< Chivumbulutso 7 >

1 Zitatha izi ndinaona angelo anayi atayima pa mbali zinayi za dziko lapansi, atagwira mphepo zinayi za dziko lapansi kuletsa kuti mphepo iliyonse isawombe pa dziko kapena pa nyanja kapena pa mtengo uliwonse.
Nakon toga vidjeh: četiri anđela stoje na četiri kraja zemlje zadržavajući četiri vjetra zemaljska da nikakav vjetar ne puše ni zemljom ni morem nit ikojim drvećem.
2 Kenaka ndinaona mngelo wina akuchokera kummawa, ali ndi chidindo cha Mulungu wamoyo. Iye anafuwulira angelo anayi aja amene anapatsidwa mphamvu yowononga dziko ndi nyanja kuti,
I vidjeh drugoga jednog anđela gdje uzlazi od istoka sunčeva s pečatom Boga živoga. On povika iza glasa onoj četvorici anđela kojima bi dano nauditi zemlji i moru:
3 “Musawononge dziko, nyanja ndi mitengo kufikira titalemba chizindikiro pa mphumi za atumiki a Mulungu wathu.”
“Ne udite ni zemlji ni moru ni drveću dok ne opečatimo sluge Boga našega na čelima!”
4 Choncho ndinamva chiwerengero cha amene ankayenera kulembedwa chizindikiro aja. Analipo okwanira 144,000 kuchokera ku mafuko onse a Israeli.
I začujem broj opečaćenih - sto četrdeset i četiri tisuće opečaćenih iz svih plemena sinova Izraelovih:
5 Ochokera fuko la Yuda analipo 12,000 amene analembedwa chizindikiro. Ochokera fuko la Rubeni analipo 12,000; ochokera fuko la Gadi analipo 12,000;
iz plemena Judina dvanaest tisuća opečaćenih, iz plemena Rubenova dvanaest tisuća, iz plemena Gadova dvanaest tisuća,
6 ochokera fuko la Aseri analipo 12,000; ochokera fuko la Nafutali analipo 12,000; ochokera fuko la Manase analipo 12,000;
iz plemena Ašerova dvanaest tisuća, iz plemena Naftalijeva dvanest tisuća, iz plemena Manašeova dvanaest tisuća,
7 ochokera fuko la Simeoni analipo 12,000; ochokera fuko la Levi analipo 12,000; ochokera fuko la Isakara analipo 12,000;
iz plemena Šimunova dvanaest tisuća, iz plemena Levijeva dvanaest tisuća, iz plemena Jisakarova dvanaest tisuća,
8 ochokera fuko la Zebuloni analipo 12,000; ochokera fuko la Yosefe analipo 12,000; ochokera fuko la Benjamini analipo 12,000.
iz plemena Zebulunova dvanaest tisuća, iz plemena Josipova dvanaest tisuća, iz plemena Benjaminova dvanaest tisuća opečaćenih.
9 Zitatha izi ndinayangʼana patsogolo panga ndipo ndinaona gulu lalikulu la anthu loti munthu sangathe kuliwerenga lochokera dziko lililonse, fuko lililonse, mtundu wa anthu uliwonse ndi chiyankhulo chilichonse, atayima patsogolo pa mpando waufumu, pamaso pa Mwana Wankhosa. Iwo anali atavala mikanjo yoyera ndi kunyamula nthambi za kanjedza mʼmanja mwawo.
Nakon toga vidjeh: eno velikoga mnoštva, što ga nitko ne mogaše izbrojiti, iz svakoga naroda, i plemena, i puka, i jezika! Stoje pred prijestoljem i pred Jaganjcem odjeveni u bijele haljine; palme im u rukama.
10 Ndipo ankafuwula mokweza kuti: “Chipulumutso chimachokera kwa Mulungu wathu, wokhala pa mpando waufumu ndi kwa Mwana Wankhosa.”
Viču iz glasa: “Spasenje Bogu našemu koji sjedi na prijestolju i Jaganjcu!”
11 “Angelo onse anayimirira kuzungulira mpando waufumu uja, kuzunguliranso akuluakulu aja ndi zamoyo zinayi zija. Angelo aja anadzigwetsa pansi chafufumimba patsogolo pa mpando waufumu napembedza Mulungu.
I svi anđeli, što stajahu uokolo prijestolja i starješina i četiriju bića, padoše pred prijestoljem ničice, na svoja lica,
12 Iwo anati, “Ameni! Matamando ndi ulemerero, nzeru, mayamiko, ulemu, ulamuliro ndi mphamvu zikhale kwa Mulungu wathu kunthawi zanthawi, Ameni!” (aiōn g165)
i pokloniše se Bogu govoreći: “Amen! Blagoslov i slava, i mudrost, i zahvalnica, i čast, i moć i snaga Bogu našemu u vijeke vjekova. Amen.” (aiōn g165)
13 Pamenepo mmodzi wa akuluakulu aja anandifunsa kuti, “Kodi avala mikanjo yoyerawa ndani ndipo akuchokera kuti?”
I jedan me od starješina upita: “Ovi odjeveni u bijele haljine, tko su i odakle dođoše?”
14 Ine ndinayankha kuti, “Mbuye wanga mukudziwa ndinu.” Tsono iye anandiwuza kuti, “Amenewa ndi amene anatuluka mʼmazunzo aakulu aja. Anachapa mikanjo yawo naziyeretsa mʼmagazi a Mwana Wankhosa.
Odgovorih mu: “Gospodine moj, ti to znaš.” A on će mi: “Oni dođoše iz nevolje velike i oprali su haljine svoje i ubijelili ih u krvi Jaganjčevoj.
15 Nʼchifukwa chake, “iwowa ali patsogolo pa mpando waufumu wa Mulungu ndipo akutumikira usana ndi usiku mʼNyumba ya Mulungu; ndipo Iye wokhala pa mpando waufumu adzawaphimba ndi tenti yake.
Zato su pred prijestoljem Božjim i služe mu dan i noć u hramu njegovu, i Onaj koji sjedi na prijestolju razapet će Šator svoj nad njima.
16 ‘Iwowa sadzamvanso njala, sadzamvanso ludzu, dzuwa kapena kutentha kulikonse sikudzawawotcha.’
Neće više gladovati ni žeđati, neće ih više paliti sunce nit ikakva žega
17 Pakuti Mwana Wankhosa amene ali pakati pa mpando waufumu adzakhala mʼbusa wawo. ‘Iye adzawatsogolera ku akasupe a madzi amoyo.’ ‘Ndipo Mulungu adzawapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo.’”
jer - Jaganjac koji je posred prijestolja bit će pastir njihov i vodit će ih na izvore voda života. I otrt će Bog svaku suzu s očiju njihovih.”

< Chivumbulutso 7 >