< Aroma 13 >

1 Aliyense ayenera kumvera akulu olamulira, chifukwa palibe ulamuliro umene sunachokere kwa Mulungu. Olamulira amene alipo anayikidwa ndi Mulungu.
Let every individual be obedient to those who rule over him; for no one is a ruler except by God's permission, and our present rulers have had their rank and power assigned to them by Him.
2 Kotero kuti, iwo amene awukira ulamuliro atsutsana ndi chimene Mulungu anakhazikitsa. Ndipo amene atero adzibweretsera okha chilango.
Therefore the man who rebels against his ruler is resisting God's will; and those who thus resist will bring punishment upon themselves.
3 Pakuti olamulira saopseza amene amachita zabwino koma amene amachita zoyipa. Kodi mukufuna kukhala osaopa olamulira? Tsono chitani zoyenera ndipo adzakuyamikirani.
For judges and magistrates are to be feared not by right-doers but by wrong-doers. You desire--do you not? --to have no reason to fear your ruler. Well, do the thing that is right, and then he will commend you.
4 Pakuti iyeyo ndi mtumiki wa Mulungu wokuchitirani zabwino. Koma ngati muchita zoyipa muchite mantha, pakuti iye ali ndi mphamvu zolangira. Iye ndi mtumiki wa Mulungu wobweretsa mkwiyo ndi kulanga onse ochita zoyipa.
For he is God's servant for your benefit. But if you do what is wrong, be afraid. He does not wear the sword to no purpose: he is God's servant--an administrator to inflict punishment upon evil-doers.
5 Nʼchifukwa chake ndi koyenera kugonjera olamulira, osati chifukwa choopa kulangidwa kokha komanso chifukwa cha chikumbumtima.
We must obey therefore, not only in order to escape punishment, but also for conscience' sake.
6 Ichi nʼchifukwa chakenso inu mumapereka msonkho. Pakuti olamulira ndi atumiki a Mulungu amene amapereka nthawi yawo yonse kulamulira.
Why, this is really the reason you pay taxes; for tax-gatherers are ministers of God, devoting their energies to this very work.
7 Mubwezereni aliyense amene munamukongola. Ngati inu muli ndi ngongole yamsonkho, perekani msonkho kwa oyenera kuwalipira. Ngati ndi kuopa perekeni kwa oyenera kuwaopa ndipo ngati ndi ulemu kwa oyenera ulemu.
Pay promptly to all men what is due to them: taxes to those to whom taxes are due, toll to those to whom toll is due, respect to those to whom respect is due, honour to those to whom honour is due.
8 Musakhale ndi ngongole ndi wina aliyense kupatula ngongole ya kukondana wina ndi mnzake. Pakuti amene amakonda munthu mnzake wakwaniritsa lamulo.
Owe nothing to any one except mutual love; for he who loves his fellow man has satisfied the demands of Law.
9 Malamulo awa: “Usachite chigololo,” “Usaphe,” “Usabe,” “Usasirire,” ndi malamulo ena onse amene alipo, akhazikika pa lamulo limodzi ili, “Konda mnansi wako monga iwe mwini.”
For the precepts, "Thou shalt not commit adultery," "Thou shalt do no murder," "Thou shalt not steal," "Thou shalt not covet," and all other precepts, are summed up in this one command, "Thou shalt love thy fellow man as much as thou lovest thyself."
10 Chikondi sichichitira mnzake zoyipa. Chifukwa chake chikondi ndicho chokwaniritsa lamulo.
Love avoids doing any wrong to one's fellow man, and is therefore complete obedience to Law.
11 Ndipo chitani ichi pozindikira nthawi ino. Nthawi yafika yoti inu mudzuke kutulo, chifukwa chipulumutso chathu chili pafupi tsopano kuposa pamene tinayamba kukhulupirira.
Carry out these injunctions because you know the critical period at which we are living, and that it is now high time, to rouse yourselves from sleep; for salvation is now nearer to us than when we first became believers.
12 Usiku watsala pafupifupi kutha. Kwatsala pangʼono kucha. Tiyeni tsono tichotse ntchito zamdima ndipo tivale chovala chakuwunika.
The night is far advanced, and day is about to dawn. We must therefore lay aside the deeds of darkness, and clothe ourselves with the armour of Light.
13 Tiyeni tikhale moyenera monga nthawi ya masana, osati mʼmagulu amadyerero, achiwerewere ndi kuledzera, mʼmadama ndi zonyansa komanso osati mʼmagawano ndi nsanje.
Living as we do in broad daylight, let us conduct ourselves becomingly, not indulging in revelry and drunkenness, nor in lust and debauchery, nor in quarrelling and jealousy.
14 Koma valani Ambuye Yesu Khristu ndipo musaganizire za momwe mungakwaniritsire zokhumba zachikhalidwe cha uchimo.
On the contrary, clothe yourselves with the Lord Jesus Christ, and make no provision for gratifying your earthly cravings.

< Aroma 13 >