< Aroma 5 >
1 Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
Deci, fiind îndreptățiți prin credință, avem pace cu Dumnezeu, prin Domnul nostru Isus Hristos,
2 Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu.
prin care, de asemenea, avem acces prin credință la acest har în care stăm. Ne bucurăm în speranța gloriei lui Dumnezeu.
3 Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira.
Și nu numai atât, ci ne bucurăm și în suferințele noastre, știind că suferința produce perseverență;
4 Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo.
iar perseverența, caracter dovedit; iar caracterul dovedit, speranță;
5 Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.
iar speranța nu ne dezamăgește, pentru că dragostea lui Dumnezeu a fost revărsată în inimile noastre prin Duhul Sfânt care ne-a fost dat.
6 Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe.
Căci, pe când eram noi încă slabi, Hristos a murit la vremea potrivită pentru cei nelegiuiți.
7 Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera.
Căci cu greu va muri cineva pentru un om neprihănit. Totuși, poate că pentru un om bun cineva chiar va îndrăzni să moară.
8 Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.
Dar Dumnezeu Își recomandă dragostea față de noi, prin faptul că, pe când eram încă păcătoși, Hristos a murit pentru noi.
9 Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu.
Cu atât mai mult, fiind acum îndreptățiți prin sângele Lui, vom fi mântuiți prin El de mânia lui Dumnezeu.
10 Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye?
Căci dacă, pe când eram vrăjmași, am fost împăcați cu Dumnezeu prin moartea Fiului Său, cu atât mai mult, fiind împăcați, vom fi mântuiți prin viața lui.
11 Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.
Și nu numai atât, ci ne și bucurăm în Dumnezeu prin Domnul nostru Isus Hristos, prin care am primit acum împăcarea.
12 Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa.
Așadar, după cum păcatul a intrat în lume printr-un singur om și moartea prin păcat, tot așa și moartea a trecut la toți oamenii, pentru că toți au păcătuit.
13 Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo.
Căci, până la apariția Legii, păcatul era în lume; dar păcatul nu este acuzat când nu există Legea.
14 Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.
Cu toate acestea, moartea a domnit de la Adam până la Moise, chiar și peste cei ale căror păcate nu au fost ca neascultarea lui Adam, care este o prefigurare a celui ce avea să vină.
15 Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri!
Dar darul gratuit nu este ca și fărădelegea. Căci, dacă prin greșeala unuia singur au murit cei mulți, cu atât mai mult harul lui Dumnezeu și darul prin harul unui singur om, Isus Hristos, a abundat pentru cei mulți.
16 Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa.
Darul nu este ca prin unul singur care a păcătuit; căci judecata a venit prin unul singur spre osândă, dar darul gratuit a urmat multor fărădelegi spre îndreptățire.
17 Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.
Căci, dacă prin fărădelegea unuia singur a domnit moartea prin unul singur, cu atât mai mult cei care primesc abundența harului și a darului neprihănirii vor domni în viață prin unul singur, Isus Hristos.
18 Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo.
Astfel, după cum, printr-o singură fărădelege, toți oamenii au fost condamnați, tot așa, printr-o singură faptă de dreptate, toți oamenii au fost îndreptățiți pentru viață.
19 Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.
Căci, după cum prin neascultarea unui singur om, mulți au fost făcuți păcătoși, tot așa, prin ascultarea unuia singur, mulți vor fi făcuți neprihăniți.
20 Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa.
Legea a venit pentru ca fărădelegea să abunde; dar acolo unde a abundat păcatul, harul a abundat și mai mult,
21 Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu. (aiōnios )
pentru ca, după cum păcatul a domnit în moarte, tot așa harul să domnească prin dreptate pentru viața veșnică, prin Isus Hristos, Domnul nostru. (aiōnios )