< Chivumbulutso 22 +

1 Ndipo mngeloyo anandionetsa mtsinje wamadzi amoyo, oyera ngati mwala wa krustalo ukutuluka ku mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa,
و نهری از آب حیات به من نشان داد که درخشنده بود، مانند بلور و از تخت خدا و بره جاری می‌شود.۱
2 Ukuyenda pakati pa msewu waukulu wa mu mzindawo. Mbali iliyonse ya mtsinjewo kunali mtengo wamoyo, utabala zipatso khumi ndi ziwiri. Kubereka zipatso mwezi uliwonse. Ndipo masamba a mtengowo ndi mankhwala wochiritsa anthu a mitundu ina.
و در وسط شارع عام آن و بر هر دو کناره نهر، درخت حیات را که دوازده میوه می‌آورد یعنی هر ماه میوه خود رامی دهد؛ و برگهای آن درخت برای شفای امت هامی باشد.۲
3 Sipadzakhalanso temberero lililonse. Mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa udzakhala mu mzindawo, ndipo atumiki ake adzamutumikira.
و دیگر هیچ لعنت نخواهد بود و تخت خدا و بره در آن خواهد بود و بندگانش او راعبادت خواهند نمود.۳
4 Iwo adzaona nkhope yake ndipo dzina lake lidzalembedwa pa mphumi zawo.
و چهره او را خواهنددید و اسم وی بر پیشانی‌ایشان خواهد بود.۴
5 Sipadzakhalanso usiku. Sadzafuna kuwala kwa nyale kapena kwa dzuwa pakuti Ambuye Mulungu adzakhala kuwala kwawo. Ndipo adzalamulira kwamuyaya. (aiōn g165)
ودیگر شب نخواهد بود و احتیاج به چراغ و نورآفتاب ندارند، زیرا خداوند خدا بر ایشان روشنایی می‌بخشد و تا ابدالاباد سلطنت خواهندکرد. (aiōn g165)۵
6 Mngeloyo anandiwuza kuti, “Mawu awa ndi okhulupirika ndi owona. Ambuye Mulungu wa mizimu ya aneneri anatumiza mngelo wake kudzaonetsa atumiki ake zinthu zimene ziyenera kuchitika posachedwapa.”
و مرا گفت: «این کلام امین و راست است وخداوند خدای ارواح انبیا، فرشته خود را فرستادتا به بندگان خود آنچه را که زود می‌باید واقع شود، نشان دهد.»۶
7 “Taonani, ndikubwera posachedwa! Wodala ndi amene asunga mawu oneneratu za kutsogolo a mʼbuku ili.”
«و اینک به زودی می‌آیم. خوشابحال کسی‌که کلام نبوت این کتاب را نگاه دارد.»۷
8 Ine Yohane, ndine amene ndinamva ndi kuona zinthu izi. Ndipo pamene ndinamva ndi kuona izi ndinagwa pansi kuti ndipembedze mngelo amene amandionetsa zimenezi.
و من، یوحنا، این امور را شنیدم و دیدم وچون شنیدم و دیدم، افتادم تا پیش پایهای آن فرشته‌ای که این امور را به من نشان داد سجده کنم.۸
9 Koma mngeloyo anandiwuza kuti, “Usatero ayi! Ine ndine wotumikira monga iwe pamodzi ndi abale ako aneneri ndi onse amene amasunga mawu a mʼbuku pembedzani Mulungu.”
او مرا گفت: «زنهار نکنی، زیرا که همخدمت با تو هستم و با انبیا یعنی برادرانت و باآنانی که کلام این کتاب را نگاه دارند. خدا راسجده کن.»۹
10 Kenaka anandiwuza kuti, “Usabise mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili chifukwa nthawi yayandikira.
