< Chivumbulutso 21 >
1 Kenaka ndinaona kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano pakuti kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zinapita ndipo kunalibenso nyanja ina iliyonse.
anantaraM navInam AkAzamaNDalaM navInA pRthivI ca mayA dRSTe yataH prathamam AkAzamaNDalaM prathamA pRthivI ca lopaM gate samudro 'pi tataH paraM na vidyate|
2 Ndinaona mzinda wopatulika, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu, utakonzedwa ngati mkwatibwi wovala zokongola kukonzekera mwamuna wake.
aparaM svargAd avarohantI pavitrA nagarI, arthato navInA yirUzAlamapurI mayA dRSTA, sA varAya vibhUSitA kanyeva susajjitAsIt|
3 Ndipo ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Mpando Waufumu kuti, “Taonani! Malo wokhalapo Mulungu ali pakati pa anthu, ndipo Iye adzakhala ndi anthuwo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulungu mwini adzakhala nawo nakhala Mulungu wawo.
anantaraM svargAd eSa mahAravo mayA zrutaH pazyAyaM mAnavaiH sArddham IzvarasyAvAsaH, sa taiH sArddhaM vatsyati te ca tasya prajA bhaviSyanti, Izvarazca svayaM teSAm Izvaro bhUtvA taiH sArddhaM sthAsyati|
4 ‘Mulungu adzapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo. Sikudzakhalanso imfa kapena kukhuza maliro kapena kulira kapena ululu popeza zakale zapita.’”
teSAM netrebhyazcAzrUNi sarvvANIzvareNa pramArkSyante mRtyurapi puna rna bhaviSyati zokavilApaklezA api puna rna bhaviSyanti, yataH prathamAni sarvvANi vyatItini|
5 Amene anakhala pa mpando waufumuyo anati, “Ndikulenga zinthu zonse zikhale zatsopano!” Ndipo anati, “Lemba izi, pakuti mawu awa ndi okhulupirika ndi woona.”
aparaM siMhAsanopaviSTo jano'vadat pazyAhaM sarvvANi nUtanIkaromi| punaravadat likha yata imAni vAkyAni satyAni vizvAsyAni ca santi|
6 Iye anandiwuza kuti, “Kwatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa onse akumva ludzu, ndidzawapatsa zakumwa zaulere zochokera ku kasupe wamadzi amoyo.
pana rmAm avadat samAptaM, ahaM kaH kSazca, aham Adirantazca yaH pipAsati tasmA ahaM jIvanadAyiprasravaNasya toyaM vinAmUlyaM dAsyAmi|
7 Iye amene adzapambane adzalandira zonsezi, ndipo ndidzakhala Mulungu wake ndi Iye adzakhala mwana wanga.
yo jayati sa sarvveSAm adhikArI bhaviSyati, ahaJca tasyezvaro bhaviSyAmi sa ca mama putro bhaviSyati|
8 Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.” (Limnē Pyr )
kintu bhItAnAm avizvAsinAM ghRNyAnAM narahantRNAM vezyAgAminAM mohakAnAM devapUjakAnAM sarvveSAm anRtavAdinAJcAMzo vahnigandhakajvalitahrade bhaviSyati, eSa eva dvitIyo mRtyuH| (Limnē Pyr )
9 Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja, anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi miliri yotsiriza isanu ndi iwiri anandiwuza kuti, “Bwera, ine ndidzakuonetsa mkwatibwi wa Mwana Wankhosa.”
anantaraM zeSasaptadaNDaiH paripUrNAH sapta kaMsA yeSAM saptadUtAnAM kareSvAsan teSAmeka Agatya mAM sambhASyAvadat, AgacchAhaM tAM kanyAm arthato meSazAvakasya bhAvibhAryyAM tvAM darzayAmi|
10 Ndipo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku phiri lalikulu ndi lalitali nandionetsa mzinda wopatulika, Yerusalemu ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu.
tataH sa AtmAviSTaM mAm atyuccaM mahAparvvatameMka nItvezvarasya sannidhitaH svargAd avarohantIM yirUzAlamAkhyAM pavitrAM nagarIM darzitavAn|
11 Unawala ndi ulemerero wa Mulungu, ndipo kuthwanima kwake kunali ngati mwala wamtengowapatali, ngati jasipa; woyera ngati krustalo.
sA IzvarIyapratApaviziSTA tasyAstejo mahArgharatnavad arthataH sUryyakAntamaNitejastulyaM|
12 Mzindawo unali ndi mpanda waukulu ndi wautali, unali ndi zipata khumi ndi ziwiri, ndipo panali angelo khumi ndi awiri. Pa chipata chilichonse panayima mngelo. Pa chipata chilichonse panalembedwa dzina la fuko la Israeli.
tasyAH prAcIraM bRhad uccaJca tatra dvAdaza gopurANi santi tadgopuropari dvAdaza svargadUtA vidyante tatra ca dvAdaza nAmAnyarthata isrAyelIyAnAM dvAdazavaMzAnAM nAmAni likhitAni|
13 Kummawa kunali zipata zitatu, kumpoto zitatu, kummwera zitatu ndi kumadzulo zitatu.
pUrvvadizi trINi gopurANi uttaradizi trINi gopurANi dakSiNadiSi trINi gopurANi pazcImadizi ca trINi gopurANi santi|
14 Mpanda wa mzindawu unali ndi maziko khumi ndi awiri ndipo pa mazikopo panali mayina khumi ndi awiri a atumwi a Mwana Wankhosa.
