< Chivumbulutso 2 >

1 “Lembera mngelo wa mpingo wa ku Efeso kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri zija mʼdzanja lake lamanja amene akuyenda pakati pa zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide.
Kwa malaika bha kanisa lya Efeso jhandikayi: 'Agha ndo malobhi gha jhola jhaikamu ila matonda ghala saba mu kibhoko kya muene kya kuume. Muene jhaigenda mu finara fya dhahabu fya taa saba ijobha naha,”
2 Ine ndimadziwa zochita zako, ntchito yako yowawa ndi kupirira kwako. Ine ndimadziwa kuti sungalekerere anthu oyipa amene amadzitcha atumwi pamene sichoncho, unawayesa, ndipo unawapeza kuti ndi abodza.
“Nimanyili kyaukhelili ni bidii jha jhobhi jha mbombo ni uvumilivu bhwa jhobhi thabiti, ni kwamba ghwibhwesya lepi kuhusiana nabhu bhabhajhele bhaovu, na ubhajaribu bhoha bhabhikikuta kujha mitume kumbe lepi, na bhabhonekene kujha bhadesi.
3 Iwe wapirira ndipo wakumana ndi zovuta chifukwa cha dzina langa, ndipo sunatope.
Nimanyili kujha ujhe ni subira ni uvumilivu, na ubhwesi ghamehele kwa ndabha jha lihina lya nene, na utondilepi bado.
4 Komabe ndili ndi chotsutsana nawe: Wataya chikondi chako chapoyamba.
Lakini ele ndo lyanijhe nalu dhidi jha jhobhi, ughulekili upendo ghwa jhobhi bhwa kubhwandelu.
5 Kumbukirani kuti munagwa kuchokera patali. Lapa ndikuchita zinthu zimene unkachita poyamba. Ngati sulapa ndidzabwera ndikukuchotsera choyikapo nyale chako pamalo pake.
Kwa hiyo ukhombokayi pa ubinili, ukatubuajhi ni kubhomba matendo ghaubhombeghe kuh'omela kubhuandu. Ukabelayi kutubu, nibeta kuhida kwa bhebhe ni kukibhosya kinara kya jhobhi kuh'oma mahali pa kyene.
6 Komabe chokomera chako ndi chakuti umadana ndi zochita za Anikolai, zimene Inenso ndimadana nazo.
Lakini bhebhe ujhe ni ele, ghwidada ghala ambagho Bhanikolai bhaghabhombili, ambagho hata ni ghadadili.
7 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wakudya zipatso za mtengo wopatsa moyo umene uli ku paradizo wa Mulungu.
Kama ujhe ni mb'olokoto, pelekesiajhi ghala ambagho Roho akaghajobhela makanisa. Na jhaibeta kushinda nibeta kumpela kibali kya kulya kuhoma mu libehe lya uzima lyajhele mu Paradiso jha K'yara.'
8 “Lembera mngelo wa mpingo wa ku Simurna kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi Woyamba ndi Wotsiriza, amene anafa nʼkukhalanso ndi moyo.
“Kwa malaika bha kanisa lya Smirna jhandikayi: 'Agha ndo malobhi gha jhola. ambajhe ndo mwanzo ni mwishu ambajhe afuili ni kujha hai kabhele:
9 Ine ndimadziwa masautso ako ndi umphawi wako, chonsecho ndiwe wolemera! Ndikudziwa zimene amakusinjirira anthu amene amati ndi Ayuda pamene sizili choncho, koma ndi a mpingo wa Satana.
“Nimanyili malombosi ghako ni umaskini bhwa jhobhi (lakini bhebhe ndo tajiri), ni udesi bhwa bhala bhabhikikuta bhayahudi (lakini lepi - bhene ndo sinagogi lya syetani).
10 Musachite mantha ndi zimene muti musauke nazo posachedwapa. Ndithu, Satana adzayika ena a inu mʼndende pofuna kukuyesani, ndipo mudzazunzika kwa masiku khumi. Khalani okhulupirika ngakhale zitafika pa imfa, ndipo Ine ndidzakupatsani chipewa cha ulemerero wamoyo.
