< Aroma 5 >

1 Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
Since we stand justified as the result of faith, let us continue to enjoy the peace we have with God through our Lord Jesus Christ.
2 Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu.
Through him also we have had our access into this grace in which we have taken our stand, and are exulting in hope of the glory of God.
3 Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira.
And not only so, but we are actually exulting also even in our troubles; for we know that trouble works fortitude,
4 Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo.
and fortitude character, and character, hope -
5 Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.
a hope which never disappoints us. For through the Holy Spirit who has given to us, the "brimming river of the love of God" has overflowed in our hearts.
6 Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe.
For while we were still without strength, Christ died in due time for the ungodly.
7 Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera.
Why, a man will hardly give his life for another, even for a righteous man, though perchance for a good man one might even take it upon himself to die.
8 Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.
But God gives proof of his love to us by the fact that while we were still sinners, Christ died for us.
9 Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu.
By how much more, then, being now justified in his blood, shall we be saved through him from the wrath of God.
10 Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye?
For if, when we were God’s enemies, we were reconciled to him through the death of his Son, how much more, now that we are reconciled, shall we be saved in his life.
11 Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.
And not only that, but we exult in God through our Lord Jesus Christ, through whom we have now obtained our reconciliation.
12 Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa.
Thus, then, sin came into the world through one man, and through sin came death and so death spread to all men, because all had sinned.
13 Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo.
For prior to the Law, sin actually existed in the world, but sin was not set down to man’s account when there was no law.
14 Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.
Nevertheless, from Adam to Moses death reigned as king, even over those who had not sinned after the likeness of Adam’s transgression. Now Adam is a type of Him who was to come.
15 Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri!
But the free gift is not like the transgression; for if through the transgression of that one man the rest on men died, much more did the grace of God and the gift given in his grace in the one Man, Jesus Christ, overflow unto the rest of men.
16 Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa.
And it is not with the free gift as it was through the one that sinned; for the judgment came from one transgression unto condemnation; but the free gift came from many transgressions unto acquittal.
17 Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.
For if through the transgression of the one, death reigned as king through the one, much more shall those who receive the overflowing grace and gift of righteousness reign as kings in life through One, through Jesus Christ.
18 Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo.
It follows then, as through the transgression of one man came condemnation unto all men, even so through the act of righteousness of One came acquittal and life to all men.
19 Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.
For just as through the disobedience of one man the rest were made sinners; even so by the obedience of One shall all the rest be made righteous.
20 Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa.
Now law was brought in so that transgression might abound; but where sin abounded, grace super-abounded;
21 Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu. (aiōnios g166)
in order that as sin has ruled as king in death, so also grace might rule as king in righteousness which issues in eternal life, through Jesus Christ our Lord, - ours! (aiōnios g166)

< Aroma 5 >