< Aroma 3 >
1 Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe?
Přece však má židovský národ zvláštní postavení a určité výsady. Jaké? Není jich málo!
2 Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.
Předně jim byla svěřena Boží slova.
3 Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu?
A co když jim někteří neuvěřili – můžete namítnout. A já se ptám: Myslíte, že Bůh jen pro jejich nedůvěru nedostojí svému slovu?
4 Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti, “Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi kupambana pamene muweruza.”
Ale kdepak! Právě na tom ukáže, jak dovede být věrný i tehdy, když mu člověk nevěří. Tak to stojí i v Písmu: „Každý uzná, že čestně dodržíš to, co jsi slíbil, a jako vítěz vyjdeš z každého obvinění.“
5 Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira).
Někdo však může namítnout: „Jestliže naše špatnost dává vyniknout Boží spravedlnosti, snad by nás Bůh neměl za ni trestat.“
6 Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi?
Jaký smysl by potom měl Boží soud?
7 Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?”
To bychom mohli rovnou nabádat ke zlu, aby se dobro vedle něj tím víc zaskvělo.
8 Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.
Někteří lidé to opravdu dělají, ale my ne, i když nás z toho obviňují. Takoví hříšníci budou plným právem odsouzeni.
9 Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa.
Napsal jsem vám již, že židovský národ má určité přednosti. To však neznamená, že židé jsou před Bohem lepší než ostatní. O všech lidech je v Žalmech napsáno:
10 Monga kwalembedwa kuti, “Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.
„Nikdo na světě není spravedlivý, ani jediný.
11 Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira, palibe amene amafunafuna Mulungu.
Nikdo není moudrý, nikdo Boha nehledá.
12 Onse apatukira kumbali, onse pamodzi asanduka opandapake. Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino, palibe ngakhale mmodzi.”
Všichni úplně zabloudili, jejich život ztratil smysl. Opuštěná je cesta dobra, nikdo po ní nekráčí.
13 “Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.” “Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”
Jejich hrdlo – otevřený hrob; jazyk – nástroj lsti a podvodu; rty – schránky jedu, uštknou tě jako had.
14 “Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”
15 “Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.
K prolití krve je nemusíš pobízet,
16 Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,
zkáza a bída jsou jejich průvodci,
17 ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”
cestu k pokoji však neznají,
18 “Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”
ani úctu před Bohem.“
19 Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu.
Víme však, že ustanovení zákona jsou závazná pro všechny, kterým byla určena. Každý tu musí uznat, že před Bohem je vinen,
20 Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.
neboť sebeupřímnější snahou dodržovat zákon si nikdo před Bohem nedobude postavení bezúhonného; zákon naši vinu pouze blíže určuje a usvědčuje nás z ní.
21 Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni.
Dnes však už známe jinou cestu k věčnému životu než spoléhání se na vlastní dodržování Božích zákonů. Už Mojžíš a proroci o ní mluvili,
22 Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina,
ale teprve Kristem ji Bůh otevřel. On sám, jak odpovídá jeho povaze, rozhodl se dát novou příležitost lidem, kteří svými vinami ztratili podíl na Boží slávě: odevzdat život do všech důsledků Kristu.
23 pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu
24 ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola.
Jaká to milost, že nic jiného není člověku zapotřebí. Kristus – toť svrchovaný důkaz Boží shovívavosti k nám.
25 Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale.
Jeho krev prolitá na popravišti je pečetí smíření Boha se světem. Až dosud Bůh trest za naše viny pouze s nekonečnou trpělivostí odkládal; nyní je však vložil na Ježíše Krista, který pro ně zemřel. A tak jsou nám definitivně odpuštěny; odpuštěny všem, kdo tuto Boží nabídku smíření přijali. Tak Bůh z hříšných dělá opět bezúhonné, aniž sám cokoliv slevuje ze své spravedlnosti.
26 Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.
27 Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro.
Čím se tedy můžeme před Bohem chlubit? Ničím! Skutky? Ty nás nespasí. Jedině víra nás může zachránit.
28 Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo.
Jsem přesvědčen, že nikoliv úzkostlivé dodržování všech přikázání a předpisů, ale pouze víra nás uschopní obstát před Bohem.
29 Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso,
Což je tu Bůh jen pro členy církve? Není snad Bohem všech lidí? To se rozumí, že je!
30 popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho.
Bůh je pouze jeden a bez rozdílu přijímá všechny, kdo se obrátí ke Kristu.
31 Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.
Neprohlašujeme snad zákon za bezcenný tím, že stavíme víru tak vysoko? Rozhodně ne! Naopak, platnost zákona se tím jen potvrzuje.