< Aroma 4 >

1 Nanga tsono tidzati chiyani za Abrahamu kholo lathu, iyeyu anapezana ndi zotani pa nkhani imeneyi?
Ninia fi aowa A: ibalaha: me ea hou amola ea hawa: hamosu, amo ninia ba: mu da defea.
2 Kunena zoona, Abrahamu akanalungamitsidwa ndi ntchito zake, akanakhala nako kanthu kodzitamandira, koma osati pamaso pa Mulungu.
E da hi hou moloidafa hamoiba: le, Gode da e moloidafa hamoi ganiaba, e da gasa fi hou hamomu da defea gala: loba. Be dunu da gasa fi hamomu, amo Gode da higa: i hodosa.
3 Kodi Malemba akuti chiyani? “Abrahamu anakhulupirira Mulungu, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.”
Gode Sia: da agoane dedei diala, “A: ibalaha: me da Gode Ea hou dafawaneyale dawa: i. Amaiba: le, Gode da A: ibalaha: me afadenene moloidafa hamoi ba: i.”
4 Tsopano munthu amene wagwira ntchito, malipiro ake satengedwa kukhala ngati mphatso koma zimene anayenera kulandira.
Hawa: hamosu dunu da hawa: hamobeba: le, bidi laha. Be ea bidi lai da hahawane dogolegele iasu hame. E da hawa: hamobeba: le fawane lasa.
5 Koma kwa munthu amene sanagwire ntchito ndipo akhulupirira Mulungu amene amalungamitsa ochimwa, chikhulupiriro chakecho chimatengedwa kukhala chilungamo.
Gode da wadela: i hamosu dunu lale, afadenene, dunu moloidafa hamomusa: dawa: Osobo bagade dunu da hi hawa: hamobe amo mae dawa: le, amo dafawaneyale dawa: sea, Gode da amo dunu ea hou afadenene, bu moloidafa hamoi ba: sa.
6 Davide ponena zomwezi pamene anayankhula za kudala kwa munthu amene Mulungu amulungamitsa osati chifukwa cha ntchito zake akuti,
Amo hou Da: ibidi da amane olelei, nowa dunu da mae hawa: hamone, udigili Gode Ea hanaiba: le afadenei moloidafa ba: sa, amo dunu da hahawane bagade.
7 “Odala ndi amene zoyipa zawo zakhululukidwa; amene machimo awo afafanizidwa.
“Dunu da ea wadela: i hou da gogolema: ne olofoi dagoi ba: sa, amo dunu da hahawane bagade.
8 Ngodala munthu amene machimo ake Ambuye sadzawakumbukiranso.”
Gode da amo dunu ea wadela: i hou hobea hamedafa bu dawa: mu. Amaiba: le, e da hahawane bagade!”
9 Kodi madalitso amenewa ali kwa ochita mdulidwe okha kapena kwa amene sanachitepo mdulidwe? Ife takhala tikunena kuti chikhulupiriro cha Abrahamu chinamuchititsa kukhala wolungama.
Amo hahawane hou, gadofo damui dunu fawane da hame dawa: , be gadofo hame damui dunu amola amo hou dawa: lala. Ninia musa: Gode Sia: dedei, amane olelei, “A: ibalaha: me da Gode Ea hou dafawaneyale dawa: i. Amaiba: le, Gode da A: ibalaha: me afadenene, moloidafa hamoi ba: i.”
10 Kodi chinatengedwa bwanji? Kodi nʼkuti iye atachita mdulidwe kapena asanachite? Osati atachita mdulidwe koma asanachite!
Amo hou da habogala hamobela: ? Amo hou da A: ibalaha: me ea gadofo hame damui esoga degabo ba: i.
11 Ndipo iye anachita mdulidwe ngati chizindikiro ndi chitsimikizo cha kulungama kumene anali nako mwachikhulupiriro pomwe anali asanachite mdulidwe. Choncho, iye ndi kholo la onse amene akhulupirira koma sanachite mdulidwe, ndi cholinga chakuti alungamitsidwe.
