< Aroma 12 >
1 Nʼchifukwa chake ine ndikukupemphani abale, mwa chifundo cha Mulungu, kuti mupereke matupi anu monga nsembe yamoyo, yopatulika ndi yokondweretsa Mulungu. Nsembeyi ndiye kupembedza kwanu kwa uzimu.
I plead with you therefore, brethren, by the compassionsof God, to present all your faculties to Him as a living and holy sacrifice acceptable to Him. This with you will be an act of reasonable worship.
2 Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro. (aiōn )
And do not follow the customs of the present age, but be transformed by the entire renewal of your minds, so that you may learn by experience what God's will is--that will which is good and beautiful and perfect. (aiōn )
3 Chifukwa cha chisomo chopatsidwa kwa ine, ndinena kwa aliyense wa inu kuti musadziyenereze nokha kuposa mmene mulili. Koma mudziganizire nokha modzichepetsa, molingana ndi muyeso wa chikhulupiriro chimene Mulungu wakupatsani.
For through the authority graciously given to me I warn every individual among you not to value himself unduly, but to cultivate sobriety of judgement in accordance with the amount of faith which God has allotted to each one.
4 Pakuti monga aliyense wa ife ali ndi thupi limodzi koma ziwalo zambiri, ziwalozi sizili ndi ntchito yofanana.
For just as there are in the one human body many parts, and these parts have not all the same function;
5 Momwemonso mwa Khristu ife amene tili ambiri tipanga thupi limodzi ndipo chiwalo chilichonse ndi cholumikizika ku chinzake.
so collectively we form one body in Christ, while individually we are linked to one another as its members.
6 Ife tili ndi mphatso zosiyana, molingana ndi chisomo chopatsidwa kwa ife. Ngati mphatso ya munthu ndi kunenera, musiyeni ayigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chake.
But since we have special gifts which differ in accordance with the diversified work graciously entrusted to us, if it is prophecy, let the prophet speak in exact proportion to his faith;
7 Ngati ndi kutumikira, musiyeni atumikire. Ngati ndi kuphunzitsa, musiyeni aphunzitse.
if it is the gift of administration, let the administrator exercise a sound judgement in his duties.
8 Ngati ndi kulimbikitsa, musiyeni alimbikitse. Ngati ndi kupereka kuthandiza osowa, musiyeni apereke mowolowamanja. Ngati ndi utsogoleri, musiyeni alamulire mosamala. Ngati ndi kuonetsa chifundo, musiyeni achite mosangalala.
The teacher must do the same in his teaching; and he who exhorts others, in his exhortation. He who gives should be liberal; he who is in authority should be energetic and alert; and he who succours the afflicted should do it cheerfully.
9 Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino.
Let your love be perfectly sincere. Regard with horror what is evil; cling to what is right.
10 Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni.
As for brotherly love, be affectionate to one another; in matters of worldly honour, yield to one another.
11 Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye.
Do not be indolent when zeal is required. Be thoroughly warm-hearted, the Lord's own servants,
12 Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero.
full of joyful hope, patient under persecution, earnest and persistent in prayer.
13 Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.
Relieve the necessities of God's people; always practise hospitality.
14 Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere.
Invoke blessings on your persecutors--blessings, not curses.
15 Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira.
Rejoice with those who rejoice; weep with those who weep.
16 Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.
Have full sympathy with one another. Do not give your mind to high things, but let humble ways content you. Do not be wise in your own conceits.
17 Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense.
Pay back to no man evil for evil. Take thought for what is right and seemly in every one's esteem.
18 Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere.
If you can, so far as it depends on you, live at peace with all the world.
19 Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye.
Do not be revengeful, my dear friends, but give way before anger; for it is written, "'Revenge belongs to Me: I will pay back,' says the Lord."
20 Koma, “Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya. Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa. Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”
On the contrary, therefore, if your enemy is hungry, give him food; if he is thirsty, quench his thirst. For by doing this you will be heaping burning coals upon his head.
21 Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.
Do not be overcome by evil, but overcome the evil with goodness.