< Chivumbulutso 9 >

1 Mngelo wachisanu anayimba lipenga lake, ndipo ndinaona nyenyezi ikugwa pa dziko lapansi kuchokera ku thambo. Nyenyeziyo inapatsidwa kiyi ya ku chidzenje chakuya. (Abyssos g12)
Le cinquième ange sonna de la trompette, et je vis du ciel une étoile qui était tombée sur la terre. La clé du puits de l'abîme lui fut donnée. (Abyssos g12)
2 Nyenyeziyo itatsekula pa chidzenje chakuyacho panatuluka utsi ngati wochokera mʼngʼanjo yayikulu. Dzuwa ndi thambo zinada chifukwa cha utsi ochokera mʼdzenjemo. (Abyssos g12)
Il ouvrit le puits de l'abîme, et de la fumée monta du puits, comme la fumée d'une fournaise ardente. Le soleil et l'air s'obscurcirent à cause de la fumée qui sortait du puits. (Abyssos g12)
3 Ndipo mʼkati mwa utsimo munatuluka dzombe kukalowa mʼdziko lapansi ndipo linapatsidwa mphamvu zoluma ngati za zinkhanira pa dziko lapansi.
Alors, de la fumée sortirent des sauterelles sur la terre, et un pouvoir leur fut donné, comme un pouvoir aux scorpions de la terre.
4 Dzombelo linalamulidwa kuti lisawononge udzu wa pa dziko lapansi, kapena chomera chilichonse, kapena mtengo uliwonse, koma anthu okhawo amene analibe chizindikiro cha Mulungu pa mphumi zawo.
On leur dit qu'elles ne devaient pas faire de mal à l'herbe de la terre, ni à aucune verdure, ni à aucun arbre, mais seulement aux personnes qui n'ont pas le sceau de Dieu sur le front.
5 Silinapatsidwe mphamvu yowapha koma yowazunza kwa miyezi isanu. Ndipo ululu umene anthuwo anawumva unali ngati wa chinkhanira chikaluma munthu.
Ils reçurent le pouvoir, non pas de les tuer, mais de les tourmenter pendant cinq mois. Leur tourment était semblable au tourment d'un scorpion quand il frappe une personne.
6 Masiku amenewo anthu adzafunafuna imfa koma sadzayipeza. Adzalakalaka kufa koma imfa izidzawathawa.
En ces jours-là, les gens chercheront la mort, et ils ne la trouveront pas. Ils désireront mourir, et la mort les fuira.
7 Dzombe linkaoneka ngati akavalo okonzekera nkhondo. Pamitu pawo panali ngati zipewa zaufumu zagolide ndipo nkhope zawo ngati za anthu.
Les sauterelles avaient la forme de chevaux préparés pour la guerre. Sur leurs têtes il y avait quelque chose comme des couronnes d'or, et leurs visages étaient comme des visages d'hommes.
8 Tsitsi lawo linali ngati la amayi, mano awo ngati a mikango.
Elles avaient des cheveux comme des cheveux de femme, et leurs dents étaient comme celles des lions.
9 Dzombelo linavala za pachifuwa zachitsulo. Phokoso la mapiko awo linali ngati phokoso la magaleta ankhondo ambiri okokedwa ndi akavalo othamangira ku nkhondo.
Ils avaient des cuirasses comme des cuirasses de fer. Le bruit de leurs ailes était comme le bruit de beaucoup de chars et de chevaux qui se précipitent à la guerre.
10 Linali ndi michira ngati zinkhanira ndi mbola. Mʼmichira yake munali mphamvu yozunza nayo anthu kwa miyezi isanu.
Ils avaient des queues semblables à celles des scorpions, avec des aiguillons. Dans leurs queues, ils ont le pouvoir de faire du mal aux hommes pendant cinq mois.
