< Aroma 16 >

1 Ine ndikupereka kwa inu mlongo wathu Febe, mtumiki wa mpingo wa ku Kenkreya.
Doporučuji vám sestru Fébu, obětavou služebnici Kenchrejského křesťanského sboru. Ochotně pomáhala mně i jiným.
2 Ine ndikukupemphani kuti mumulandire mwa Ambuye mʼnjira yoyenera oyera mtima ndi kumupatsa thandizo lililonse limene akulifuna kuchokera kwa inu, pakuti iye wakhala thandizo lalikulu kwa anthu ambiri kuphatikiza ine.
Jestli se na vás obrátí, udělejte pro ni všechno, co budete moci, jak se na křesťany sluší.
3 Perekani moni kwa Prisila ndi Akura, atumiki anzanga mwa Khristu Yesu.
Pozdravujte Prisku a Akvilu, kteří pro mne v Kristových službách riskovali život; nejen já, ale všichni křesťané jsou jim za to dlužníky.
4 Iwo anapereka miyoyo yawo chifukwa cha ine. Osati ine ndekha komanso mipingo yonse ya a mitundu ina ikuyamika.
5 Perekaninso moni kwa mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwawo. Perekani moni kwa mʼbale wanga wokondedwa Epeneto, amene ndi woyamba kukhulupirira Khristu mʼchigawo cha Asiya.
Také všem věřícím, kteří se u nich scházejí, posílám srdečný pozdrav. Obzvlášť zdravím Epaineta, prvního asijského křesťana,
6 Perekani moni kwa Mariya, amene wakhala akukugwirirani ntchito kwambiri.
a Marii, která tolik pro vás udělala.
7 Perekani moni kwa Androniko ndi Yuniya abale anga amene anali mʼndende pamodzi ndi ine. Iwo amadziwika ndi atumwi, ndipo iwo anali mwa Khristu ine ndisanakhale.
Pozdravujte mé krajany a bývalé spoluvězně Andronika a Junia, vynikající muže mezi apoštoly, kteří se stali křesťany dříve než já.
8 Perekani moni kwa Ampliato, amene ine ndimamukonda mwa Ambuye.
Dále pozdravujte Ampliáta, Urbana, Stachyna a Apella. Také všechny od Aristobulů a Narcisů, Herodiona, Tryfainu, Tryfosu a Persidu. A ovšem Rufa a jeho matku – měla mě jako vlastního. A ještě Asynkrita, Flegonta, Herma, Patrobu, Hermeu a ostatní tamější bratry, Filologa, Julii, Nerea a jeho sestru, Olympa a všechny křesťany u nich. Pozdravte je ode mne bratrským polibkem. Taky ode všech křesťanských sborů a skupin vyřizuji pozdravy.
9 Perekani moni kwa Urbano, mtumiki mnzathu mwa Khristu ndi wokondedwa wanga Staku.
10 Perekani moni kwa Apele, woyesedwa ndi wovomerezeka mwa Khristu. Perekani moni kwa a mʼbanja la Aristobulo.
11 Perekani moni kwa Herodiona, mʼbale wanga. Perekani moni kwa a mʼbanja la Narkiso amene ali mwa Ambuye.
12 Perekani moni kwa Trufena ndi Trufosa, amayi aja amene amagwira ntchito ya Ambuye molimbika. Perekani moni kwa mnzanga wokondedwa Persida, mayi winanso amene wagwira ntchito kwambiri mwa Ambuye.
13 Perekani moni kwa Rufo, wosankhidwa mwa Ambuye, ndi amayi ake, amene akhala amayi anganso.
14 Perekani moni kwa Asunkrito, Felego, Herima, Patroba, Herima ndi abale amene ali nawo pamodzi.
15 Perekani moni kwa Filologo, Yuliya, Neriya ndi mlongo wake, ndi Olumpa ndi oyera mtima onse amene ali nawo pamodzi.
16 Mupatsane moni wina ndi mnzake mwachikondi choona. Mipingo yonse ya Khristu ikupereka moni.
17 Abale, ine ndikukupemphani kuti musamale chifukwa cha amene ayambitsa mipatuko ndi kuyika zokhumudwitsa panjira yanu, motsutsana ndi chiphunzitso chimene mwachiphunzira. Muwapewe iwo.
Jedno bych vám ještě rád položil na srdce: dejte si pozor na ty, kdo vyvolávají spory a svádějí vás z cesty, kterou jste nastoupili.
18 Pakuti otero sakutumikira Ambuye athu Khristu koma zilakolako zawo. Ndi mawu okoma ndi oshashalika iwo amanamiza anthu osalakwa.
Takoví kážou ne proto, aby sloužili Kristu, ale pro svůj vlastní prospěch. Vyhýbejte se jim. Bezelstného člověka snadno zmatou líbivými řečmi.
19 Aliyense anamva za kumvera kwanu, choncho ndine odzaza ndi chimwemwe chifukwa cha inu. Koma ine ndikufuna kuti inu mukhale anzeru pa zabwino, ndi wopanda cholakwa pa zimene zili zoyipa.
O vaší víře všude slyším jen to nejlepší a mám z toho radost. Přeji vám moudrost v konání dobra a zlo ať se vás ani nedotkne.
20 Mulungu wamtendere adzaphwanya Satana msanga pansi pa mapazi anu. Chisomo cha Ambuye athu Yesu chikhale ndi inu.
Bůh, dárce pokoje, už brzo rozdrtí satana u vašich nohou. Náš Pán Ježíš Kristus ať vás obdaří svou milostí.
21 Timoteyo, mtumiki mnzanga, akupereka moni. Nawonso, Lusio, Yasoni ndi Sosipatro, abale anga akutero.
Pozdravuje vás můj spolupracovník Timoteus a přátelé Lucius, Jáson a Sozipater.
22 Ine Tertio, amene ndalemba kalatayi, ndi kupereka moni mwa Ambuye.
I já, písař tohoto listu, Tercius, připojuji svůj pozdrav.
23 Gayo, amene chifukwa cha chisamaliro chake, ine ndi mpingo wonse kuno tikusangalala, akupereka moni. Erasto, amene ndi msungichuma wa mzinda wonse ndiponso mʼbale wathu Kwato, akupereka moni.
Také Gaius, náš hostitel, vás pozdravuje a rovněž vás zdraví správce městské pokladny Erastus a bratr Kvartus.
24 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse. Ameni.
25 Tsopano kwa Iye amene ali ndi mphamvu yokhazikitsa monga mwa uthenga wanga wabwino ndikulalikidwa kwa Yesu Khristu, monga mwa vumbulutso lachinsinsi chobisika kwa nthawi yayitali, (aiōnios g166)
Bůh vám může dát schopnost žít podle slov, která jsem vám zvěstoval. Byly vám zjeveny jeho dávné plány, dlouho skryté, (aiōnios g166)
26 koma tsopano chavumbulutsidwa ndi kudziwika kudzera mʼMalemba a uneneri mwa lamulo la Mulungu wosatha, kuti mitundu yonse ikhulupirire ndi kumvera Iye, (aiōnios g166)
ale nyní objasněné proroctvími, abyste je vírou poslušně přijali a podle nich žili. (aiōnios g166)
27 kwa Mulungu yekhayo wanzeru kukhale ulemerero kwamuyaya kudzera mwa Yesu Khristu! Ameni. (aiōn g165)
Nade vše moudrému Bohu věčná sláva za Ježíše Krista. Váš Pavel (aiōn g165)

< Aroma 16 >