< Chivumbulutso 9 >

1 Mngelo wachisanu anayimba lipenga lake, ndipo ndinaona nyenyezi ikugwa pa dziko lapansi kuchokera ku thambo. Nyenyeziyo inapatsidwa kiyi ya ku chidzenje chakuya. (Abyssos g12)
Amalalu, a:igele dunu bi da dalabede fulaboi. Na ba: loba, gasumuni afae da osoboga sa: i. Gode da gi ema i. Amo gi da Gelabo Nosonodafa (A: bisi), amo doasimu gi e da lai dagoi. (Abyssos g12)
2 Nyenyeziyo itatsekula pa chidzenje chakuyacho panatuluka utsi ngati wochokera mʼngʼanjo yayikulu. Dzuwa ndi thambo zinada chifukwa cha utsi ochokera mʼdzenjemo. (Abyssos g12)
Gasumuni da amo uli dogoi doasili, mobi amo lalu bagade mobi defele heda: beba: le, eso hadigi uligiba: le, gasi bagade ba: i. (Abyssos g12)
3 Ndipo mʼkati mwa utsimo munatuluka dzombe kukalowa mʼdziko lapansi ndipo linapatsidwa mphamvu zoluma ngati za zinkhanira pa dziko lapansi.
Amalalu, danuba: bagohame da amo mobi ganodini esalu yolesili, osobo bagadega sa: i. Ilia da gasa amo gamaloa defele lai dagoi.
4 Dzombelo linalamulidwa kuti lisawononge udzu wa pa dziko lapansi, kapena chomera chilichonse, kapena mtengo uliwonse, koma anthu okhawo amene analibe chizindikiro cha Mulungu pa mphumi zawo.
Gode da ilima amane sia: i, “Dilia gisi amola ifa huluane mae wadela: ma! Be nowa dunu ilia Gode Ea dawa: digima: ne ilegesu dedesu odagiga hame dedei galea, amo fawane wadela: ma.
5 Silinapatsidwe mphamvu yowapha koma yowazunza kwa miyezi isanu. Ndipo ululu umene anthuwo anawumva unali ngati wa chinkhanira chikaluma munthu.
Dilia ili mae medole legema, be udigili oubi biyale gala amoga ilima se bagade ima!” Amo se iasu da se amo gamaloa ea gasonasu defele ba: i.
6 Masiku amenewo anthu adzafunafuna imfa koma sadzayipeza. Adzalakalaka kufa koma imfa izidzawathawa.
Amo oubi biyale gala ganodini, dunu huluane ilia da bogomu logo hogoi helele hame ba: mu. Dafawane, ilia da bogomusa: bagade hanamu, be bogosu da ilima hobeamu.
7 Dzombe linkaoneka ngati akavalo okonzekera nkhondo. Pamitu pawo panali ngati zipewa zaufumu zagolide ndipo nkhope zawo ngati za anthu.
Amo danuba: ilia ba: su da gegesu hosi amo defele ba: i. Ilia dialuma da: iya gouli habuga agoane ba: i amola ilia odagi da dunu ilia odagi agoane ba: i.
8 Tsitsi lawo linali ngati la amayi, mano awo ngati a mikango.
Ilia dialuma hinabo da uda dialuma hinabo agoane sedadedafa ba: i, amola ilia bese da laione wa: me amo ilia bese agoane ba: i.
9 Dzombelo linavala za pachifuwa zachitsulo. Phokoso la mapiko awo linali ngati phokoso la magaleta ankhondo ambiri okokedwa ndi akavalo othamangira ku nkhondo.
Ilia bida: igia da: igene ga: su liligi sali ba: i. Ilia ougia da sia: amo hosi ilia sa: liode hiougili gegemusa: ahoa amo ea genena: genena: be defele nabi.
10 Linali ndi michira ngati zinkhanira ndi mbola. Mʼmichira yake munali mphamvu yozunza nayo anthu kwa miyezi isanu.
Ilia la: go amola gasonasu guisu da gamaloa ea liligi agoane ba: i. Ilia da la: go amoga gasonabeba: le, dunu da oubi biyale gala amoga, se bagade nabalumu.
11 Mfumu yawo inali mngelo wolamulira Chidzenje chakuya chija. Mʼchihebri dzina lake ndi Abadoni ndipo mʼChigriki ndi Apoliyoni (tanthauzo lake ndiye kuti, Wowononga). (Abyssos g12)
Ilia ouligisu da a: igele dunu amo da Gelabo Nosonodafa (A: bisi) gala amoma ouligisu esala. Ea dio da Hibulu sia: ga “Aba: dane.” Galigi sia: ga, ea dio da Abolione (dawa: loma: ne da “Gugunufinisisu Dunu”). (Abyssos g12)
12 Tsoka loyamba lapita; matsoka ena awiri akubwerabe.
Defea! Se nabasu afadafa da dagoi. Be se nabasu aduna eno da misunu galebe.
