< Chivumbulutso 21 >
1 Kenaka ndinaona kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano pakuti kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zinapita ndipo kunalibenso nyanja ina iliyonse.
Hessafe guye tani ooratha salone ooratha biitta beyadis. Kase saloyne kase biittay aadhi bida. Hayssafe guye abayka deena.
2 Ndinaona mzinda wopatulika, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu, utakonzedwa ngati mkwatibwi wovala zokongola kukonzekera mwamuna wake.
Geesha katamiya ooratha Yerusalamey ba azinas giigetida mishira mala lo7a giigettada Salo Xoossa achchefe wodhdhishin tani beyadis.
3 Ndipo ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Mpando Waufumu kuti, “Taonani! Malo wokhalapo Mulungu ali pakati pa anthu, ndipo Iye adzakhala ndi anthuwo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulungu mwini adzakhala nawo nakhala Mulungu wawo.
Algazape hizgiza gita qaalay kezishin tani siyadis “Heko Xoossa aqosoy asara dees. Izi isttara deyana. Isttika iza dereta gidana. Xoossi izi isttara gidana. Izi istta Xoossu gidana.
4 ‘Mulungu adzapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo. Sikudzakhalanso imfa kapena kukhuza maliro kapena kulira kapena ululu popeza zakale zapita.’”
Izi istta ayfepe ayfunthu wursi quccana. Kase wogay aadhida gishshi hayqoy woykko muuzotethi woykko yeehoy woykko waayey hayssafe guye deena.”
5 Amene anakhala pa mpando waufumuyo anati, “Ndikulenga zinthu zonse zikhale zatsopano!” Ndipo anati, “Lemba izi, pakuti mawu awa ndi okhulupirika ndi woona.”
He alga bolla uttidayssika “Heko tani wursaka oorathi kessana!” gides. Qasseka tana “Hayssi qaalazi ammanettida tumu gidida gishshi ne hayssa xaafa!” gides.
6 Iye anandiwuza kuti, “Kwatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa onse akumva ludzu, ndidzawapatsa zakumwa zaulere zochokera ku kasupe wamadzi amoyo.
Hessafe guye taasi hizgides “Polettides! alfayne omegay, koyrone wursethi tanakko, saamottida uras tani deyo pultto haathe qanxxisontta ta izas coo mela immana.
7 Iye amene adzapambane adzalandira zonsezi, ndipo ndidzakhala Mulungu wake ndi Iye adzakhala mwana wanga.
Xoonida uray hayssa laatana. Taka izades Goda gidana. Izika taasi na gidana.
8 Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.” (Limnē Pyr )
Gido attin hanko baboti, isttas ammanoy bayindayti, tunati, asa shempo wodhizayti, Laymmatizayti, betizayti, eeqas goynizayti, wordotizayti, heyta wursota qaaday diinen exxiza tama abba giddon gidana. Hessika nam7antho hayqokko.” (Limnē Pyr )
9 Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja, anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi miliri yotsiriza isanu ndi iwiri anandiwuza kuti, “Bwera, ine ndidzakuonetsa mkwatibwi wa Mwana Wankhosa.”
Wursethan laapun bochati isttan kumida laapun xuwata oykida laapun kiitanchatape issay taako yiidi tana “Ha ya, ta nena dorsaza machcheyo mishirayo bessana” gides.
10 Ndipo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku phiri lalikulu ndi lalitali nandionetsa mzinda wopatulika, Yerusalemu ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu.
Izi tana ayanan issi gita dhoqa zuma bolla kessidi geesha katamaya ooratha Yerusalemey Xoossa achafe salope wodhdhizaro besides.
11 Unawala ndi ulemerero wa Mulungu, ndipo kuthwanima kwake kunali ngati mwala wamtengowapatali, ngati jasipa; woyera ngati krustalo.
Izaka Xoossa bonchon po7isayssu. Izi po7oza lo7etethay qass keehi bonchetiza shuchcha malane birile mala geeshine Iyassiphida geetettiza inqqo malakko.
12 Mzindawo unali ndi mpanda waukulu ndi wautali, unali ndi zipata khumi ndi ziwiri, ndipo panali angelo khumi ndi awiri. Pa chipata chilichonse panayima mngelo. Pa chipata chilichonse panalembedwa dzina la fuko la Israeli.
Izis tammane nam7u pengetara diza gita aduussa ginbe lashay dees. He tammane nam7u pengetan tammane nam7u Kiitanchati eqqidi naagetes. He pengeta bolla tammane nam7u Isiraa7eele kochata sunthi xaafeti uttides.
13 Kummawa kunali zipata zitatu, kumpoto zitatu, kummwera zitatu ndi kumadzulo zitatu.
Arishey mokkiza baggara heedzdzu pengey dees. Pude baggara heedzdzu pengey dees. Duge baggara hedzdzu pengey dees. Arishey wulliza baggara hedzdzu pengay dees.
