurrection;
6 Ife tikudziwa kuti umunthu wathu wakale unapachikidwa pamodzi ndi Iye kuti thupi la uchimo likhale lopanda mphamvu ndi kuti tisakakhalenso akapolo a tchimo
knowing this, that our old man was crucified with [him], that the body of sin might be done away, that so we should no longer be in bondage to sin;
7 chifukwa aliyense amene anafa anamasuka ku tchimo.
for he that hath died is justified from sin.
8 Koma ngati tinafa pamodzi ndi Khristu, tikhulupirira kuti tidzakhalanso ndi moyo pamodzi ndi Iye.
But if we died with Christ, we believe that we shall also live with him;
9 Pakuti tikudziwa kuti popeza Khristu anaukitsidwa kwa akufa, Iye sangafenso. Imfa ilibenso mphamvu pa Iye.
knowing that Christ being raised from the dead dieth no more; death no more hath dominion over him.
10 Imfa imene Iye anafa, anafa ku tchimo kamodzi kokha, koma moyo umene akhala ndi wa kwa Mulungu.
For the death that he died, he died unto sin once: but the life that he liveth, he liveth unto God.
11 Kotero inunso, mudzione nokha ngati akufa ku tchimo koma a moyo kwa Mulungu mwa Khristu Yesu.
Even so reckon ye also yourselves to be dead unto sin, but alive unto God in Christ Jesus.
12 Nʼchifukwa chake, musalole tchimo lilamulire matupi anu amene anafa kuti mumvere zilakolako zonyansa.
Let not sin therefore reign in your mortal body, that ye should obey the lusts thereof:
13 Musapereke ziwalo zathupi lanu ku tchimo, ngati zipangizo zamakhalidwe oyipa. Mʼmalo mwake, mudzipereke kwa Mulungu, ngati amene achoka ku imfa kupita ku moyo. Ndipo mupereke ziwalo zathupi lanu ngati zipangizo zachilungamo.
neither present your members unto sin [as] instruments of unrighteousness; but present yourselves unto God, as alive from the dead, and your members [as] instruments of righteousness unto God.
14 Tchimo silidzakhalanso ndi mphamvu pa inu, chifukwa Malamulo sakulamulira moyo wanu koma chisomo.
For sin shall not have dominion over you: for ye are not under law, but under grace.
15 Nʼchiyani tsono? Kodi tidzichimwa chifukwa sitikulamulidwa ndi Malamulo koma chisomo? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi!
What then? shall we sin, because we are not under law, but under grace? God forbid.
16 Kodi inu simudziwa kuti pamene mudzipereka kwa wina wake, kumumvera ngati akapolo, ndinu akapolo a amene mumumvera? Ngati ndinu akapolo a tchimo mudzafa. Koma ngati ndinu akapolo akumvera, mudzakhala olungama pamaso pake.
Know ye not, that to whom ye present yourselves [as] servants unto obedience, his servants ye are whom ye obey; whether of sin unto death, or of obedience unto righteousness?
17 Koma ayamikidwe Mulungu pakuti ngakhale munali akapolo a tchimo, munamvera ndi mtima wonse chiphunzitso chimene munalandira.
But thanks be to God, that, whereas ye were servants of sin, ye became obedient from the heart to that form of teaching whereunto ye were delivered;
18 Inu munamasulidwa ku tchimo ndipo tsopano mwasanduka akapolo achilungamo.
and being made free from sin, ye became servants of righteousness.
19 Ine ndikufanizira zinthu za tsiku ndi tsiku chifukwa chikhalidwe chanu nʼchofowoka. Monga momwe munkapereka ziwalo za matupi kukhala akapolo a zonyansa ndi makhalidwe oyipa, zimene zimanka zichulukirabe, choncho tsopano dziperekeni ziwalozo kuti zikhale akapolo achilungamo ndi a kuyera mtima.
I speak after the manner of men because of the infirmity of your flesh: for as ye presented your members [as] servants to uncleanness and to iniquity unto iniquity, even so now present your members [as] servants to righteousness unto sanctification.
20 Pomwe munali akapolo atchimo, simunkalabadira za chilungamo.
For when ye were servants of sin, ye were free in regard of righteousness.
21 Kodi munapeza phindu lanji pochita zinthu zimenezi, zomwe tsopano mukuchita nazo manyazi? Zinthu zimenezo zotsatira zake ndi imfa!
What fruit then had ye at that time in the things whereof ye are now ashamed? for the end of those things is death.
22 Koma tsopano pakuti inu mwamasulidwa ku tchimo ndipo mwasanduka akapolo a Mulungu, phindu lomwe mulipeza ndi kuyera mtima ndipo chotsatira chake ndi moyo wosatha. (aiōnios g166)
But now being made free from sin, and become servants to God, ye have your fruit unto sanctification, and the end eternal life. (aiōnios g166)
23 Pakuti malipiro a tchimo ndi imfa, koma mphatso yaulere imene Mulungu amapereka ndi moyo wosatha mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōnios g166)
For the wages of sin is death; but the free gift of God is eternal life in Christ Jesus our Lord. (aiōnios g166)

< Aroma 6 >