11 Mfumu yawo inali mngelo wolamulira Chidzenje chakuya chija. Mʼchihebri dzina lake ndi Abadoni ndipo mʼChigriki ndi Apoliyoni (tanthauzo lake ndiye kuti, Wowononga). (Abyssos g12)
Ils ont sur eux comme roi l'ange de l'abîme. Son nom en hébreu est « Abaddon », mais en grec, il porte le nom d' « Apollyon ». (Abyssos g12)
12 Tsoka loyamba lapita; matsoka ena awiri akubwerabe.
Le premier malheur est passé. Voici, il y a encore deux malheurs qui viennent après celui-ci.
13 Mngelo wachisanu ndi chimodzi anayimba lipenga lake, ndipo ndinamva liwu lochokera ku ngodya zinayi za guwa lansembe lagolide lija lokhala pamaso pa Mulungu.
Le sixième ange sonna de la trompette. Et j'entendis une voix venant des cornes de l'autel d'or qui est devant Dieu,
14 Liwulo linati kwa mngelo wachisanu ndi chimodzi amene anali ndi lipenga uja, “Masula angelo anayi amene anamangidwa pa mtsinje waukulu wa Yufurate.”
et disant au sixième ange qui avait la trompette: « Libérez les quatre anges qui sont liés au grand fleuve d'Euphrate! »
15 Ndipo anamasulidwadi angelo anayi aja amene anasungidwa kukonzekera ora ili, tsiku ili, mwezi uwu ndi chaka ichi kuti aphe limodzi la magawo atatu a anthu.
Les quatre anges furent libérés qui avaient été préparés pour cette heure, ce jour, ce mois et cette année, afin qu'ils tuent un tiers de l'humanité.
16 Ndinamva chiwerengero cha ankhondo a pa akavalo aja, kuti chinali 200 miliyoni.
Le nombre des armées des cavaliers était de deux cent millions. J'en entendis le nombre.
17 Akavalo ndi okwerapo amene ndinaona mʼmasomphenya anga ankaoneka motere: Zovala za pachifukwa pawo zinali zofiira ngati moto, zobiriwira ngati utsi, ndi zachikasu ngati miyala ya sulufule. Mitu ya akavalowo inali ngati ya mikango ndipo mʼkamwa mwawo munkatuluka moto, utsi ndi sulufule.
C'est ainsi que je vis dans la vision les chevaux et ceux qui les montaient, ayant des cuirasses d'un rouge ardent, d'un bleu d'hyacinthe et d'un jaune de soufre; et les têtes des chevaux ressemblaient à des têtes de lions. De leurs bouches sortent du feu, de la fumée et du soufre.
18 Gawo limodzi la magawo atatu a anthu linaphedwa ndi miliri yamoto, utsi ndi sulufule zimene zinkachoka mʼkamwa mwawo.
Par ces trois fléaux, un tiers du genre humain fut tué: par le feu, la fumée et le soufre, qui sortaient de leurs bouches.
19 Mphamvu za akavalowo inali mʼkamwa mwawo ndi mʼmichira mwawo; pakuti michira yawo inali ngati njoka; ndi mitu imene inkalumira.
Car la puissance des chevaux est dans leurs bouches et dans leurs queues. Car leurs queues sont comme des serpents, et elles ont des têtes; et c'est avec elles qu'ils font du mal.
20 Anthu ena onse amene sanaphedwe ndi miliri imeneyi sanalapebe kuti asiye ntchito zawo zoyipa. Iwo sanasiye kupembedza ziwanda ndi mafano agolide, asiliva, amkuwa, amwala ndi amtengo, mafano amene sangathe kuona, kumva kapena kuyankhula.
Le reste de l'humanité, qui n'a pas été tué par ces fléaux, ne s'est pas repenti des œuvres de ses mains pour ne pas adorer les démons et les idoles d'or, d'argent, d'airain, de pierre et de bois, qui ne peuvent ni voir, ni entendre, ni marcher.
21 Sanalapenso kuleka zakupha, zamatsenga awo, zachigololo zawo kapena umbava wawo.
Ils ne se sont pas repentis de leurs meurtres, de leurs enchantements, de leur immoralité sexuelle, ni de leurs vols.

< Chivumbulutso 9 >