< Aroma 12 >

1 Nʼchifukwa chake ine ndikukupemphani abale, mwa chifundo cha Mulungu, kuti mupereke matupi anu monga nsembe yamoyo, yopatulika ndi yokondweretsa Mulungu. Nsembeyi ndiye kupembedza kwanu kwa uzimu.
Proszę was tedy, bracia! przez litości Boże, abyście stawiali ciała wasze ofiarą żywą, świętą, przyjemną Bogu, to jest rozumną służbę waszę.
2 Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro. (aiōn g165)
A nie przypodobywajcie się temu światu, ale się przemieńcie przez odnowienie umysłu waszego na to, abyście doświadczyli, która jest wola Boża dobra, przyjemna i doskonała. (aiōn g165)
3 Chifukwa cha chisomo chopatsidwa kwa ine, ndinena kwa aliyense wa inu kuti musadziyenereze nokha kuposa mmene mulili. Koma mudziganizire nokha modzichepetsa, molingana ndi muyeso wa chikhulupiriro chimene Mulungu wakupatsani.
Albowiem powiadam przez łaskę, która mi jest dana, każdemu, co jest między wami, aby więcej o sobie nie rozumiał, niżeli potrzeba rozumieć; ale żeby o sobie rozumiał skromnie, tak jako komu Bóg udzielił miarę wiary.
4 Pakuti monga aliyense wa ife ali ndi thupi limodzi koma ziwalo zambiri, ziwalozi sizili ndi ntchito yofanana.
Albowiem jako w jednem ciele wiele członków mamy, ale wszystkie członki nie jednoż dzieło mają:
5 Momwemonso mwa Khristu ife amene tili ambiri tipanga thupi limodzi ndipo chiwalo chilichonse ndi cholumikizika ku chinzake.
Tak wiele nas jest jednem ciałem w Chrystusie, aleśmy z osobna jedni drugich członkami.
6 Ife tili ndi mphatso zosiyana, molingana ndi chisomo chopatsidwa kwa ife. Ngati mphatso ya munthu ndi kunenera, musiyeni ayigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chake.
Mając tedy różne dary według łaski, która nam jest dana; jeźli proroctwo, niech będzie według sznuru wiary;
7 Ngati ndi kutumikira, musiyeni atumikire. Ngati ndi kuphunzitsa, musiyeni aphunzitse.
Jeźli posługowanie, niech będzie w posługowaniu; jeźli kto naucza, niech trwa w nauczaniu;
8 Ngati ndi kulimbikitsa, musiyeni alimbikitse. Ngati ndi kupereka kuthandiza osowa, musiyeni apereke mowolowamanja. Ngati ndi utsogoleri, musiyeni alamulire mosamala. Ngati ndi kuonetsa chifundo, musiyeni achite mosangalala.
Jeźli kto napomina, w napominaniu; kto rozdaje, w szczerości; kto przełożony jest, w pilności; kto czyni miłosierdzie, niech czyni z ochotą.
9 Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino.
Miłość niech będzie nieobłudna; miejcie w obrzydliwości złe; imając się dobrego.
10 Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni.
Miłością braterską jedni ku drugim skłonni bądźcie, uczciwością jedni drugich uprzedzając.
11 Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye.
W pracy nie leniwi, duchem pałający, Panu służący;
12 Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero.
W nadziei się weselący, w ucisku cierpliwi, w modlitwie ustawiczni;
13 Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.
Potrzebom świętych udzielający, gościnności naśladujący.
14 Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere.
Dobrorzeczcie tym, którzy was prześladują; dobrorzeczcie, a nie przeklinajcie.
15 Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira.
Weselcie się z weselącymi, a płaczcie z płaczącymi.
16 Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.
Bądźcie między sobą jednomyślni, wysoko o sobie nie rozumiejąc, ale się do niskich nakłaniając.
17 Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense.
(Bracia!) nie bądźcie mądrymi sami u siebie; żadnemu złem za złe nie oddawajcie, obmyśliwając to, co jest uczciwego przed wszystkimi ludźmi.
18 Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere.
Jeźli można, ile z was jest, ze wszystkimi ludźmi pokój miejcie.
19 Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye.
Nie mścijcie się sami, najmilsi: ale dajcie miejsce gniewowi; albowiem napisano: Mnie pomsta, a Ja oddam, mówi Pan.
20 Koma, “Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya. Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa. Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”
Jeźli tedy łaknie nieprzyjaciel twój, nakarm go; jeźli pragnie, napój go: bo to czyniąc, węgle rozpalone zgarniesz na głowę jego.
21 Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.
Nie daj się zwyciężyć złemu, ale złe dobrem zwyciężaj.

< Aroma 12 >