Usitili malombosi ghaghibeta kukabha. Langayi! Ibilisi ilonda kubhatagha baadhi jha muenga muligereza ili mubhwesiajhi kujaribibhwa, na mwibeta kutesibhwa kwa magono kumi. Mujhelayi mwebhaaminifu hadi kufwa, na nibeta kubhapela taji jha uzima.
11 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana sadzapwetekedwa ndi pangʼono pomwe ndi imfa yachiwiri.
Kama ujhe ni mb'olokoto, pelekesiajhi Roho kyaakaghajobhela makanisa. Muene jha ibeta kushinda ibetalepi kukabha mauti gha pili.'
12 “Lembera mngelo wa mpingo wa ku Pergamo kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi lupanga lakuthwa konsekonse.
Kwa malaika bha kanisa lya Pergamo jhandikayi: 'Agha ndo ghaijobha muene jhaajhe ni upanga obhu mkali, bhwabhujhe ni makali kubhele.
13 Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa kumene mumakhala, kumene kuli mpando waufumu wa Satana. Komabe inu ndinu okhulupirika kwa Ine. Simunataye chikhulupiriro chanu pa Ine, ngakhale mʼmasiku a Antipa, mboni yanga yokhulupirika, amene anaphedwa mu mzinda wanu, kumene amakhala Satana.
“Nimanyili mahali paghwitama mahali pa kijhele kiti kya enzi kya shetani. Hata naha bhebhe ulikamuili sana lihina lya nene, na ghwajhibelili lepi imani jha jhobhi jhaijhele kwa nene hata magono ghala gha Antipasi shahidi ghwa nene, mwaminifu ghwa nene, jhaakhomibhu miongoni mwa jhomu, apu ndo syetani itama.
14 Komabe, ndili ndi zinthu zingapo zotsutsana nanu. Kumeneko muli ndi anthu ena amene amatsata ziphunzitso za Balaamu, uja amene anaphunzitsa Baraki kukopa Aisraeli kuti azidya nsembe zoperekedwa ku mafano ndi kumachita chigololo.
Lakini nijheni mambo madebe dhidi jha bhebhe: ujhe nabhu okhu bhanu bhabhikamula mafundisu gha Balaamu, muene jhaamfundisi Balaki kubheka fikwazo palongolo jha bhene bha Israeli ili bhaliajhi fyakulya fya fipisibhu sadaka kwa masieto ni kuzini.
15 Chimodzimodzinso inuyo muli ndi ena amene amatsatira ziphunzitso za Anikolai.
Mu hali ejhu hata bhebhe ujhe ni baadhi jha bhene bhikamula mafundisu gha Bhanikolai.
16 Tsono tembenukani mtima. Mukapanda kutero, ndidzabwera kwanuko posachedwa ndipo ndidzachita nanu nkhondo ndi lupanga lotuluka mʼkamwa mwanga lija.
Basi tubuajhi! Na ubelili kukheta naha, nihida manyata, na nibeta kukheta vita dhidi jha bhene kwa upanga bhwa bhwihomela mu kinywa kya nene.
17 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Kwa amene adzapambane ndidzamupatsa chakudya chobisika cha mana. Ndidzamupatsanso mwala woyera wolembedwapo dzina latsopano, lodziwa iye yekha amene walandirayo.’”
Kama ujhe ni mb'olokoto, pelekesiajhi Roho kya ikabhajobhela makanisa. Muene jha ibeta kushinda nibeta kumpela baadhi jha jhela mana jhajhafighibhu, kabhele nibeta kumpela liganga libhalabhu lya litembibhu lihina lipya panani pa liganga, lihina ambalya ajhelepi jha alimanyili isipokujha muene jhaakalipokela.'
18 “Lembera mngelo wampingo wa ku Tiyatira kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa Mwana wa Mulungu, amene maso ake ali ngati moto woyaka ndi mapazi ake ngati chitsulo chonyezimira.
Kwa malaika bha kanisa lya Thiatira jhandikayi: “Agha ndo malobhi gha mwana ghwa K'yara, muene jha ajhe ni mihu gha muene kama mwali ghwa muoto, ni jhayu kama shaba jhajhisugulibhu nasu:
19 Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zanu, chikondi chanu ndi chikhulupiriro chanu, kutumikira kwanu ndi kupirira kwanu. Ndikudziwa tsopano kuti ntchito zanu ndi zabwino kuposa zoyamba zija.