13 Mngelo wachisanu ndi chimodzi anayimba lipenga lake, ndipo ndinamva liwu lochokera ku ngodya zinayi za guwa lansembe lagolide lija lokhala pamaso pa Mulungu.
Amalalu, a:igele dunu gafe da dalabede fulaboi. Na nabaloba, sia: da gouliga hamoi oloda amo Gode Ea midadi gala, amo hegomai biyaduyale gala amoga misi.
14 Liwulo linati kwa mngelo wachisanu ndi chimodzi amene anali ndi lipenga uja, “Masula angelo anayi amene anamangidwa pa mtsinje waukulu wa Yufurate.”
Sia: da a: igele dunu gafe ema amane sia: i, “A: igele dunu biyaduyale gala ilia da Iufala: idisi Hano amo gadenene lala: gili esala. Ilia halegale masa: ne, dia ilia lala: gi fadegama!”
15 Ndipo anamasulidwadi angelo anayi aja amene anasungidwa kukonzekera ora ili, tsiku ili, mwezi uwu ndi chaka ichi kuti aphe limodzi la magawo atatu a anthu.
Amalalu, e da a: igele biyaduyale gala ilia lala: gi fadegai. Bai Gode da ilia amo aua, amo eso, amo oubi, amo ode, amoga ilia osobo bagade dunu fi udiana agoane mogili afafane, afadafa medole legemusa: , momagele ilegei.
16 Ndinamva chiwerengero cha ankhondo a pa akavalo aja, kuti chinali 200 miliyoni.
Na nabaloba, dadi gagui dunu amo da hosi da: iya fila heda: i ilia idi da 200,000,000.
17 Akavalo ndi okwerapo amene ndinaona mʼmasomphenya anga ankaoneka motere: Zovala za pachifukwa pawo zinali zofiira ngati moto, zobiriwira ngati utsi, ndi zachikasu ngati miyala ya sulufule. Mitu ya akavalowo inali ngati ya mikango ndipo mʼkamwa mwawo munkatuluka moto, utsi ndi sulufule.
Na esala ba: su amo ganodini, na da hosi amola amoga fila heda: i dunu ba: i. Ilia bida: igiga da: igene ga: su liligi yoi, ela: me amola bua: iya: i ba: i. Hosi ilia dialuma da laione wa: me amo ilia dialuma agoane ba: i. Ilia lafidili, lalu, mobi amola salafa manebe ba: i.
18 Gawo limodzi la magawo atatu a anthu linaphedwa ndi miliri yamoto, utsi ndi sulufule zimene zinkachoka mʼkamwa mwawo.
Amalalu, osobo bagade fi dunu da mogili udiana agoane hamone, idi afae da huluane lalu, mobi amola salafa, hosi ilia lafidili manebe ba: i, amoga medole legei dagoi ba: i.
19 Mphamvu za akavalowo inali mʼkamwa mwawo ndi mʼmichira mwawo; pakuti michira yawo inali ngati njoka; ndi mitu imene inkalumira.
Hosi ilia gasa da ilia lafi amola ilia la: go, amo ganodini diala. Ilia la: go da sania agoane dialuma gala, amo da dunu gasomanusa: dawa:
20 Anthu ena onse amene sanaphedwe ndi miliri imeneyi sanalapebe kuti asiye ntchito zawo zoyipa. Iwo sanasiye kupembedza ziwanda ndi mafano agolide, asiliva, amkuwa, amwala ndi amtengo, mafano amene sangathe kuona, kumva kapena kuyankhula.
Dunu fifi asi gala eno, ilia amo medosu liligi amoga hame medole legei. Be ilia wadela: i loboga hamoi ‘gode’ liligi ilima sia: ne gadosu hou hame yolesi. Ilia da Fio liligi amola loboga hamoi ‘gode’ liligi amo gouli, silifa, balasi, igi amola ifa amoga hamoi liligi, (ba: su, nabasu, ahoasu amola hame dawa: liligi), amo dawa: beba: le ilia Godema sinidigimusa: hame dawa: i.
21 Sanalapenso kuleka zakupha, zamatsenga awo, zachigololo zawo kapena umbava wawo.
Amola ilia da dunu fasu hou, wamuni dawa: su hou, wadela: i uda lasu hou amola wamolasu hou amoba: le hame gogosia: i amola hame yolesi.

< Chivumbulutso 9 >