nagaryyAH prAcIrasya dvAdaza mUlAni santi tatra meSAzAvAkasya dvAdazapreritAnAM dvAdaza nAmAni likhitAni|
15 Mngelo amene ankayankhula nane uja anali ndi ndodo yagolide yoyezera mzindawo, zipata zake ndi mpanda wake.
anaraM nagaryyAstadIyagopurANAM tatprAcIrasya ca mApanArthaM mayA sambhASamANasya dUtasya kare svarNamaya ekaH parimANadaNDa AsIt|
16 Mzindawo unamangidwa mofanana kutalika kwake, mulitali ndi mulifupi munali mofanana. Anayeza mzindawo ndi ndodo ija ndipo anapeza kuti mulitali, mulifupi ndi msinkhu wake kutalika kwake kunali makilomita 2,200.
nagaryyA AkRtizcaturasrA tasyA dairghyaprasthe same| tataH paraM sa tega parimANadaNDena tAM nagarIM parimitavAn tasyAH parimANaM dvAdazasahasranalvAH| tasyA dairghyaM prastham uccatvaJca samAnAni|
17 Anayesa mpanda uja ndipo kuchindikala kwake kunali kopitirirapo mamita 65 monga mwa muyeso wa anthu umene mngelo anagwiritsa ntchito.
aparaM sa tasyAH prAcIraM parimitavAn tasya mAnavAsyArthato dUtasya parimANAnusAratastat catuzcatvAriMzadadhikAzatahastaparimitaM |
18 Mpandawo unapangidwa ndi yasipa, ndipo mzindawo unali wagolide oyengeka owala ngati galasi.
tasya prAcIrasya nirmmitiH sUryyakAntamaNibhi rnagarI ca nirmmalakAcatulyena zuddhasuvarNena nirmmitA|
19 Maziko a mpanda wa mzindawo anali okongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali ya mtundu uliwonse. Maziko oyamba anali yasipa, achiwiri anali safiro, achitatu ndi kalikedo, achinayi ndi simaragido,
nagaryyAH prAcIrasya mUlAni ca sarvvavidhamahArghamaNibhi rbhUSitAni| teSAM prathamaM bhittimUlaM sUryyakAntasya, dvitIyaM nIlasya, tRtIyaM tAmramaNeH, caturthaM marakatasya,
20 achisanu ndi sardiyo, achisanu ndi chiwiri ndi krusolito, achisanu ndi chitatu ndi berulo, achisanu ndi chinayi ndi topaziyo, a khumi ndi krusoprazo, a khumi ndi chimodzi ndi huakito, a khumi ndi chiwiri ndi emetusto.
paJcamaM vaidUryyasya, SaSThaM zoNaratnasya, saptamaM candrakAntasya, aSTamaM gomedasya, navamaM padmarAgasya, dazamaM lazUnIyasya, ekAdazaM Serojasya, dvAdazaM marTISmaNezcAsti|
21 Zipata khumi ndi ziwiri zija zinapangidwa ndi ngale, chipata chilichonse chinapangidwa ndi ngale imodzi. Misewu ya mzindawo inali yopangidwa ndi golide oyengeka, owala ngati galasi.
dvAdazagopurANi dvAdazamuktAbhi rnirmmitAni, ekaikaM gopuram ekaikayA muktayA kRtaM nagaryyA mahAmArgazcAcchakAcavat nirmmalasuvarNena nirmmitaM|
22 Ine sindinaone Nyumba ya Mulungu iliyonse mu mzindawo chifukwa Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse ndi Mwana Wankhosa ndiwo Nyumba yake.
tasyA antara ekamapi mandiraM mayA na dRSTaM sataH sarvvazaktimAn prabhuH paramezvaro meSazAvakazca svayaM tasya mandiraM|
23 Palibe chifukwa choti dzuwa kapena mwezi ziwale popeza mu mzindawo ulemerero wa Mulungu ndiwo umawalamo ndipo nyale yake ndi Mwana Wankhosa uja.
tasyai nagaryyai dIptidAnArthaM sUryyAcandramasoH prayojanaM nAsti yata Izvarasya pratApastAM dIpayati meSazAvakazca tasyA jyotirasti|
24 Mitundu ya anthu idzayenda mʼkuwala kwake ndipo mafumu a dziko lapansi adzabweretsa ulemerero wawo mu mzindamo.
paritrANaprAptalokanivahAzca tasyA Aloke gamanAgamane kurvvanti pRthivyA rAjAnazca svakIyaM pratApaM gauravaJca tanmadhyam Anayanti|
25 Zipata zake sizidzatsekedwa ngakhale tsiku limodzi lomwe pakuti sikudzakhala usiku kumeneko.
tasyA dvArANi divA kadApi na rotsyante nizApi tatra na bhaviSyati|
26 Ulemerero ndi ulemu wa mitundu ya anthu adzapita nazo kumeneko.
sarvvajAtInAM gauravapratApau tanmadhyam AneSyete|
27 Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa.
parantvapavitraM ghRNyakRd anRtakRd vA kimapi tanmadhyaM na pravekSyati meSazAvakasya jIvanapustake yeSAM nAmAni likhitAni kevalaM ta eva pravekSyanti|