< Aroma 2 >

1 Choncho, iwe amene umaweruza munthu wina, ulibe pokanira pakuti nthawi iliyonse pamene uweruza wina ukudzitsutsa wekha chifukwa iwe amene umaweruzawe umachitanso zinthu zomwezo.
Wherefore thou art inexcusable, O man, whosoever thou art that judgest. For wherein thou judgest another, thou condemnest thyself. For thou dost the same things which thou judgest.
2 Tsopano ife tikudziwa kuti chiweruzo cha Mulungu, chotsutsa amene amachita zinthu zotere, nʼchokhazikika pa choonadi.
For we know that the judgment of God is, according to truth, against them that do such things.
3 Kodi ukuganiza kuti udzathawa chiweruzo cha Mulungu iwe munthu wamba, pamene uweruza ena, iwe ndi kumachitanso zomwezo?
And thinkest thou this, O man, that judgest them who do such things, and dost the same, that thou shalt escape the judgment of God?
4 Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa Mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirira kwake? Kodi sukuzindikira kuti kukoma mtima kwakeko, nʼkofuna kuti iweyo ulape machimo ako?
Or despisest thou the riches of his goodness, and patience, and longsuffering? Knowest thou not, that the benignity of God leadeth thee to penance?
5 Koma pakuti ndiwe wosamvera ndi wa mtima wosafuna kulapa, ukudzisungira chilango pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu, pamene chiweruzo cholungama cha Mulungu chidzaonetsedwa.
But according to thy hardness and impenitent heart, thou treasurest up to thyself wrath, against the day of wrath, and revelation of the just judgment of God.
6 Mulungu adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake.
Who will render to every man according to his works.
7 Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. (aiōnios g166)
To them indeed, who according to patience in good work, seek glory and honour and incorruption, eternal life: (aiōnios g166)
8 Koma Mulungu adzakhuthulira mkwiyo ndi ukali wake pa amene amachita zofuna zawo ndi kukana choonadi nʼkumatsatira zoyipa.
But to them that are contentious, and who obey not the truth, but give credit to iniquity, wrath and indignation.
9 Masautso ndi zowawa zidzagwera munthu aliyense amene amachita zonyansa, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
Tribulation and anguish upon every soul of man that worketh evil, of the Jew first, and also of the Greek.
10 Koma ulemerero, ulemu ndi mtendere zidzakhala kwa aliyense amene amachita zabwino, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
But glory, and honour, and peace to every one that worketh good, to the Jew first, and also to the Greek.
11 Pajatu Mulungu alibe tsankho.
For there is no respect of persons with God.
12 Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo.
For whosoever have sinned without the law, shall perish without the law; and whosoever have sinned in the law, shall be judged by the law.
13 Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama.
For not the hearers of the law are just before God, but the doers of the law shall be justified.
14 Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo.
For when the Gentiles, who have not the law, do by nature those things that are of the law; these having not the law are a law to themselves:
15 Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza.
Who shew the work of the law written in their hearts, their conscience bearing witness to them, and their thoughts between themselves accusing, or also defending one another,
16 Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.
In the day when God shall judge the secrets of men by Jesus Christ, according to my gospel.
17 Koma iweyo, amene umadzitcha kuti ndiwe Myuda, umadalira Malamulo, ndipo umanyadira ubale wako ndi Mulungu,
But if thou art called a Jew and restest in the law, and makest thy boast of God,
18 ngati umadziwa chifuniro chake, ndi kudziwa zoyenera kuchita chifukwa unaphunzitsidwa ndi Malamulo;
And knowest his will, and approvest the more profitable things, being instructed by the law,
19 ngati umadziwadi kuti ndiwe mtsogoleri wa osaona, nyale yowunikira amene ali mu mdima,
Art confident that thou thyself art a guide of the blind, a light of them that are in darkness,
20 mlangizi wa anthu opusa, mphunzitsi wa makanda, chifukwa umadziwa kuti mʼMalamulo uli nayo nzeru yonse ndi choonadi,
An instructor of the foolish, a teacher of infants, having the form of knowledge and of truth in the law.
21 tsono, iwe amene umaphunzitsa ena, sudziphunzitsa wekha kodi? Kodi iwe amene umalalikira kuti anthu asabe, umabanso?
Thou therefore that teachest another, teachest not thyself: thou that preachest that men should not steal, stealest:
22 Kodi iwe amene umanena kuti anthu asachite chigololo, umachitanso chigololo? Kodi iwe amene umanyasidwa ndi mafano, umalandanso za mʼnyumba zopembedzera mafanowo?
Thou that sayest, men should not commit adultery, committest adultery: thou that abhorrest idols, committest sacrilege:
23 Kodi iwe amene umadzitama ndi Malamulo, umamuchititsa manyazi Mulungu posamvera Malamulowo?
Thou that makest thy boast of the law, by transgression of the law dishonourest God.
24 Monga kwalembedwa, “Dzina la Mulungu likuchitidwa chipongwe pakati pa a mitundu ina chifukwa cha inu.”
(For the name of God through you is blasphemed among the Gentiles, as it is written.)
25 Mdulidwe umakhala ndi phindu ngati usunga Malamulo, koma ngati sumvera Malamulo, iweyo umakhala ngati kuti sunachite mdulidwe.
Circumcision profiteth indeed, if thou keep the law; but if thou be a transgressor of the law, thy circumcision is made uncircumcision.
26 Ngati amene sanachite mdulidwe achita zomwe zili mʼMalamulo, kodi sadzatengedwa ngati ochita mdulidwe?
If, then, the uncircumcised keep the justices of the law, shall not this uncircumcision be counted for circumcision?
27 Munthu amene sanachite mdulidwe mʼthupi koma amamvera Malamulo adzakutsutsa iwe wosamvera Malamulowe, ngakhale kuti uli nawo Malamulo olembedwawo.
And shall not that which by nature is uncircumcision, if it fulfill the law, judge thee, who by the letter and circumcision art a transgressor of the law?
28 Myuda weniweni si amene angooneka ngati Myuda pamaso pa anthu, ndipo mdulidwe weniweni si umene umangochitika mʼthupi pamaso pa anthu.
For it is not he is a Jew, who is so outwardly; nor is that circumcision which is outwardly in the flesh:
29 Ayi, Myuda weniweni ndi amene ali Myuda mu mtima mwake, ndipo mdulidwe weniweni ndi wa mtima, wochitika ndi Mzimu, osati ndi malamulo olembedwa. Woyamikira munthu wotere ndi Mulungu, osati anthu ayi.
But he is a Jew, that is one inwardly; and the circumcision is that of the heart, in the spirit, not in the letter; whose praise is not of men, but of God.

< Aroma 2 >