14 Mpanda wa mzindawu unali ndi maziko khumi ndi awiri ndipo pa mazikopo panali mayina khumi ndi awiri a atumwi a Mwana Wankhosa.
He Katamay ginbe lashazas tammane nam7u waana magalati dettes. He magalata bolla tammane nam7u he dorsaza hawarista sunthi xaafeti dees.
15 Mngelo amene ankayankhula nane uja anali ndi ndodo yagolide yoyezera mzindawo, zipata zake ndi mpanda wake.
Hessa taas yootida Kiitanchazas he katamayone izi pengeta qasseka he ginbe lashaza izara wadhdhiza worqa zangey dees.
16 Mzindawo unamangidwa mofanana kutalika kwake, mulitali ndi mulifupi munali mofanana. Anayeza mzindawo ndi ndodo ija ndipo anapeza kuti mulitali, mulifupi ndi msinkhu wake kutalika kwake kunali makilomita 2,200.
He katamay adusatethine aahotethi oyddu baggaraka issi ginakko. He kiitanchayka katamayo ba izara wadhdhiza wadha zangezara wadhdhin adusatethay nam7u shiiyane oyddu xeetu kilo mitire mala giddies. Izi dhoqatethine aahotethika izi adusatetha gina giddies.
17 Anayesa mpanda uja ndipo kuchindikala kwake kunali kopitirirapo mamita 65 monga mwa muyeso wa anthu umene mngelo anagwiritsa ntchito.
Kiitanchazi ginbeza wodhdhides. He kiitanchazi izara wadhdhiza miishazi erettida wadha miishazi laapun tammane nam7u mitire mala giddies.
18 Mpandawo unapangidwa ndi yasipa, ndipo mzindawo unali wagolide oyengeka owala ngati galasi.
He ginbezi ginbetiday Iyasiphide geetettiza shuchankko. He katamayaka masttote mala geeya uttida geesha worqafe oothistadus.
19 Maziko a mpanda wa mzindawo anali okongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali ya mtundu uliwonse. Maziko oyamba anali yasipa, achiwiri anali safiro, achitatu ndi kalikedo, achinayi ndi simaragido,
He katamayssa garsa magala shuchchay duma duma al7o shuchchan lo7i giigides. Koyro magalezi Iyasiphide, nam7anthozi Sinpere, heedzdzanthozi Kelqedone, oydanthozi margide,
20 achisanu ndi sardiyo, achisanu ndi chiwiri ndi krusolito, achisanu ndi chitatu ndi berulo, achisanu ndi chinayi ndi topaziyo, a khumi ndi krusoprazo, a khumi ndi chimodzi ndi huakito, a khumi ndi chiwiri ndi emetusto.
Ichachanthoy sardonkise, usupunthoy sardiyone, laapunthoy kirstolobe, ospunthoy birile, udupunthoy wurawure, tammanthoy kirisphirasise, tammane issinthoy yakintte, tammane nam7unthoy ametisxinose geetettiza shuchchatapekko.
21 Zipata khumi ndi ziwiri zija zinapangidwa ndi ngale, chipata chilichonse chinapangidwa ndi ngale imodzi. Misewu ya mzindawo inali yopangidwa ndi golide oyengeka, owala ngati galasi.
He tammane nam7u pengetika tammane nam7u inqotakko. Pengeti wurka issay issay issi inqofe oothetida he katamay giddo ogey masttote mala haa zaari bessiza muuruta worqafe oothetides.
22 Ine sindinaone Nyumba ya Mulungu iliyonse mu mzindawo chifukwa Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse ndi Mwana Wankhosa ndiwo Nyumba yake.
Wursi danda7iza Godaa Xoossayne dorsazi izis kase `gidida gishshi he katamay giddon hara Xoossa keethe beya beyike.
23 Palibe chifukwa choti dzuwa kapena mwezi ziwale popeza mu mzindawo ulemerero wa Mulungu ndiwo umawalamo ndipo nyale yake ndi Mwana Wankhosa uja.
Xoossa bonchoy izis po7iza gishshine dorsazi izi po7o gidida gishshi he katamays awa arishey woykko aginay po7isanas koshshenna.
24 Mitundu ya anthu idzayenda mʼkuwala kwake ndipo mafumu a dziko lapansi adzabweretsa ulemerero wawo mu mzindamo.
Dereti izi po7ozan simeristana. Biitta kawoti wurka ba boncho izis ehana.
25 Zipata zake sizidzatsekedwa ngakhale tsiku limodzi lomwe pakuti sikudzakhala usiku kumeneko.
He Katamayn qamay bayinda gishshi izi pengeti ay wodeka gordettettena.
26 Ulemerero ndi ulemu wa mitundu ya anthu adzapita nazo kumeneko.
Hara kawota gitatethine bonchoy izis yaana.
27 Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa.
Harassiza miishey muleka gede izin galena. Tunateth oothizaytine wordo hasa7izayti muleka hee iziko galena. He iziko gelanayti istta sunthi kase he dorsaza deyo maxaafan xaafetidayta xalalakko.