< Chivumbulutso 21 >
1 Kenaka ndinaona kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano pakuti kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zinapita ndipo kunalibenso nyanja ina iliyonse.
J'ai vu un nouveau ciel et une nouvelle terre, car le premier ciel et la première terre ont disparu, et la mer n'est plus.
2 Ndinaona mzinda wopatulika, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu, utakonzedwa ngati mkwatibwi wovala zokongola kukonzekera mwamuna wake.
Je vis descendre du ciel, d'auprès de Dieu, la ville sainte, la nouvelle Jérusalem, préparée comme une épouse qui s'est parée pour son mari.
3 Ndipo ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Mpando Waufumu kuti, “Taonani! Malo wokhalapo Mulungu ali pakati pa anthu, ndipo Iye adzakhala ndi anthuwo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulungu mwini adzakhala nawo nakhala Mulungu wawo.
J'ai entendu du ciel une voix forte qui disait: « Voici la demeure de Dieu avec les hommes; il habitera avec eux, et ils seront son peuple, et Dieu lui-même sera avec eux comme leur Dieu.
4 ‘Mulungu adzapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo. Sikudzakhalanso imfa kapena kukhuza maliro kapena kulira kapena ululu popeza zakale zapita.’”
Il essuiera toute larme de leurs yeux. La mort ne sera plus; il n'y aura plus ni deuil, ni cri, ni douleur. Les premières choses ont disparu. »
5 Amene anakhala pa mpando waufumuyo anati, “Ndikulenga zinthu zonse zikhale zatsopano!” Ndipo anati, “Lemba izi, pakuti mawu awa ndi okhulupirika ndi woona.”
Celui qui est assis sur le trône dit: « Voici, je fais toutes choses nouvelles. » Il dit: « Ecris, car ces paroles de Dieu sont fidèles et vraies. »
6 Iye anandiwuza kuti, “Kwatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa onse akumva ludzu, ndidzawapatsa zakumwa zaulere zochokera ku kasupe wamadzi amoyo.
Il me dit: « Je suis l'Alpha et l'Oméga, le Commencement et la Fin. Je donnerai gratuitement à celui qui a soif de la source d'eau de la vie.
7 Iye amene adzapambane adzalandira zonsezi, ndipo ndidzakhala Mulungu wake ndi Iye adzakhala mwana wanga.
Celui qui vaincra, je lui donnerai ces choses. Je serai son Dieu, et il sera mon fils.
8 Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.” (Limnē Pyr )
Mais pour les lâches, les incrédules, les pécheurs, les abominables, les meurtriers, les impudiques, les enchanteurs, les idolâtres, et tous les menteurs, leur part est dans l'étang ardent de feu et de soufre, qui est la seconde mort. » (Limnē Pyr )
9 Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja, anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi miliri yotsiriza isanu ndi iwiri anandiwuza kuti, “Bwera, ine ndidzakuonetsa mkwatibwi wa Mwana Wankhosa.”
L'un des sept anges qui tenaient les sept coupes chargées des sept derniers fléaux vint, et il me parla en disant: « Viens ici. Je vais te montrer l'épouse, la femme de l'Agneau. »
10 Ndipo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku phiri lalikulu ndi lalitali nandionetsa mzinda wopatulika, Yerusalemu ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu.
Il me transporta en esprit sur une grande et haute montagne, et il me montra la ville sainte, Jérusalem, qui descendait du ciel d'auprès de Dieu,
11 Unawala ndi ulemerero wa Mulungu, ndipo kuthwanima kwake kunali ngati mwala wamtengowapatali, ngati jasipa; woyera ngati krustalo.
et qui avait la gloire de Dieu. Sa lumière était comme une pierre très précieuse, comme une pierre de jaspe, limpide comme du cristal.
12 Mzindawo unali ndi mpanda waukulu ndi wautali, unali ndi zipata khumi ndi ziwiri, ndipo panali angelo khumi ndi awiri. Pa chipata chilichonse panayima mngelo. Pa chipata chilichonse panalembedwa dzina la fuko la Israeli.
Elle avait une grande et haute muraille, avec douze portes, et aux portes douze anges, avec des noms écrits dessus, qui sont les noms des douze tribus des enfants d'Israël.
13 Kummawa kunali zipata zitatu, kumpoto zitatu, kummwera zitatu ndi kumadzulo zitatu.
Il y avait trois portes à l'orient, trois portes au nord, trois portes au midi, et trois portes à l'occident.
