< Aroma 11 >

1 Ine ndikufunsa kuti kodi Mulungu anakana anthu ake? Ayi. Ndi pangʼono pomwe! Inenso ndine Mwisraeli, mmodzi mwa zidzukulu za Abrahamu, ndiponso wa fuko la Benjamini.
Ptám se tedy: Zavrhl snad Bůh svůj národ? Rozhodně ne! Vždyť já jsem také židovské národnosti, potomek Abrahamův z větve Benjamínovy.
2 Mulungu sanawakane anthu ake amene Iye anawadziwiratu. Kodi inu simukudziwa zimene Malemba akunena pa ndime imene Eliya akudandaula kwa Mulungu kuneneza Aisraeli? Iye anati,
Bůh nezavrhl svůj lid, který si předtím vybral. V Bibli se dočteme, že už Elijáš si Bohu na svůj národ stěžoval:
3 “Ambuye, anthuwa apha aneneri anu ndi kugwetsa maguwa anu ansembe. Ndatsala ine ndekha wamoyo ndipo akufuna kundipha?”
„Pane, tvé proroky povraždili, tvé oltáře rozbořili. Už jen já jsem zůstal při tobě a také mně o život ukládají.“
4 Ndipo yankho la Mulungu linali lotani? “Ine ndadzisungira ndekha anthu 7,000 amene sanapembedzepo Baala.”
A co mu na to odpovídá Bůh? „Sedm tisíc věrných – kromě tebe – se bohům cizím ještě neklaní!“
5 Chimodzimodzinso lero lino, alipo Aisraeli pangʼono osankhidwa mwachisomo.
Stejně tak dnes je tu takový zbytek věrných. Bůh je ovšem nevyvolil pro jejich zásluhy, nýbrž ze své milosti.
6 Ndipo ngati ndi mwachisomo, sikungakhalenso mwa ntchito. Ngati zikanatero, chisomo sichikanakhalanso chisomo ayi.
Tak tedy: o co se tolik snažili Izraelci, toho – kromě těch vyvolených – nedosáhli.
7 Nʼchiyani tsopano? Chimene Aisraeli anachifuna ndi mtima wonse sanachipeze koma osankhidwawo anachipeza. Enawo anawumitsidwa mtima
8 monga kwalembedwa kuti, “Mulungu anawapatsa mzimu wosatha kumvetsa zinthu, maso osatha kupenya; makutu osatha kumva mpaka lero lino.”
Bůh je ranil slepotou, takže mají oči – a přesto nevidí, mají uši – a přesto neslyší, slepí a hluší jsou až dodnes.
9 Ndipo Davide akuti, “Maphwando awo asanduke msampha ndi diwa lowakola ndi chopunthwitsa kuti alandire chilango.
A David říká v jednom svém žalmu: „Jejich blahobyt ať je jim osidlem a kamenem úrazu.
10 Maso awo atsekedwe kuti asaone, ndi misana yawo ikhale yokhota nthawi zonse.”
Zatmi jim zrak, ať nevidí a pod břemenem stále se hrbí.“
11 Ine ndikufunsanso kuti, kodi iwo anapunthwa ndi kugwa kotheratu? Ayi. Ndi pangʼono pomwe! Koma chifukwa cha kulakwa kwawo, chipulumutso chinafika kwa a mitundu ina kuti Aisraeli achite nsanje.
Ptám se tedy: Je snad smyslem jejich klopýtnutí, aby padli nadobro? V žádném případě!
12 Koma ngati kulakwa kwawo kwapindulitsa dziko lapansi ndi kulephera kwawo kwapindulitsa a mitundu ina, nanga kudzakhala kupindula kwakukulu chotani iwo akadzabwera chonse!
Jejich pád však umožnil záchranu pohanů, a to má probudit u židů zdravou žárlivost. Oč větším požehnáním pro svět bude návrat Izraele k Bohu, když jeho úpadek znamenal už takové dobrodiní!