Nimanyili gha ubhombili - upendo bhwa jhobhi ni imani ni huduma ni uvumilivu bhwa jhobhi thabiti, ni kujha khela kya ukhetili naha karibuni ndo zaidi jha khela kya abhombili kubhuandu.
20 Komabe ndili ndi chinthu chokudzudzula nacho. Umamulekerera mkazi uja Yezebeli amene amadzitcha yekha kuti ndi mneneri. Iye amaphunzitsa atumiki anga kuti azichita zadama ndi kumadya zansembe zoperekedwa ku mafano.
Lakini nijhe ni e'le dhidi jha bhebhe: ukamvumilila n'dala Yezebeli jhaikikuta muene nabii n'dala. Kwa mafundisu gha muene, akabhapotosya bhatumishi bha nene kuzini ni kulya kyakulya kya kipisibhu sadaka kwa sanamu.
21 Ndamupatsa nthawi kuti aleke zachigololo zake koma sakufuna.
Nampelili muda bhwa kutubu, lakini ajhelepi tayari kutubila uovu bhwa muene.
22 Tsono ndidzamugwetsa mʼmasautso ndipo amene amachita naye zadama zakezo ndidzawasautsa kwambiri akapanda kulapa ndi kuleka njira za mkaziyo.
Langayi! Nibetakun'tagha mu kitanda kya maradhi, ni bhala bhabhibhomba uasherati naku mu malombosi makali, vinginevyo bhatubuajhi kwa kyabhakhetili.
23 Ana ake ndidzawakantha ndi kuwapheratu. Kotero mipingo yonse idzadziwa kuti Ine ndine uja amene ndimafufuza mʼmitima mwa anthu ndi mʼmaganizo mwawo. Aliyense wa inu ndidzachita naye monga mwa ntchito zake.
Nibeta kubhatobha bhana bhabhi bhafuajhi ni makanisa ghoha ghibetakumanya nene ndo nikaghalangilila mawazo ni tamaa. Nibeta kumpela khila mmonga bhinu kadri jha matendo gha muene.
24 Tsopano ndikunena kwa enanu a ku Tiyatira, kwa inu amene simunatsate chiphunzitso cha mkaziyo ndipo simunaphunzire zimene iwo amati ndi ‘zinsinsi zonama’ za Satana. Kwa inu mawu anga ndi akuti sindikuwunjikirani malamulo ena.
Lakini kwa baadhi jha muenga jhamubakili mu Thiatira, kwa bhala mwebhoha jha mkamuili lepi lifundisu e'le, na jha mumanyilepi khela ambakyo baadhi bhikuta mafumbo gha shetani, nijobha kwa muenga, 'Nibeta lepi kubheka kwa muenga n'sighu ghoghuoha ghola.'
25 Inu mungogwiritsa zimene munaphunzira basi, mpaka Ine ndidzabwere.
Kwa lijambo lyolyoha, lazima mujhelayi imara mpaka panibeta kuhida.
26 Amene adzapambana ndi kuchita chifuniro changa mpaka kumapeto, ndidzamupatsa ulamuliro pa mitundu yonse ya anthu.
Jhejhioha jhaibeta kushinda ni kubhomba khela kya nibhomba I mpaka kumwisu, muene nibeta kumpela mamlaka panani pa mataifa.
27 Adzayilamulira ndi ndodo yachitsulo ndipo nadzayiphwanyaphwanya ngati mbiya. Ulamuliro umenewu ndi omwe ndinalandira kwa Atate anga.
'Ibetakubhatawala kwa ndongo jha chuma, kama makaburi gha udongo, ibetakubhatenya fipandi.'
28 Ine ndidzamupatsanso nthanda, nyenyezi yowala mʼmamawa ija.
Kama kyanipokili kuhoma kwa Dadi jhangu, nibeta kumpela kabhele litondo lya lukhela.
29 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.
Ukajhelayi ni mb'olokoto, pelekesiajhi khela ambakyo Roho akaghajobhela makanisa.'

< Chivumbulutso 2 >