و مرا گفت: «کلام نبوت این کتاب را مهر مکن زیرا که وقت نزدیک است.۱۰
11 Wochita zoyipa apitirire kuchita zoyipazo; wochita zonyansa apitirire kuchita zonyansazo; wochita zabwino apitirire kuchita zabwinozo; ndipo woyera mtima apitirire kukhala woyera mtima.”
هر‌که ظالم است، باز ظلم کند و هر‌که خبیث است، بازخبیث بماند و هر‌که عادل است، باز عدالت کند وهر‌که مقدس است، باز مقدس بشود.»۱۱
12 “Taonani, ndikubwera posachedwa! Ndikubwera ndi mphotho zanga kuti ndidzapereke kwa aliyense malinga ndi zimene anachita.
«و اینک به زودی می‌آیم و اجرت من با من است تا هر کسی را بحسب اعمالش جزا دهم.۱۲
13 Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chimaliziro ndine.
من الف و یاء و ابتدا و انتها و اول و آخر هستم۱۳
14 “Odala amene achapa mikanjo yawo, kuti akhale ndi ufulu wopita ku mtengo wamoyo ndi kuti akalowe mʼzipata za mu mzindawo.
خوشابحال آنانی که رختهای خود رامی شویند تا بر درخت حیات اقتدار یابند و به دروازه های شهر درآیند،۱۴
15 Kunja kuli agalu, amatsenga, achiwerewere, akupha anthu, opembedza mafano ndi aliyense amene amakonda bodza ndi kulichita.
زیرا که سگان وجادوگران و زانیان و قاتلان و بت‌پرستان و هر‌که دروغ را دوست دارد و بعمل آورد، بیرون می‌باشند.۱۵
16 “Ine Yesu, ndatuma mngelo wanga kuti achitire umboni uwu ku mipingo. Ine ndine Muzu ndi Chipatso cha Davide ndipo ndine Nthanda Yonyezimira.”
من عیسی فرشته خود را فرستادم تاشما را در کلیساها بدین امور شهادت دهم. من ریشه و نسل داود و ستاره درخشنده صبح هستم.»۱۶
17 Mzimu Woyera ndi mkwatibwi akuti, “Bwerani!” Ndipo amene akumva anena kuti Bwerani! Iye amene ali ndi ludzu abwere, ndipo aliyense amene afuna alandire mphatso yaulere ya madzi amoyo.
و روح و عروس می‌گویند: «بیا!» و هر‌که می‌شنود بگوید: «بیا!» و هر‌که تشنه باشد، بیاید وهر‌که خواهش دارد، از آب حیات بی‌قیمت بگیرد.۱۷
18 Ndikuchenjeza aliyense amene akumva mawu onena zamʼtsogolo a mʼbukuli kuti, “Ngati wina awonjezerapo kalikonse, Mulungu adzamuwonjezera miliri imene yalembedwa mʼbuku ili.
زیرا هر کس را که کلام نبوت این کتاب را بشنود، شهادت می‌دهم که اگر کسی بر آنهابیفزاید، خدا بلایای مکتوب در این کتاب را بروی خواهد افزود.۱۸
19 Ndipo wina akachotsapo mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili, Mulungu adzachotsa gawo lake pa mtengo wamoyo ndi la mu mzinda woyera zimene zanenedwa mʼbuku ili.”
و هر گاه کسی از کلام این نبوت چیزی کم کند، خدا نصیب او را از درخت حیات و از شهر مقدس و از چیزهایی که در این کتاب نوشته است، منقطع خواهد کرد.۱۹
20 Iye amene akuchitira umboni pa zinthu izi akuti, “Inde, Ine ndikubwera posachedwa.” Ameni. Bwerani Ambuye Yesu.
او که بر این امور شاهد است، می‌گوید: «بلی، به زودی می‌آیم!» آمین. بیا، ای خداوند عیسی!۲۰
21 Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi anthu onse. Ameni.
فیض خداوند ما عیسی مسیح با همه شماباد. آمین.۲۱

< Chivumbulutso 22 +