Gode da A: ibalaha: me moloidafa ba: i. Fa: no e da gadofo damusu hou hamoi. Ea gadofo damui da dawa: digima: ne olelesu fawane. Amo dawa: digima: ne olelesu da e da Gode Ea hou dafawaneyale dawa: beba: le, Gode da A: ibalaha: me moloidafa hamoi ba: i. Gadofo damui da fa: no ba: i. Amaiba: le dunu huluane Gode Ea hou dafawaneyale dawa: beba: le gadofo damui amola gadofo hame damui, amo Gode da moloidafa hamoi ba: sa. Amola amo huluane da A: ibalaha: me ea mano agoane.
12 Ndipo iyenso ndiyenso kholo la ochita mdulidwe osati amene anangochita mdulidwe kokha koma amene amatsata chitsanzo cha chikhulupiriro chimene kholo lathu Abrahamu anali nacho asanachite mdulidwe.
Gadofo damui dunu amola ilia A: ibalaha: me ea dafawaneyale dawa: su hou e da ea gadofo hame damui amo esoga hamosu, amo defele ilia hamobeba: le, ilia amola da A: ibalaha: me ea mano agoane.
13 Abrahamu ndi zidzukulu zake sanalandire lonjezano lakuti adzalandira dziko lapansi kudzera mu Malamulo, koma kudzera mu chilungamo chimene chimabwera ndi chikhulupiriro.
Gode da A: ibalaha: mema, e amola egaga fi da hobea osobo bagade huluane lalegagumu sia: i. A: ibalaha: me da sema huluane mae giadofale hamoiba: le, Gode da amo hame sia: i. Be A: ibalaha: me da Gode dafawaneyale dawa: le, moloidafa hamoiba: le, Gode da ema amane sia: i.
14 Pakuti ngati amene amadalira Malamulo ndiye olowa mʼmalo, ndiye kuti chikhulupiriro nʼchopanda pake ndipo lonjezano ndi lopanda phindu
Gode Ea hahawane dogolegele iasu da Sema nabasu dunu ilima fawane iaha ganiaba, osobo bagade dunu ilia dafawaneyale dawa: su hou da hamedei liligi agoai ba: la: loba, amola Gode Ea hahawane dogolegele iasu da hamedei liligi agoai ba: la: loba.
15 chifukwa Malamulo anabweretsa chilango. Ndipo kumene kulibe Malamulo kulibenso kuwalakwitsa.
Gode Ea Sema da dialebeba: le, amo wadela: beba: le, dunu ilia Gode Ea ougi se dabe iasu ba: mu. Be Sema da hame galea, Sema amoma hame nabasu hou amola da hame gala.
16 Motero, timalandira lonjezo mwachikhulupiriro. Laperekedwa mwachisomo kuti patsimikizidwe kuti lonjezolo liperekedwa kwa ana ndi zidzukulu zonse za Abrahamu, osati kwa iwo okha amene amatsatira Malamulo komanso kwa iwo amene ali ndi chikhulupiriro cha Abrahamu. Iye ndiye kholo la ife tonse.
Amaiba: le, hahawane dogolegele iasu hou bai, amo Gode da Ema dafawaneyale dawa: su hou amoga hamoi. Gode da A: ibalaha: me egaga fi huluane ilima hahawane dogolegele imunu sia: i. Sema nabasu dunu ilima fawane hame. Be nowa dunu e da A: ibalaha: me ea hou defele dafawaneyale dawa: sa, ilima amola. A: ibalaha: me da nini huluanema a: silibu ada agoane esala.
17 Monga kwalembedwa kuti, “Ine ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri.” Iye ndiye kholo lathu pamaso pa Mulungu, amene anamukhulupirira, Mulungu amene amapereka moyo kwa akufa ndipo amapereka moyo kwa zinthu zopanda moyo.
