< Chivumbulutso 21 >
1 Kenaka ndinaona kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano pakuti kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zinapita ndipo kunalibenso nyanja ina iliyonse.
In videl sem novo nebo in novo zemljo, kajti prvo nebo in prva zemlja sta prešla in ni bilo več morja.
2 Ndinaona mzinda wopatulika, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu, utakonzedwa ngati mkwatibwi wovala zokongola kukonzekera mwamuna wake.
In jaz, Janez, sem videl sveto mesto, novi Jeruzalem, prihajati dol od Boga, iz nebes, pripravljeno, kakor je nevesta okrašena za svojega soproga.
3 Ndipo ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Mpando Waufumu kuti, “Taonani! Malo wokhalapo Mulungu ali pakati pa anthu, ndipo Iye adzakhala ndi anthuwo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulungu mwini adzakhala nawo nakhala Mulungu wawo.
In zaslišal sem močan glas z neba, rekoč: »Glej, šotorsko svetišče Boga je z ljudmi in prebival bo z njimi in oni bodo njegovi ljudje in sam Bog bo z njimi in bo njihov Bog.
4 ‘Mulungu adzapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo. Sikudzakhalanso imfa kapena kukhuza maliro kapena kulira kapena ululu popeza zakale zapita.’”
In Bog bo obrisal vse solze z njihovih oči; in ne bo več smrti, niti bridkosti, niti jokanja, niti ne bo več nobene bolečine, kajti prejšnje stvari so minile.«
5 Amene anakhala pa mpando waufumuyo anati, “Ndikulenga zinthu zonse zikhale zatsopano!” Ndipo anati, “Lemba izi, pakuti mawu awa ndi okhulupirika ndi woona.”
In tisti, ki je sedel na prestolu, je rekel: »Poglej, vse stvari delam nove.« In rekel mi je: »Zapiši, kajti te besede so resnične in zveste.«
6 Iye anandiwuza kuti, “Kwatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa onse akumva ludzu, ndidzawapatsa zakumwa zaulere zochokera ku kasupe wamadzi amoyo.
In rekel mi je: »Končano je. Jaz sem Alfa in Omega, začetek in konec. Temu, ki je žejen, bom zastonj dal iz studenca vode življenja.
7 Iye amene adzapambane adzalandira zonsezi, ndipo ndidzakhala Mulungu wake ndi Iye adzakhala mwana wanga.
Kdor premaga, bo podedoval vse stvari; in jaz bom njegov Bog, on pa bo moj sin.
8 Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.” (Limnē Pyr )
Toda strahopetci, neverniki, gnusneži, morilci, vlačugarji, čarodeji, malikovalci in vsi lažnivci bodo imeli svoj delež v jezeru, ki gori z ognjem in žveplom, kar je druga smrt.« (Limnē Pyr )
9 Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja, anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi miliri yotsiriza isanu ndi iwiri anandiwuza kuti, “Bwera, ine ndidzakuonetsa mkwatibwi wa Mwana Wankhosa.”
In k meni je prišel eden izmed sedmih angelov, ki so imeli sedem stekleničk, polnih sedmih zadnjih nadlog in govoril z menoj, rekoč: »Pridi sèm, pokazal ti bom nevesto, Jagnjetovo ženo.«
10 Ndipo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku phiri lalikulu ndi lalitali nandionetsa mzinda wopatulika, Yerusalemu ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu.
In v duhu me je odvedel proč, k veliki in visoki gori in mi pokazal tisto veliko mesto, sveti Jeruzalem, ki se je od Boga spuščal z neba,
11 Unawala ndi ulemerero wa Mulungu, ndipo kuthwanima kwake kunali ngati mwala wamtengowapatali, ngati jasipa; woyera ngati krustalo.
ki je imel Božjo slavo in njegova svetloba je bila podobna najdragocenejšemu kamnu, celó podobna kamnu jaspisu, čistemu kakor kristal;
12 Mzindawo unali ndi mpanda waukulu ndi wautali, unali ndi zipata khumi ndi ziwiri, ndipo panali angelo khumi ndi awiri. Pa chipata chilichonse panayima mngelo. Pa chipata chilichonse panalembedwa dzina la fuko la Israeli.
in imelo je veliko in visoko obzidje in dvanajst velikih vrat in ob velikih vratih dvanajst angelov in na njih so bila napisana imena, ki so imena dvanajsterih rodov Izraelovih otrok:
13 Kummawa kunali zipata zitatu, kumpoto zitatu, kummwera zitatu ndi kumadzulo zitatu.
na vzhodu troje velikih vrat, na severu troje velikih vrat, na jugu troje velikih vrat in na zahodu troje velikih vrat.
