< Aroma 12 >
1 Nʼchifukwa chake ine ndikukupemphani abale, mwa chifundo cha Mulungu, kuti mupereke matupi anu monga nsembe yamoyo, yopatulika ndi yokondweretsa Mulungu. Nsembeyi ndiye kupembedza kwanu kwa uzimu.
I entreat you therefore, brothers, by the mercies of God, to present your bodies to Him as a living sacrifice, holy and acceptable to God. This is your reasonable service of worship.
2 Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro. (aiōn )
And be not conformed to this world, but be transformed by the renewing of your minds, so that you may prove what is the good and acceptable and perfect will of God. (aiōn )
3 Chifukwa cha chisomo chopatsidwa kwa ine, ndinena kwa aliyense wa inu kuti musadziyenereze nokha kuposa mmene mulili. Koma mudziganizire nokha modzichepetsa, molingana ndi muyeso wa chikhulupiriro chimene Mulungu wakupatsani.
For, through the grace that was given to me, I tell every man among you not to think of himself more highly than he ought to think; but so to think, as to think soberly, according to the measure of faith which God has given him.
4 Pakuti monga aliyense wa ife ali ndi thupi limodzi koma ziwalo zambiri, ziwalozi sizili ndi ntchito yofanana.
For even as we have many members in one body, and not all members have the same function;
5 Momwemonso mwa Khristu ife amene tili ambiri tipanga thupi limodzi ndipo chiwalo chilichonse ndi cholumikizika ku chinzake.
so we, who are many, are one body in Christ, and we are severally members of one another.
6 Ife tili ndi mphatso zosiyana, molingana ndi chisomo chopatsidwa kwa ife. Ngati mphatso ya munthu ndi kunenera, musiyeni ayigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chake.
But we have gifts differing according to the grace which was given to us. He that has the gift of prophecy, let him prophesy according to the proportion of his faith.
7 Ngati ndi kutumikira, musiyeni atumikire. Ngati ndi kuphunzitsa, musiyeni aphunzitse.
If it is the gift of administration, let us give ourselves to our service.
8 Ngati ndi kulimbikitsa, musiyeni alimbikitse. Ngati ndi kupereka kuthandiza osowa, musiyeni apereke mowolowamanja. Ngati ndi utsogoleri, musiyeni alamulire mosamala. Ngati ndi kuonetsa chifundo, musiyeni achite mosangalala.
Let the teacher give himself to his teaching; and he who exhorts others to his exhortation. He who gives, let him do it in singleness of mind. He who rules, let him rule with diligence; and he who shows mercy must be cheerful.
9 Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino.
Let love be without insincerity. Abhor what is evil; wed yourselves to what is good.
10 Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni.
As for brotherly love, be tenderly affectionate one to another, in honor preferring one another.
11 Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye.
In your diligence be free from sloth. Be glowing in spirit. Slave for the master.
12 Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero.
Rejoice in hope; be patient under affliction; continue stedfast in prayer.
13 Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.
Be liberal to needy saints. Practise hospitality.
14 Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere.
Bless your persecutors, bless, and curse not.
15 Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira.
Rejoice with those who rejoice, and weep with those who weep.
16 Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.
Have full sympathy with one another. Set not your minds on high affairs, but associate with lowly folk. Do not be wise in your own conceits.
17 Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense.
Do not pay back evil for evil. Aim to do what is honorable in the eyes of all.
18 Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere.
If it be possible, so far as it lies with you, be at peace with all men.
19 Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye.
Never revenge yourself, beloved, but leave the field clear for God’s wrath; for it is written, "Vengeance is mine, I will repay," says the Lord.
20 Koma, “Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya. Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa. Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”
On the contrary, therefore, If your enemy is hungry, feed him; if he is thirsty, give him drink; for by so doing you will be heaping burning coals on his head.
21 Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.
Do not be overcome by evil, but be overcoming evil with good.