< Chivumbulutso 9 >
1 Mngelo wachisanu anayimba lipenga lake, ndipo ndinaona nyenyezi ikugwa pa dziko lapansi kuchokera ku thambo. Nyenyeziyo inapatsidwa kiyi ya ku chidzenje chakuya. (Abyssos )
The fifth angel blew his trumpet. Then I saw [an evil angel. He was like] a star that had fallen from the sky to the earth. He was given {[Someone] gave him} the key to the shaft [that descended] ([to] the underworld/[to] the deep dark pit). (Abyssos )
2 Nyenyeziyo itatsekula pa chidzenje chakuyacho panatuluka utsi ngati wochokera mʼngʼanjo yayikulu. Dzuwa ndi thambo zinada chifukwa cha utsi ochokera mʼdzenjemo. (Abyssos )
When he opened that shaft, smoke arose from it like smoke from a huge burning furnace. The smoke prevented [anyone from seeing] the sky and the light of the sun. (Abyssos )
3 Ndipo mʼkati mwa utsimo munatuluka dzombe kukalowa mʼdziko lapansi ndipo linapatsidwa mphamvu zoluma ngati za zinkhanira pa dziko lapansi.
Locusts came out of the smoke onto the earth. [They were given] {[God] gave them} power [to sting people], like scorpions [sting people].
4 Dzombelo linalamulidwa kuti lisawononge udzu wa pa dziko lapansi, kapena chomera chilichonse, kapena mtengo uliwonse, koma anthu okhawo amene analibe chizindikiro cha Mulungu pa mphumi zawo.
[God] told the locusts that they should not harm grass, nor any plants, nor any tree. [God said that they should harm only] those people who did not have a mark on the forehead [to show that they belonged to God].
5 Silinapatsidwe mphamvu yowapha koma yowazunza kwa miyezi isanu. Ndipo ululu umene anthuwo anawumva unali ngati wa chinkhanira chikaluma munthu.
[God] did not allow the locusts to kill those people. Instead, [he] allowed them to continue torturing people for five months. When they tortured people, the pain those people felt was like the pain a scorpion causes when it stings someone.
6 Masiku amenewo anthu adzafunafuna imfa koma sadzayipeza. Adzalakalaka kufa koma imfa izidzawathawa.
During the time [when the locusts torture rebellious people, the pain will be so bad that] people will want to find a way to die, but they will not be able to [PRS].
7 Dzombe linkaoneka ngati akavalo okonzekera nkhondo. Pamitu pawo panali ngati zipewa zaufumu zagolide ndipo nkhope zawo ngati za anthu.
The locusts looked like horses that are ready for battle. They had on their heads what looked like golden crowns. Their faces were like the faces of people.
8 Tsitsi lawo linali ngati la amayi, mano awo ngati a mikango.
They had [long] hair like the [long] hair of women. Their teeth were [strong], like lions’ teeth.
9 Dzombelo linavala za pachifuwa zachitsulo. Phokoso la mapiko awo linali ngati phokoso la magaleta ankhondo ambiri okokedwa ndi akavalo othamangira ku nkhondo.
They wore metal breastplates. [When they were flying], their wings made a noise like the roar when many horses [pull chariots as they are] rushing into battle.
10 Linali ndi michira ngati zinkhanira ndi mbola. Mʼmichira yake munali mphamvu yozunza nayo anthu kwa miyezi isanu.
They had tails like scorpions have. With their tails they stung [people] for five months.
11 Mfumu yawo inali mngelo wolamulira Chidzenje chakuya chija. Mʼchihebri dzina lake ndi Abadoni ndipo mʼChigriki ndi Apoliyoni (tanthauzo lake ndiye kuti, Wowononga). (Abyssos )
The king who ruled over them was the angel of the underworld. His name in the Hebrew language is Abaddon. In the Greek language it is Apollyon. [Both of] those names [mean ‘Destroyer’]. (Abyssos )
12 Tsoka loyamba lapita; matsoka ena awiri akubwerabe.
That was the end of the first terrible event. [Be aware that] two tragic events are still to come.
13 Mngelo wachisanu ndi chimodzi anayimba lipenga lake, ndipo ndinamva liwu lochokera ku ngodya zinayi za guwa lansembe lagolide lija lokhala pamaso pa Mulungu.
The sixth angel blew his trumpet. Then I heard a voice from the four corners of the golden altar that is in God’s presence.
14 Liwulo linati kwa mngelo wachisanu ndi chimodzi amene anali ndi lipenga uja, “Masula angelo anayi amene anamangidwa pa mtsinje waukulu wa Yufurate.”
It was saying to the sixth angel, the one who had the trumpet, “Release the four angels whom [I] have bound at the great river Euphrates!”
15 Ndipo anamasulidwadi angelo anayi aja amene anasungidwa kukonzekera ora ili, tsiku ili, mwezi uwu ndi chaka ichi kuti aphe limodzi la magawo atatu a anthu.
The four angels were released, those who had been {[He] released the four angels, whom [God] had} kept ready for that [exact] hour of that day, of that month, of that year. They were released {[He] released them} in order that they might enable [their soldiers to] kill a third of the [rebellious] people.
16 Ndinamva chiwerengero cha ankhondo a pa akavalo aja, kuti chinali 200 miliyoni.
The number of the soldiers riding on horses who did that was 200 million. I heard [someone say] how many there were.
17 Akavalo ndi okwerapo amene ndinaona mʼmasomphenya anga ankaoneka motere: Zovala za pachifukwa pawo zinali zofiira ngati moto, zobiriwira ngati utsi, ndi zachikasu ngati miyala ya sulufule. Mitu ya akavalowo inali ngati ya mikango ndipo mʼkamwa mwawo munkatuluka moto, utsi ndi sulufule.
In the vision I saw what the horses and the [beings] that rode them looked like. They [wore] breastplates that were [red] like fire, [dusky blue] like smoke, and [yellow] like sulfur. The heads of the horses were like the heads of lions. From their mouths came fire, smoke, and [fumes of burning] sulfur.
18 Gawo limodzi la magawo atatu a anthu linaphedwa ndi miliri yamoto, utsi ndi sulufule zimene zinkachoka mʼkamwa mwawo.
Those three things—the fire, the smoke, and the [burning] sulfur from [the horses’] mouths—killed a third of the [rebellious] people.
19 Mphamvu za akavalowo inali mʼkamwa mwawo ndi mʼmichira mwawo; pakuti michira yawo inali ngati njoka; ndi mitu imene inkalumira.
The horses had power with their mouths and with their tails. Their tails have heads like snakes by which they harm people.
20 Anthu ena onse amene sanaphedwe ndi miliri imeneyi sanalapebe kuti asiye ntchito zawo zoyipa. Iwo sanasiye kupembedza ziwanda ndi mafano agolide, asiliva, amkuwa, amwala ndi amtengo, mafano amene sangathe kuona, kumva kapena kuyankhula.
The rest of the [rebellious] people, those who were not killed by these plagues of [fire and smoke and burning sulfur], did not turn from their sinful behavior. [They did not stop worshipping] the idols that they had made with their own hands. They did not stop worshipping demons and idols [that were made] of gold, of silver, of bronze, of stone, and of wood, [even though they are idols] that can neither see nor hear nor walk.
21 Sanalapenso kuleka zakupha, zamatsenga awo, zachigololo zawo kapena umbava wawo.
They did not stop murdering people, or practicing sorcery, or acting in sexually immoral ways, or stealing [things].