14 Mpanda wa mzindawu unali ndi maziko khumi ndi awiri ndipo pa mazikopo panali mayina khumi ndi awiri a atumwi a Mwana Wankhosa.
La muraille de la ville avait douze fondements, et sur eux douze noms des douze apôtres de l'Agneau.
15 Mngelo amene ankayankhula nane uja anali ndi ndodo yagolide yoyezera mzindawo, zipata zake ndi mpanda wake.
Celui qui me parlait avait pour mesure un roseau d'or pour mesurer la ville, ses portes et ses murs.
16 Mzindawo unamangidwa mofanana kutalika kwake, mulitali ndi mulifupi munali mofanana. Anayeza mzindawo ndi ndodo ija ndipo anapeza kuti mulitali, mulifupi ndi msinkhu wake kutalika kwake kunali makilomita 2,200.
La ville est carrée. Sa longueur est aussi grande que sa largeur. Il mesura la ville avec le roseau: douze mille douze stades. Sa longueur, sa largeur et sa hauteur sont égales.
17 Anayesa mpanda uja ndipo kuchindikala kwake kunali kopitirirapo mamita 65 monga mwa muyeso wa anthu umene mngelo anagwiritsa ntchito.
Sa muraille a cent quarante-quatre coudées, à la mesure d'un homme, c'est-à-dire d'un ange.
18 Mpandawo unapangidwa ndi yasipa, ndipo mzindawo unali wagolide oyengeka owala ngati galasi.
La construction de sa muraille était en jaspe. La ville était d'un or pur, comme du verre pur.
19 Maziko a mpanda wa mzindawo anali okongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali ya mtundu uliwonse. Maziko oyamba anali yasipa, achiwiri anali safiro, achitatu ndi kalikedo, achinayi ndi simaragido,
Les fondements de la muraille de la ville étaient ornés de toutes sortes de pierres précieuses. Le premier fondement était le jaspe, le second le saphir, le troisième la calcédoine, le quatrième l'émeraude,
20 achisanu ndi sardiyo, achisanu ndi chiwiri ndi krusolito, achisanu ndi chitatu ndi berulo, achisanu ndi chinayi ndi topaziyo, a khumi ndi krusoprazo, a khumi ndi chimodzi ndi huakito, a khumi ndi chiwiri ndi emetusto.
le cinquième le sardonyx, le sixième la sardoine, le septième la chrysolithe, le huitième le béryl, le neuvième le topaze, le dixième la chrysoprase, le onzième le jacinthe et le douzième l'améthyste.
21 Zipata khumi ndi ziwiri zija zinapangidwa ndi ngale, chipata chilichonse chinapangidwa ndi ngale imodzi. Misewu ya mzindawo inali yopangidwa ndi golide oyengeka, owala ngati galasi.
Les douze portes étaient douze perles. Chacune des portes était faite d'une perle. Les rues de la ville étaient en or pur, comme du verre transparent.
22 Ine sindinaone Nyumba ya Mulungu iliyonse mu mzindawo chifukwa Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse ndi Mwana Wankhosa ndiwo Nyumba yake.
Je n'y ai vu aucun temple, car le Seigneur Dieu tout-puissant et l'Agneau sont son temple.
23 Palibe chifukwa choti dzuwa kapena mwezi ziwale popeza mu mzindawo ulemerero wa Mulungu ndiwo umawalamo ndipo nyale yake ndi Mwana Wankhosa uja.
La ville n'a besoin ni du soleil ni de la lune pour briller, car la gloire même de Dieu l'éclaire et sa lampe est l'Agneau.
24 Mitundu ya anthu idzayenda mʼkuwala kwake ndipo mafumu a dziko lapansi adzabweretsa ulemerero wawo mu mzindamo.
Les nations marcheront à sa lumière. Les rois de la terre y apportent la gloire et l'honneur des nations.
25 Zipata zake sizidzatsekedwa ngakhale tsiku limodzi lomwe pakuti sikudzakhala usiku kumeneko.
Ses portes ne se fermeront pas le jour, car il n'y aura pas de nuit,
26 Ulemerero ndi ulemu wa mitundu ya anthu adzapita nazo kumeneko.
et l'on y introduira la gloire et l'honneur des nations pour qu'elles y entrent.
27 Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa.
Il n'y entrera rien de profane, ni personne qui commette une abomination ou un mensonge, mais seulement ceux qui sont écrits dans le livre de vie de l'Agneau.