< Chivumbulutso 7 >

1 Zitatha izi ndinaona angelo anayi atayima pa mbali zinayi za dziko lapansi, atagwira mphepo zinayi za dziko lapansi kuletsa kuti mphepo iliyonse isawombe pa dziko kapena pa nyanja kapena pa mtengo uliwonse.
And after this, I saw four angels standing on the four quarters of the earth, holding the four winds of the earth, so that no wind would blow on the earth, or on the sea, or on any tree.
2 Kenaka ndinaona mngelo wina akuchokera kummawa, ali ndi chidindo cha Mulungu wamoyo. Iye anafuwulira angelo anayi aja amene anapatsidwa mphamvu yowononga dziko ndi nyanja kuti,
I saw another angel ascend from the sunrise, having the seal of the living God. He called out with a loud voice to the four angels to whom it was given to harm the earth and the sea,
3 “Musawononge dziko, nyanja ndi mitengo kufikira titalemba chizindikiro pa mphumi za atumiki a Mulungu wathu.”
saying, "Do not harm the earth, neither the sea, nor the trees, until we have sealed the servants of our God on their foreheads."
4 Choncho ndinamva chiwerengero cha amene ankayenera kulembedwa chizindikiro aja. Analipo okwanira 144,000 kuchokera ku mafuko onse a Israeli.
I heard the number of those who were sealed, one hundred forty-four thousand, sealed out of every tribe of the children of Israel:
5 Ochokera fuko la Yuda analipo 12,000 amene analembedwa chizindikiro. Ochokera fuko la Rubeni analipo 12,000; ochokera fuko la Gadi analipo 12,000;
of the tribe of Judah were sealed twelve thousand, of the tribe of Reuben twelve thousand, of the tribe of Gad twelve thousand,
6 ochokera fuko la Aseri analipo 12,000; ochokera fuko la Nafutali analipo 12,000; ochokera fuko la Manase analipo 12,000;
of the tribe of Asher twelve thousand, of the tribe of Naphtali twelve thousand, of the tribe of Manasseh twelve thousand,
7 ochokera fuko la Simeoni analipo 12,000; ochokera fuko la Levi analipo 12,000; ochokera fuko la Isakara analipo 12,000;
of the tribe of Simeon twelve thousand, of the tribe of Levi twelve thousand, of the tribe of Issachar twelve thousand,
8 ochokera fuko la Zebuloni analipo 12,000; ochokera fuko la Yosefe analipo 12,000; ochokera fuko la Benjamini analipo 12,000.
of the tribe of Zebulun twelve thousand, of the tribe of Joseph twelve thousand, of the tribe of Benjamin were sealed twelve thousand.
9 Zitatha izi ndinayangʼana patsogolo panga ndipo ndinaona gulu lalikulu la anthu loti munthu sangathe kuliwerenga lochokera dziko lililonse, fuko lililonse, mtundu wa anthu uliwonse ndi chiyankhulo chilichonse, atayima patsogolo pa mpando waufumu, pamaso pa Mwana Wankhosa. Iwo anali atavala mikanjo yoyera ndi kunyamula nthambi za kanjedza mʼmanja mwawo.
After these things I looked, and suddenly there was a great multitude, which no one could number, out of every nation and of all tribes, peoples, and languages, standing before the throne and before the Lamb, dressed in white robes, with palm branches in their hands.
10 Ndipo ankafuwula mokweza kuti: “Chipulumutso chimachokera kwa Mulungu wathu, wokhala pa mpando waufumu ndi kwa Mwana Wankhosa.”
They shouted with a loud voice, saying, "Salvation be to our God, who sits on the throne, and to the Lamb."
11 “Angelo onse anayimirira kuzungulira mpando waufumu uja, kuzunguliranso akuluakulu aja ndi zamoyo zinayi zija. Angelo aja anadzigwetsa pansi chafufumimba patsogolo pa mpando waufumu napembedza Mulungu.
All the angels were standing around the throne, the elders, and the four living creatures; and they fell on their faces before the throne, and worshiped God,
12 Iwo anati, “Ameni! Matamando ndi ulemerero, nzeru, mayamiko, ulemu, ulamuliro ndi mphamvu zikhale kwa Mulungu wathu kunthawi zanthawi, Ameni!” (aiōn g165)
saying, "Amen. Blessing, glory, wisdom, thanksgiving, honor, power, and might, be to our God forever and ever. Amen." (aiōn g165)
13 Pamenepo mmodzi wa akuluakulu aja anandifunsa kuti, “Kodi avala mikanjo yoyerawa ndani ndipo akuchokera kuti?”
One of the elders answered, saying to me, "These who are arrayed in white robes, who are they, and from where did they come?"
14 Ine ndinayankha kuti, “Mbuye wanga mukudziwa ndinu.” Tsono iye anandiwuza kuti, “Amenewa ndi amene anatuluka mʼmazunzo aakulu aja. Anachapa mikanjo yawo naziyeretsa mʼmagazi a Mwana Wankhosa.
So I said to him, "My lord, you know." He said to me, "These are the ones who came out of the great tribulation. They washed their robes, and made them white in the Lamb's blood.
15 Nʼchifukwa chake, “iwowa ali patsogolo pa mpando waufumu wa Mulungu ndipo akutumikira usana ndi usiku mʼNyumba ya Mulungu; ndipo Iye wokhala pa mpando waufumu adzawaphimba ndi tenti yake.
Therefore they are before the throne of God, they serve him day and night in his temple. He who sits on the throne will spread his tabernacle over them.
16 ‘Iwowa sadzamvanso njala, sadzamvanso ludzu, dzuwa kapena kutentha kulikonse sikudzawawotcha.’
They will hunger no more, neither thirst any more; neither will the sun beat on them, nor any heat;
17 Pakuti Mwana Wankhosa amene ali pakati pa mpando waufumu adzakhala mʼbusa wawo. ‘Iye adzawatsogolera ku akasupe a madzi amoyo.’ ‘Ndipo Mulungu adzawapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo.’”
for the Lamb who is in the midst of the throne shepherds them, and leads them to springs of waters of life. And God will wipe away every tear from their eyes."

< Chivumbulutso 7 >