13 Ine ndikuyankhula kwa inu a mitundu ina monga ine ndili mtumwi wa kwa a mitundu ina ndipo ndimawunyadira utumiki wangawu.
Proto vám, bývalým pohanům, sloužím tak horlivě,
14 Ine cholinga changa nʼchakuti ndichititse nsanje anthu a mtundu wanga kuti ena mwa iwo apulumutsidwe.
abych vyvolal žárlivost u svých soukmenovců a alespoň některé tak zachránil.
15 Pakuti ngati kukanidwa kwawo kunayanjanitsa anthu a dziko lapansi ndi Mulungu, nanga kudzatani, Iye akadzawalandiranso? Kudzakhala monga ngati anthu akufa akuuka.
To, že se ocitli v nepřátelském táboře, přineslo světu smíření s Bohem. A což teprve, až je Bůh znovu přijme! To bude přímo vzkříšení z mrtvých!
16 Ngati chigawo chimodzi cha buledi woperekedwa monga zipatso zoyamba ndi choyera, ndiye kuti zonsezo ndi zoyera. Ngati muzu ndi oyera, nʼchimodzimodzinso nthambi zake.
Co vyrostlo ze svatých kořenů, je rovněž svaté.
17 Ngati nthambi zina zinakhadzulidwa ndipo inu, inu ndiye nthambi za olivi wakuthengo, nʼkulumikizidwa pamalo pa nthambi zimenezo, ndipo tsopano mukulandira nawo zakudya zochokera ku mizu ya olivi,
Jestli byly některé větve ze svatého stromu ulomeny a vy, jako plané větve, naroubováni na jejich místo,
18 musadzitame kunyoza nthambi zinazo. Ngati mutero, ganizirani ichi kuti Inu simugwiriziza mizu, koma muzu ukugwiriziza inu.
nevypínejte se nad větve původní. Nezapomeňte, že kořen nese vás a ne naopak!
19 Tsono mudzati, “Nthambizo zinakhadzulidwa kuti ine ndilumikizidwepo.”
Říkáš: „Byly přece ulámány, abych já mohl zaujmout jejich místo.“
20 Nʼzoona. Koma iwo anakhadzulidwa chifukwa chosakhulupirira ndipo inu mukuyima mwachikhulupiriro. Musadzitukumule, koma muchite mantha.
Máš pravdu, byly ulámány kvůli své nevěře a ty rosteš na jejich místě díky své víře. To však měj za důvod spíš k pokoře než k domýšlivosti.
21 Pakuti ngati Mulungu sanalekerere nthambi zachibadwidwe, Iye sadzakulekererani inunso.
Když Bůh neušetřil větve původní, tím spíš by neušetřil tebe.
22 Nʼchifukwa chake ganizirani za kukoma mtima ndi za ukali wa Mulungu. Ukali uli kwa iwo amene anagwa koma kukoma mtima kwa inu, malinga ngati musamala kukoma mtima kwakeko kupanda kutero inunso mudzakhadzulidwanso.
Máš v tom vidět důkaz jeho přísnosti, ale zároveň i dobroty: přísnosti k odpadlým a dobroty k tobě – pokud ovšem zůstaneš věrný. Jinak odřízne i tebe.
23 Ngati iwo asiya kukhala osakhulupirira, adzalumikizidwanso pakuti Mulungu akhoza kuwalumikizanso.
A stejně i židé, vrátí-li se k Bohu, budou naroubováni zase zpět. Bude to tím snadnější, že Bůh je vlastně jen vrátí na jejich původní místo. Nemělo by vám zůstat tajemstvím, bratři, jaké úmysly má Bůh s Izraelem,
24 Pakuti ngati inu, mwa chilengedwe munali mtengo wa olivi wa kuthengo, Mulungu anakukhadzulani nakulumikizani ku mtengo wa olivi wodzalidwa, zomwe ndi zotsutsana ndi chilengedwe, kodi sikudzakhala kwapafupi kwa Iye kuwalumikizanso mu mtengo wawowawo wa olivi?
