< Chivumbulutso 6 >

1 Ndinaona pamene Mwana Wankhosa anatsekula chomatira choyamba cha zomatira zisanu ndi ziwiri zija. Ndipo ndinamva chimodzi mwa zamoyo zinayi zija chikunena liwu lomveka ngati bingu kuti, “Bwera!”
Viděl jsem, jak Beránek rozlomil první z těch sedmi pečetí, a slyšel jsem, že jedna ze čtyř bytostí zvolala hromovým hlasem: „Pojď!“
2 Nditayangʼana patsogolo pake ndinaona kavalo woyera! Wokwerapo wake anali ndi uta ndipo anapatsidwa chipewa chaufumu, ndipo anatuluka kupita kukagonjetsa anthu ena.
Tu se ukázal bílý kůň. Jezdec na tom koni – mající v ruce luk a na hlavě věnec vítězů – vyjel, aby dobýval jedno vítězství za druhým.
3 Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachiwiri, ndinamva chamoyo chachiwiri chija chikuti, “Bwera!”
Když Beránek rozlomil druhou pečeť, druhá z bytostí před trůnem zvolala: „Pojď!“
4 Pamenepo kavalo wina wofiira anatulukira. Wokwerapo wake anapatsidwa mphamvu yochotsa mtendere pa dziko lapansi ndi kuchititsa anthu kuti aziphana wina ndi mnzake. Iyeyu anapatsidwa lupanga lalikulu.
Tentokrát vyběhl ohnivě rudý kůň s jezdcem ozbrojeným velikým mečem. Ten měl moc rozrušit mír na zemi, takže se lidé začali vzájemně pobíjet.
5 Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachitatu, ndinamva chamoyo chachitatu chikuti, “Bwera!” Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wakuda! Wokwerapo wake anali ndi masikelo awiri mʼmanja mwake.
Pak Beránek rozlomil třetí pečeť a třetí bytost zavolala: „Pojď!“Ukázal se černý kůň, jehož jezdec nesl váhy na znamení nedostatku.
6 Ndinamva ngati liwu kuchokera pakati pa zamoyo zinayi zija likuti, “Kilogalamu imodzi ya tirigu mtengo ndi malipiro a tsiku limodzi ndipo makilogalamu atatu a barele mtengo wake ndi malipiro a tsiku limodzi koma usawononge mafuta ndi vinyo!”
Ze středu těch čtyř bytostí zaznělo: „Celý den bude člověk pracovat za kilo pšenice nebo za tři kila ječmene. Ponech jim však dostatek oleje a vína!“
7 Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachinayi, ndinamva chamoyo chachinayi chija chikunena kuti, “Bwera!”
Když Beránek odstranil čtvrtou pečeť, slyšel jsem čtvrtou bytost, jak volá: „Pojď!“
8 Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wotuwa! Wokwerapo wake dzina lake linali Imfa ndipo Hade inali kumutsatira pambuyo pake. Anapatsidwa ulamuliro pa gawo limodzi la magawo anayi a dziko lapansi kuti aphe ndi lupanga, njala, mliri, ndi zirombo zakuthengo za mʼdziko lapansi. (Hadēs g86)
Vyrazil kůň mrtvolně bledé barvy a jela na něm sama Smrt a za ní zůstávali mrtví. Čtvrtina země jí padla za oběť: rozsévala války, hlad, epidemie a přírodní pohromy. (Hadēs g86)
9 Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachisanu, ndinaona kunsi kwa guwa lansembe kunali mizimu ya anthu amene anaphedwa chifukwa cha Mawu a Mulungu ndi chifukwa chochitira umboni.
Tu Beránek rozlomil pátou pečeť svitku a já jsem uviděl oltář a kolem něho ty, kteří podstoupili mučednickou smrt pro věrnost Bohu a pro hlásání Boží zvěsti.
10 Iwo anafuwula kuti, “Mudzawaleka mpaka liti, Inu Ambuye wamkulu, woyera ndi woona, osawaweruza anthu okhala mʼdziko lapansi ndi kulipsira magazi athu?”
Společně volali: „Svatý Pane, ty plníš své sliby. Kdy vykonáš spravedlivý soud a potrestáš ty, kdo prolili naši krev?“
11 Pamenepo aliyense wa anthuwo anapatsidwa mwinjiro woyera ndipo anawuzidwa kuti adikire pangʼono kufikira chiwerengero cha anzawo ndi abale awo amene anayeneranso kuphedwa ngati iwo, chitakwanira.
Potom každý z nich obdržel bílý šat na znamení vítězství. Bylo jim však řečeno, aby ještě čekali, protože se k nim mají připojit další mučedníci pro Krista, jejich spolupracovníci a bratři.
12 Ndinayangʼanitsitsa pamene ankatsekula chomatira chachisanu ndi chimodzi. Ndipo panachitika chivomerezi champhamvu. Dzuwa linada ngati chiguduli chopanga ndi bweya wambuzi wakuda. Mwezi wonse unafiira ngati magazi,
Pak jsem viděl, že Beránek rozlomil šestou pečeť. Nastalo velké zemětřesení, slunce se zatmělo jako smuteční flór, měsíc zrudl jako krev.
13 ndipo nyenyezi zakuthambo zinagwa pa dziko lapansi ngati muja zimagwera nkhuyu zotsalira mu mtengo mphepo yamphamvu ikawomba.
Hvězdy padaly z nebe jako zralé plody ze stromu, do kterého se opře silný vítr.
14 Thambo linachoka ngati amayalulira mphasa ndipo phiri lililonse ndi chilumba chilichonse zinachotsedwa pa malo pake.
Obloha zmizela, jako když se svine plachta. Každá hora a každý ostrov se pohnul ze svého místa.
15 Kenaka, mafumu a pa dziko lapansi, ana a mafumu, atsogoleri a ankhondo, olemera, amphamvu, kapolo aliyense, ndi mfulu aliyense anakabisala kumapanga ndi pakati pa matanthwe a ku mapiri.
Vládci země, úředníci, vojevůdci, boháči a mocipáni, otroci jako svobodní, všichni se schovávali do jeskyní a skalních rozsedlin.
16 Iwo anafuwulira mapiri ndi matanthwe kuti, “Tigwereni ndi kutivundikira kuti asatione wokhala pa mpando waufumuyo ndi kupulumuka ku mkwiyo wa Mwana Wankhosa!
Volali: „Hory a skály, sesuňte se na nás a ukryjte nás před pohledem toho, který sedí na trůnu, a před Beránkovým hněvem!
17 Pakuti tsiku lalikulu la mkwiyo wawo lafika ndipo ndi ndani angathe kulimbapo?”
Den jeho soudu přichází, kdo z nás může obstát?“

< Chivumbulutso 6 >