< Chivumbulutso 22 +
1 Ndipo mngeloyo anandionetsa mtsinje wamadzi amoyo, oyera ngati mwala wa krustalo ukutuluka ku mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa,
And he pointed out to me a river of water of life, bright as crystal, issuing forth out of the throne of God and of the Lamb,
2 Ukuyenda pakati pa msewu waukulu wa mu mzindawo. Mbali iliyonse ya mtsinjewo kunali mtengo wamoyo, utabala zipatso khumi ndi ziwiri. Kubereka zipatso mwezi uliwonse. Ndipo masamba a mtengowo ndi mankhwala wochiritsa anthu a mitundu ina.
in the midst of the broadway thereof. And, on this side of the river and on that, was a tree of life, bearing twelve crops of fruit, every several month, yielding its fruit; and, the leaves of the tree, were for the healing of the nations,
3 Sipadzakhalanso temberero lililonse. Mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa udzakhala mu mzindawo, ndipo atumiki ake adzamutumikira.
And, no curse, shall there be, any more; and, the throne of God and of the Lamb, shall be, therein, —and his servants will render divine service unto him,
4 Iwo adzaona nkhope yake ndipo dzina lake lidzalembedwa pa mphumi zawo.
and they shall see his face, and, his name, [shall be] upon their foreheads.
5 Sipadzakhalanso usiku. Sadzafuna kuwala kwa nyale kapena kwa dzuwa pakuti Ambuye Mulungu adzakhala kuwala kwawo. Ndipo adzalamulira kwamuyaya. (aiōn )
And, night, shall be, no more; and they have no need of the light of a lamp or the light of a sun, because, the Lord, God, will give them light, —and they shall reign unto the ages of ages. (aiōn )
6 Mngeloyo anandiwuza kuti, “Mawu awa ndi okhulupirika ndi owona. Ambuye Mulungu wa mizimu ya aneneri anatumiza mngelo wake kudzaonetsa atumiki ake zinthu zimene ziyenera kuchitika posachedwapa.”
And he said unto me—These words, are faithful and true; and, the Lord, the God of the spirits of the prophets, hath sent his messenger, to point out, unto his servants, the things which must needs come to pass with speed.
7 “Taonani, ndikubwera posachedwa! Wodala ndi amene asunga mawu oneneratu za kutsogolo a mʼbuku ili.”
And—Lo! I come speedily! Happy, is he that keepeth the words of the prophecy of this scroll.
8 Ine Yohane, ndine amene ndinamva ndi kuona zinthu izi. Ndipo pamene ndinamva ndi kuona izi ndinagwa pansi kuti ndipembedze mngelo amene amandionetsa zimenezi.
And, I, John, am he that was hearing and seeing these things; and, when I had heard and seen, I fell down to do homage at the feet of the messenger who had been pointing out unto me these things, —
9 Koma mngeloyo anandiwuza kuti, “Usatero ayi! Ine ndine wotumikira monga iwe pamodzi ndi abale ako aneneri ndi onse amene amasunga mawu a mʼbuku pembedzani Mulungu.”
and he saith unto me—See [thou do it] not! A fellow-servant, am I, of thee, and of thy brethren the prophets, and of them who keep the words of this scroll: unto God, do homage.
10 Kenaka anandiwuza kuti, “Usabise mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili chifukwa nthawi yayandikira.
And he saith unto me—Do not seal up the words of the prophecy of this scroll, for, the season, is, near:
11 Wochita zoyipa apitirire kuchita zoyipazo; wochita zonyansa apitirire kuchita zonyansazo; wochita zabwino apitirire kuchita zabwinozo; ndipo woyera mtima apitirire kukhala woyera mtima.”
He that is doing unjustly, let him do unjustly, still, and, he that is filthy, let him be made filthy, still; and, he that is righteous, let him do righteousness, still, and, he that is holy, let him be hallowed, still: —
12 “Taonani, ndikubwera posachedwa! Ndikubwera ndi mphotho zanga kuti ndidzapereke kwa aliyense malinga ndi zimene anachita.
Lo! I come speedily, and my reward is with me, to render unto each one as, his, work is.
13 Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chimaliziro ndine.
I, am the A and the Z, the First and the Last, the Beginning and the End.
14 “Odala amene achapa mikanjo yawo, kuti akhale ndi ufulu wopita ku mtengo wamoyo ndi kuti akalowe mʼzipata za mu mzindawo.
Happy, they who are washing their robes, that their right may be unto the tree of life and, by the gates, they may enter into the city.
15 Kunja kuli agalu, amatsenga, achiwerewere, akupha anthu, opembedza mafano ndi aliyense amene amakonda bodza ndi kulichita.
Outside, are the dogs, and the sorcerers, and the unchaste, and the murderers, and the idolaters, and every one loving and doing falsehood.
16 “Ine Yesu, ndatuma mngelo wanga kuti achitire umboni uwu ku mipingo. Ine ndine Muzu ndi Chipatso cha Davide ndipo ndine Nthanda Yonyezimira.”
I, Jesus, have sent my messenger, to bear witness unto you of these things, for the assemblies. I, am the Root and the Offspring of David, the bright and the morning Star.
17 Mzimu Woyera ndi mkwatibwi akuti, “Bwerani!” Ndipo amene akumva anena kuti Bwerani! Iye amene ali ndi ludzu abwere, ndipo aliyense amene afuna alandire mphatso yaulere ya madzi amoyo.
And, the Spirit and the Bride, say—Come! and, he that heareth, let him say—Come! and, he that is athirst, let him come, —he that will, let him take of the water of life, freely.
18 Ndikuchenjeza aliyense amene akumva mawu onena zamʼtsogolo a mʼbukuli kuti, “Ngati wina awonjezerapo kalikonse, Mulungu adzamuwonjezera miliri imene yalembedwa mʼbuku ili.
I, bear witness, unto every one that heareth the words of the prophecy of this scroll: —If anyone shall lay aught upon them, God, will lay upon him, the plagues which are written in this scroll;
19 Ndipo wina akachotsapo mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili, Mulungu adzachotsa gawo lake pa mtengo wamoyo ndi la mu mzinda woyera zimene zanenedwa mʼbuku ili.”
And, if anyone shall take away from the words of this prophetic scroll, God, will take away his part, —from the tree of life, and out of the holy city, —[from] the things written in this scroll.
20 Iye amene akuchitira umboni pa zinthu izi akuti, “Inde, Ine ndikubwera posachedwa.” Ameni. Bwerani Ambuye Yesu.
He that beareth witness of these things, saith—Yea! I come, speedily. Amen! come, Lord Jesus!
21 Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi anthu onse. Ameni.
The favour of the Lord Jesus [Christ] be with the saints.