25 Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa za chinsinsi ichi, kuti mungadziyese nokha anzeru. Kuwuma mtima kumene Aisraeli akuchita ndi kwa kanthawi kufikira chiwerengero cha a mitundu chitalowa.
a nechci vás ponechat jen vašim představám. Část židů zůstane od Boha odvrácena tak dlouho, dokud počet povolaných z ostatních národů nebude dovršen. Když se to stane,
26 Kotero tsono Aisraeli onse adzapulumuka, monga kwalembedwa kuti, “Mpulumutsi adzachokera ku Ziyoni; Iye adzachotsa zoyipa zonse za Yakobo.
otevře se cesta všemu Izraeli a nalezne spasení, jak píše Izajáš: „Z Jeruzaléma přijde vysvoboditel a všechnu bezbožnost z národa vymýtí.
27 Ndipo ili lidzakhala pangano langa ndi iwo pamene Ine ndidzachotsa machimo awo.”
Já, Bůh, s nimi učiním smlouvu, že všechny jejich viny zahladím.“
28 Chifukwa cha Uthenga Wabwino, Aisraeli asanduka adani a Mulungu kuti inu mupindule. Koma kunena za kusankhidwa, iwo ndi okondedwa ndi Mulungu chifukwa cha makolo awo aja.
Jak se tedy máte na židy dívat? Nepřijali Pána Ježíše Krista, a proto je můžete pokládat za Boží odpůrce; přitom však nezapomínejte, že vás jejich vzdor přivedl k Božímu milosrdenství. Bůh je však stále miluje, protože jsou dětmi svých předků, které on vyvolil.
29 Pakuti Mulungu akayitana munthu ndi kumupatsa mphatso sangasinthenso.
Když Bůh něco daruje, nebere to zpět; když někoho povolá, sám to neruší.
30 Monga mmene inu munalili, osamvera Mulungu pa nthawi ina, tsopano mwalandira chifundo chifukwa cha kusamvera kwawo.
Vy jste kdysi Boha odmítali, ale teď se vám dostalo Božího milosrdenství, když ho židé odmítli.
31 Chonchonso iwo akhala osamvera tsopano kuti iwonso alandire chifundo chifukwa cha chifundo cha Mulungu kwa inu.
V podobné situaci jsou teď oni. Staví se odmítavě k milosti, která byla udělena vám právě proto, aby ji nakonec mohli dostat i oni.
32 Pakuti Mulungu anasandutsa anthu onse a mʼndende ya kusamvera kuti Iye akaonetse chifundo kwa onse. (eleēsē g1653)
Tak se všichni nerozdílně stali svou neposlušností stejně závislými na Boží milosti, jak Bůh chtěl. (eleēsē g1653)
33 Aa! Nzeru za Mulungu ndi chidziwitso chake ndi zozama kwambiri! Ndani angazindikire maweruzidwe ake, ndipo njira zake angazitulukire ndani?
Jak nesmírné je Boží bohatství, jak hluboká jeho moudrost a poznání. Jak nevyzpytatelná jeho rozhodnutí a nepředvídatelné jeho jednání!
34 “Kodi wadziwa ndani maganizo a Ambuye? Kapena ndani anakhalapo mlangizi wake?”
Kdo může pochopit Boží myšlení, kdo byl kdy jeho poradcem?
35 “Kodi ndani anapereka mphatso kwa Mulungu, kuti Mulunguyo amubwezere iye?”
Kdo mu kdy dal něco ze svého, aby mu to on musel vrátit?
36 Pakuti zinthu zonse nʼzochokera kwa Iye, nʼzolengedwa ndi Iye ndipo zimabweretsa ulemerero kwa Iye. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya! Ameni. (aiōn g165)
Vždyť z Boha vše pochází, díky jemu a pro něho vše trvá. Jemu sláva na věky! (aiōn g165)

< Aroma 11 >