< Aroma 2 >
1 Choncho, iwe amene umaweruza munthu wina, ulibe pokanira pakuti nthawi iliyonse pamene uweruza wina ukudzitsutsa wekha chifukwa iwe amene umaweruzawe umachitanso zinthu zomwezo.
Ось тому без виправдання ти, кожний чоловіче, що судиш, бо в чо́му осуджуєш іншого, сам себе осуджуєш, бо чиниш те саме й ти, що судиш.
2 Tsopano ife tikudziwa kuti chiweruzo cha Mulungu, chotsutsa amene amachita zinthu zotere, nʼchokhazikika pa choonadi.
А ми знаємо, що суд Божий поправді на тих, хто чинить таке.
3 Kodi ukuganiza kuti udzathawa chiweruzo cha Mulungu iwe munthu wamba, pamene uweruza ena, iwe ndi kumachitanso zomwezo?
Чи ти ду́маєш, чоловіче, судячи тих, хто чинить таке, а сам робиш таке саме, — що ти втечеш від суду Божого?
4 Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa Mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirira kwake? Kodi sukuzindikira kuti kukoma mtima kwakeko, nʼkofuna kuti iweyo ulape machimo ako?
Або пого́рджуєш багатством Його до́брости, ла́гідности та довготерпіння, не знаючи, що Божа до́брість провадить тебе до покая́ння?
5 Koma pakuti ndiwe wosamvera ndi wa mtima wosafuna kulapa, ukudzisungira chilango pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu, pamene chiweruzo cholungama cha Mulungu chidzaonetsedwa.
Та через жорстокість свою й нерозкаяність серця збираєш собі гнів на день гніву та об'я́влення справедливого суду Бога,
6 Mulungu adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake.
що „кожному віддасть за його вчинками“:
7 Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. (aiōnios )
тим, хто витривалістю в добрім ділі шукає слави, і чести, і нетління, — життя вічне, (aiōnios )
8 Koma Mulungu adzakhuthulira mkwiyo ndi ukali wake pa amene amachita zofuna zawo ndi kukana choonadi nʼkumatsatira zoyipa.
а сварливим та тим, хто противиться правді, але кориться неправді, — лютість та гнів.
9 Masautso ndi zowawa zidzagwera munthu aliyense amene amachita zonyansa, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
Недоля та у́тиск на всяку душу людини, хто чинить зле, юдея ж перше та ге́ллена,
10 Koma ulemerero, ulemu ndi mtendere zidzakhala kwa aliyense amene amachita zabwino, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
а слава, і честь, і мир усякому, хто чинить добре, юдеєві ж перше та ге́лленові.
11 Pajatu Mulungu alibe tsankho.
Бо не дивиться Бог на обличчя!
12 Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo.
Котрі бо згрішили без Зако́ну, без Зако́ну й загинуть, а котрі згрішили в Зако́ні, при́ймуть суд за Зако́ном.
13 Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama.
Бо не слухачі Зако́ну справедливі перед Богом, але виконавці Закону ви́правдані бу́дуть.
14 Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo.
Бо коли погани, що не мають Зако́ну, з природи чинять зако́нне, вони, не мавши Зако́ну, самі собі Зако́н,
15 Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza.
що виявляють ді́ло Зако́ну, написане в серця́х своїх, як свідчить їм сумлі́ння та їхні думки́, що то осуджують, то виправдують одна о́дну,
16 Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.
дня, коли Бог, згідно з моїм благові́стям, буде судити таємні речі людей через Ісуса Христа.
17 Koma iweyo, amene umadzitcha kuti ndiwe Myuda, umadalira Malamulo, ndipo umanyadira ubale wako ndi Mulungu,
Ось ти звешся юдеєм, і спираєшся на Зако́на, і хвалишся Богом,
18 ngati umadziwa chifuniro chake, ndi kudziwa zoyenera kuchita chifukwa unaphunzitsidwa ndi Malamulo;
і знаєш волю Його, і розумієш, що́ краще, навчившись із Зако́ну,
19 ngati umadziwadi kuti ndiwe mtsogoleri wa osaona, nyale yowunikira amene ali mu mdima,
і маєш певність, що ти провідни́к для сліпих, світло для тих, хто знахо́диться в те́мряві,
20 mlangizi wa anthu opusa, mphunzitsi wa makanda, chifukwa umadziwa kuti mʼMalamulo uli nayo nzeru yonse ndi choonadi,
вихо́вник нерозумним, учитель дітям, що ти маєш зразок знання́ й правди в Зако́ні.
21 tsono, iwe amene umaphunzitsa ena, sudziphunzitsa wekha kodi? Kodi iwe amene umalalikira kuti anthu asabe, umabanso?
Отож, ти, що іншого навчаєш, себе самого не вчиш! Проповідуєш не кра́сти, а сам кра́деш!
22 Kodi iwe amene umanena kuti anthu asachite chigololo, umachitanso chigololo? Kodi iwe amene umanyasidwa ndi mafano, umalandanso za mʼnyumba zopembedzera mafanowo?
Наказуючи не чинити пере́любу, чиниш пере́люб! Гиду́ючи і́долами, чиниш святокрадство!
23 Kodi iwe amene umadzitama ndi Malamulo, umamuchititsa manyazi Mulungu posamvera Malamulowo?
Ти, що хва́лишся Зако́ном, зневажаєш Бога пере́ступом Зако́ну!
24 Monga kwalembedwa, “Dzina la Mulungu likuchitidwa chipongwe pakati pa a mitundu ina chifukwa cha inu.”
Бо „через вас зневажається Боже Ймення в поган“, як написано.
25 Mdulidwe umakhala ndi phindu ngati usunga Malamulo, koma ngati sumvera Malamulo, iweyo umakhala ngati kuti sunachite mdulidwe.
Обрі́зання кори́сне, коли виконуєш Зако́на; а коли ти пересту́пник Зако́ну, то обрі́зання твоє стало необрі́занням.
26 Ngati amene sanachite mdulidwe achita zomwe zili mʼMalamulo, kodi sadzatengedwa ngati ochita mdulidwe?
Отож, коли необрізаний зберігає постанови Зако́ну, то чи не порахується його необрізання за обрізання?
27 Munthu amene sanachite mdulidwe mʼthupi koma amamvera Malamulo adzakutsutsa iwe wosamvera Malamulowe, ngakhale kuti uli nawo Malamulo olembedwawo.
І необрізаний з природи, виконуючи Зако́на, чи не осудить тебе, переступника Закону з Писа́нням і обрі́занням?
28 Myuda weniweni si amene angooneka ngati Myuda pamaso pa anthu, ndipo mdulidwe weniweni si umene umangochitika mʼthupi pamaso pa anthu.
Бо не той юдей, що є ним назовні, і не то обрізання, що назовні на тілі,
29 Ayi, Myuda weniweni ndi amene ali Myuda mu mtima mwake, ndipo mdulidwe weniweni ndi wa mtima, wochitika ndi Mzimu, osati ndi malamulo olembedwa. Woyamikira munthu wotere ndi Mulungu, osati anthu ayi.
але той, що є юдей потаємно, духо́во, і обрі́зання — серця духом, а не за буквою; і йому похвала́ не від людей, а від Бога.