< Aroma 12 >

1 Nʼchifukwa chake ine ndikukupemphani abale, mwa chifundo cha Mulungu, kuti mupereke matupi anu monga nsembe yamoyo, yopatulika ndi yokondweretsa Mulungu. Nsembeyi ndiye kupembedza kwanu kwa uzimu.
I beseech you therefore, brethren, by the compassions of God, to present your bodies a living sacrifice, holy, acceptable to God, [which is] your intelligent service.
2 Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro. (aiōn g165)
And be not conformed to this world, but be transformed by the renewing of [your] mind, that ye may prove what [is] the good and acceptable and perfect will of God. (aiōn g165)
3 Chifukwa cha chisomo chopatsidwa kwa ine, ndinena kwa aliyense wa inu kuti musadziyenereze nokha kuposa mmene mulili. Koma mudziganizire nokha modzichepetsa, molingana ndi muyeso wa chikhulupiriro chimene Mulungu wakupatsani.
For I say, through the grace which has been given to me, to every one that is among you, not to have high thoughts above what he should think; but to think so as to be wise, as God has dealt to each a measure of faith.
4 Pakuti monga aliyense wa ife ali ndi thupi limodzi koma ziwalo zambiri, ziwalozi sizili ndi ntchito yofanana.
For, as in one body we have many members, but all the members have not the same office;
5 Momwemonso mwa Khristu ife amene tili ambiri tipanga thupi limodzi ndipo chiwalo chilichonse ndi cholumikizika ku chinzake.
thus we, [being] many, are one body in Christ, and each one members one of the other.
6 Ife tili ndi mphatso zosiyana, molingana ndi chisomo chopatsidwa kwa ife. Ngati mphatso ya munthu ndi kunenera, musiyeni ayigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chake.
But having different gifts, according to the grace which has been given to us, whether [it be] prophecy, [let us prophesy] according to the proportion of faith;
7 Ngati ndi kutumikira, musiyeni atumikire. Ngati ndi kuphunzitsa, musiyeni aphunzitse.
or service, [let us occupy ourselves] in service; or he that teaches, in teaching;
8 Ngati ndi kulimbikitsa, musiyeni alimbikitse. Ngati ndi kupereka kuthandiza osowa, musiyeni apereke mowolowamanja. Ngati ndi utsogoleri, musiyeni alamulire mosamala. Ngati ndi kuonetsa chifundo, musiyeni achite mosangalala.
or he that exhorts, in exhortation; he that gives, in simplicity; he that leads, with diligence; he that shews mercy, with cheerfulness.
9 Chikondi chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choyipa; gwiritsitsa chabwino.
Let love be unfeigned; abhorring evil; cleaving to good:
10 Mukondane kwathunthu monga abale. Lemekezanani wina ndi mnzake kuposa inu eni.
as to brotherly love, kindly affectioned towards one another: as to honour, each taking the lead in paying it to the other:
11 Musakhale aulesi mʼmachitidwe anu. Khalani achangu mu mzimu ndipo tumikirani Ambuye.
as to diligent zealousness, not slothful; in spirit fervent; serving the Lord.
12 Kondwerani mʼchiyembekezo, pirirani mʼmasautso ndiponso khulupirikani mʼpemphero.
As regards hope, rejoicing: as regards tribulation, enduring: as regards prayer, persevering:
13 Gawanani ndi anthu a Mulungu amene ali ndi chosowa. Cherezani alendo.
distributing to the necessities of the saints; given to hospitality.
14 Adalitseni amene akuzunzani. Adalitseni ndipo musawatemberere.
Bless them that persecute you; bless, and curse not.
15 Kondwani pamodzi ndi amene akukondwa ndipo lirani ndi amene akulira.
Rejoice with those that rejoice, weep with those that weep.
16 Muyanjane wina ndi mnzake. Musakhale onyada, koma lolani kuyanjana ndi anthu wamba. Musaganize kuti mumadziwa zonse.
Have the same respect one for another, not minding high things, but going along with the lowly: be not wise in your own eyes:
17 Musabwezere choyipa ndi choyipa kwa aliyense. Samalitsani kuchita chabwino pamaso pa aliyense.
recompensing to no one evil for evil: providing things honest before all men:
18 Ngati nʼkotheka, khalani mwamtendere ndi aliyense monga momwe mungathere.
if possible, as far as depends on you, living in peace with all men;
19 Okondedwa anga, musabwezere choyipa, koma lekerani Mulungu. Pakuti kwalembedwa, “Kubwezera chilango nʼkwanga. Ndidzawalanga ndine,” akutero Ambuye.
not avenging yourselves, beloved, but give place to wrath; for it is written, Vengeance [belongs] to me, I will recompense, saith the Lord.
20 Koma, “Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya. Ngati ali ndi ludzu, mupatse kanthu kakumwa. Pochita ichi, udzamuwunjikira makala amoto pamutu pake.”
If therefore thine enemy should hunger, feed him; if he should thirst, give him drink; for, so doing, thou shalt heap coals of fire upon his head.
21 Musagonjetsedwe ndi choyipa, koma gonjetsani choyipa pochita chabwino.
Be not overcome by evil, but overcome evil with good.

< Aroma 12 >