Gode Sia: da agoane dedei diala, “Na da di fifi asi gala bagohame ilima ada hamoi dagoi.” Gode da bogoi uhinisimusa: dawa: Ea sia: beba: le, musa: hamedafa gala liligi da hamosa. A: ibalaha: me da amo Gode dafawaneyale dawa: i. Amola Gode da amo musa: ilegele sia: i hahawane dogolegele iasu liligi hamoi dagoi.
18 Ngakhale zinali zosayembekezeka, Abrahamu anakhulupirira ndi chiyembekezo kuti adzakhala kholo la mitundu yambiri. Izi ndi monga zinanenedwa kwa iye kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”
Osobo bagade dunu ilia hou ganodini, Gode Ea hahawane dogolegele iasu amo misa: ne hamoma: beyale da bai hame gala. Be A: ibalaha: me da gasawane dafawaneyale dawa: beba: le, dunu fi bagohame da ea mano agoane hamosu. Gode Sia: dedei amo, “Dia fi dunu lalelegemu da gasumuni idi defele agoane ba: mu.” - amo da dafawane ba: sa.
19 Iye sanafowoke mʼchikhulupiriro. Anadziwa choonadi cha thupi lake kuti linali lakufa popeza anali ndi zaka pafupifupi 100 ndiponso mimba ya Sara inali yowuma.
A: ibalaha: me da lalelegele, ea esalebe ode idi da gadenene 100 gidigi. Be ea da: i hodo da bogomu gadenei, amola ea uda Sela da mano lamu hamedei, amo mae dawa: le, e da ea dafawaneyale dawa: su hou hame yolesi.
20 Komabe iye sanagwedezeke chifukwa chosakhulupirira pa zokhudzana ndi lonjezo la Mulungu. Iye analimbikitsidwa mʼchikhulupiriro chake ndi kupereka ulemerero kwa Mulungu.
A: ibalaha: me da Gode Ea hahawane dogolegele imunu sia: i dafawaneyale dawa: i galu. Dafawaneyale dawa: beba: le, e da gasawane hamone, Godema nodoi.
21 Anatsimikiza mu mtima mwake kuti Mulungu anali ndi mphamvu yochita chomwe analonjeza.
A: ibalaha: me da Gode da Ea musa: ilegele sia: i dafawane hamomu, amo dafawaneyale dawa: i.
22 Nʼchifukwa chake “chinamuchititsa kukhala wolungama.”
Amaiba: le, A:ibalaha: me da Gode Ea hou dafawaneyale dawa: beba: le, “afadenei bu moloidafa hamoi,” Gode da e ba: i dagoi.
23 Mawu akuti, “chinatengedwa kwa iye” sanalembedwe chifukwa cha iye yekha,
Amo sia: , “afadenei bu moloidafa hamoi,” da A: ibalaha: me fawane ea hou olelema: ne hame dedei
24 komanso chifukwa ife amene Mulungu adzatiyesa olungama, ife amene tikhulupirira mwa Iye amene anamuukitsa kwa akufa, Yesu Ambuye athu.
Be ninia amola ninia hou olelema: ne dedei. Gode da Hina Yesu Gelesu bogoi amo wa: legadolesiba: le, amo ninia dafawaneyale dawa: sea, Gode da nini amola “afadenei bu moloidafa hamoi” ba: mu.
25 Iye anaperekedwa kuti aphedwe chifukwa cha machimo athu ndipo anaukitsidwa ndi kukhala ndi moyo kuti tilungamitsidwe.
Ninia wadela: i hou gogolema: ne olofomusa: , Gode da Yesu Gelesu osobo bagade dunu medole legemusa: , ilima i. Amola Gode da ninia huluane afadenene bu moloidafa hamoi ba: musa: , E da Yesu Gelesu uhini wa: legadolesi.

< Aroma 4 >