14 Mpanda wa mzindawu unali ndi maziko khumi ndi awiri ndipo pa mazikopo panali mayina khumi ndi awiri a atumwi a Mwana Wankhosa.
In obzidje mesta je imelo dvanajst temeljev in na njih imena dvanajsterih Jagnjetovih apostolov.
15 Mngelo amene ankayankhula nane uja anali ndi ndodo yagolide yoyezera mzindawo, zipata zake ndi mpanda wake.
In tisti, ki je govoril z menoj, je imel zlat trst, da izmeri mesto in njegova velika vrata in njegovo obzidje.
16 Mzindawo unamangidwa mofanana kutalika kwake, mulitali ndi mulifupi munali mofanana. Anayeza mzindawo ndi ndodo ija ndipo anapeza kuti mulitali, mulifupi ndi msinkhu wake kutalika kwake kunali makilomita 2,200.
In mesto leži štirioglato in dolžina je tako velika kakor širina; in s trstom je izmeril mesto, dvanajst tisoč dolžin brazd. Njegova dolžina in širina in višina so enake.
17 Anayesa mpanda uja ndipo kuchindikala kwake kunali kopitirirapo mamita 65 monga mwa muyeso wa anthu umene mngelo anagwiritsa ntchito.
In izmeril je njegovo obzidje: sto štiriinštirideset komolcev, glede na človeško mero, to je, od angela.
18 Mpandawo unapangidwa ndi yasipa, ndipo mzindawo unali wagolide oyengeka owala ngati galasi.
In obzidje je bilo zgrajeno iz jaspisa in mesto je bilo čisto zlato, podobno čistemu steklu.
19 Maziko a mpanda wa mzindawo anali okongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali ya mtundu uliwonse. Maziko oyamba anali yasipa, achiwiri anali safiro, achitatu ndi kalikedo, achinayi ndi simaragido,
In temelji mestnega obzidja so bili okrašeni z vsemi vrstami dragocenih kamnov. Prvi temelj je bil jaspis, drugi safir, tretji kalcedon, četrti smaragd,
20 achisanu ndi sardiyo, achisanu ndi chiwiri ndi krusolito, achisanu ndi chitatu ndi berulo, achisanu ndi chinayi ndi topaziyo, a khumi ndi krusoprazo, a khumi ndi chimodzi ndi huakito, a khumi ndi chiwiri ndi emetusto.
peti sardoniks, šesti sardij, sedmi hrizolit, osmi beril, deveti topaz, deseti hrizopraz, enajsti hijacint, dvanajsti ametist.
21 Zipata khumi ndi ziwiri zija zinapangidwa ndi ngale, chipata chilichonse chinapangidwa ndi ngale imodzi. Misewu ya mzindawo inali yopangidwa ndi golide oyengeka, owala ngati galasi.
In dvanajst velikih vrat je bilo dvanajst biserov; vsaka posamezna velika vrata so bila iz enega bisera in ulica mesta je bila čisto zlato, kakor bi bilo prosojno steklo.
22 Ine sindinaone Nyumba ya Mulungu iliyonse mu mzindawo chifukwa Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse ndi Mwana Wankhosa ndiwo Nyumba yake.
In v njem nisem videl templja, kajti njegov tempelj sta Gospod Bog Vsemogočni in Jagnje.
23 Palibe chifukwa choti dzuwa kapena mwezi ziwale popeza mu mzindawo ulemerero wa Mulungu ndiwo umawalamo ndipo nyale yake ndi Mwana Wankhosa uja.
In mesto ni potrebovalo sonca niti lune, da bi sijala nanj, kajti razsvetljevala ga je Božja slava in Jagnje je njegova svetloba.
24 Mitundu ya anthu idzayenda mʼkuwala kwake ndipo mafumu a dziko lapansi adzabweretsa ulemerero wawo mu mzindamo.
In narodi teh, ki so rešeni, bodo hodili v njegovi svetlobi in kralji zemlje vanj prinesejo svojo slavo in čast.
25 Zipata zake sizidzatsekedwa ngakhale tsiku limodzi lomwe pakuti sikudzakhala usiku kumeneko.
In njegova velika vrata se podnevi sploh ne bodo zaprla, kajti tam ne bo noči.
26 Ulemerero ndi ulemu wa mitundu ya anthu adzapita nazo kumeneko.
In vanj bodo prinesli slavo in čast narodov.
27 Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa.
In tja nikakor ne bo stopilo karkoli, kar omadežuje niti karkoli počne ogabno ali počne laž, temveč tisti, ki so zapisani v Jagnjetovi knjigi življenja.