< Chivumbulutso 2 >

1 “Lembera mngelo wa mpingo wa ku Efeso kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri zija mʼdzanja lake lamanja amene akuyenda pakati pa zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide.
"To the angel of the church in Ephesus write: "He who holds the seven stars in his right hand, he who walks among the seven golden lampstands says these things:
2 Ine ndimadziwa zochita zako, ntchito yako yowawa ndi kupirira kwako. Ine ndimadziwa kuti sungalekerere anthu oyipa amene amadzitcha atumwi pamene sichoncho, unawayesa, ndipo unawapeza kuti ndi abodza.
"I know your works, and your toil and perseverance, and that you cannot tolerate those who are evil, and have tested those who call themselves apostles, and they are not, and found them false.
3 Iwe wapirira ndipo wakumana ndi zovuta chifukwa cha dzina langa, ndipo sunatope.
You have perseverance and have endured for my name's sake, and have not grown weary.
4 Komabe ndili ndi chotsutsana nawe: Wataya chikondi chako chapoyamba.
But I have this against you, that you left your first love.
5 Kumbukirani kuti munagwa kuchokera patali. Lapa ndikuchita zinthu zimene unkachita poyamba. Ngati sulapa ndidzabwera ndikukuchotsera choyikapo nyale chako pamalo pake.
Remember therefore from where you have fallen, and repent and do the first works; or else I am coming to you, and will move your lampstand out of its place, unless you repent.
6 Komabe chokomera chako ndi chakuti umadana ndi zochita za Anikolai, zimene Inenso ndimadana nazo.
But this you have, that you hate the works of the Nicolaitans, which I also hate.
7 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wakudya zipatso za mtengo wopatsa moyo umene uli ku paradizo wa Mulungu.
He who has an ear, let him hear what the Spirit says to the churches. To him who overcomes I will give to eat of the tree of life, which is in the Paradise of God.
8 “Lembera mngelo wa mpingo wa ku Simurna kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi Woyamba ndi Wotsiriza, amene anafa nʼkukhalanso ndi moyo.
"To the angel of the church in Smyrna write: "The first and the last, who was dead, and has come to life says these things:
9 Ine ndimadziwa masautso ako ndi umphawi wako, chonsecho ndiwe wolemera! Ndikudziwa zimene amakusinjirira anthu amene amati ndi Ayuda pamene sizili choncho, koma ndi a mpingo wa Satana.
"I know your tribulation and your poverty (but you are rich), and the blasphemy of those who say they are Jews, and they are not, but are a synagogue of Satan.
10 Musachite mantha ndi zimene muti musauke nazo posachedwapa. Ndithu, Satana adzayika ena a inu mʼndende pofuna kukuyesani, ndipo mudzazunzika kwa masiku khumi. Khalani okhulupirika ngakhale zitafika pa imfa, ndipo Ine ndidzakupatsani chipewa cha ulemerero wamoyo.
Do not be afraid of the things which you are about to suffer. Look, the devil is about to throw some of you into prison, that you may be tested; and you will have oppression for ten days. Be faithful until death, and I will give you the crown of life.
11 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana sadzapwetekedwa ndi pangʼono pomwe ndi imfa yachiwiri.
He who has an ear, let him hear what the Spirit says to the churches. He who overcomes won't be harmed by the second death.
12 “Lembera mngelo wa mpingo wa ku Pergamo kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi lupanga lakuthwa konsekonse.
"To the angel of the church in Pergamum write: "He who has the sharp two-edged sword says these things:
13 Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa kumene mumakhala, kumene kuli mpando waufumu wa Satana. Komabe inu ndinu okhulupirika kwa Ine. Simunataye chikhulupiriro chanu pa Ine, ngakhale mʼmasiku a Antipa, mboni yanga yokhulupirika, amene anaphedwa mu mzinda wanu, kumene amakhala Satana.
"I know where you dwell, where Satan's throne is. You hold firmly to my name, and did not deny my faith even in the days of Antipas, my witness, my faithful one, who was killed among you, where Satan dwells.
14 Komabe, ndili ndi zinthu zingapo zotsutsana nanu. Kumeneko muli ndi anthu ena amene amatsata ziphunzitso za Balaamu, uja amene anaphunzitsa Baraki kukopa Aisraeli kuti azidya nsembe zoperekedwa ku mafano ndi kumachita chigololo.
But I have a few things against you, because you have there some who hold the teaching of Balaam, who taught Balak to throw a stumbling block before the children of Israel, to eat things sacrificed to idols, and to commit sexual immorality.
15 Chimodzimodzinso inuyo muli ndi ena amene amatsatira ziphunzitso za Anikolai.
So you also have some who hold to the teaching of the Nicolaitans likewise.
16 Tsono tembenukani mtima. Mukapanda kutero, ndidzabwera kwanuko posachedwa ndipo ndidzachita nanu nkhondo ndi lupanga lotuluka mʼkamwa mwanga lija.
Repent therefore, or else I am coming to you quickly, and I will make war against them with the sword of my mouth.
17 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Kwa amene adzapambane ndidzamupatsa chakudya chobisika cha mana. Ndidzamupatsanso mwala woyera wolembedwapo dzina latsopano, lodziwa iye yekha amene walandirayo.’”
He who has an ear, let him hear what the Spirit says to the churches. To him who overcomes, to him I will give of the hidden manna, and I will give him a white stone, and on the stone a new name written, which no one knows but he who receives it.
18 “Lembera mngelo wampingo wa ku Tiyatira kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa Mwana wa Mulungu, amene maso ake ali ngati moto woyaka ndi mapazi ake ngati chitsulo chonyezimira.
"To the angel of the church in Thyatira write: "The Son of God, who has his eyes like a flame of fire, and his feet are like burnished bronze, says these things:
19 Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zanu, chikondi chanu ndi chikhulupiriro chanu, kutumikira kwanu ndi kupirira kwanu. Ndikudziwa tsopano kuti ntchito zanu ndi zabwino kuposa zoyamba zija.
"I know your works, your love, faith, service, patient endurance, and that your last works are more than the first.
20 Komabe ndili ndi chinthu chokudzudzula nacho. Umamulekerera mkazi uja Yezebeli amene amadzitcha yekha kuti ndi mneneri. Iye amaphunzitsa atumiki anga kuti azichita zadama ndi kumadya zansembe zoperekedwa ku mafano.
But I have this against you, that you tolerate the woman, Jezebel, who calls herself a prophetess. She teaches and seduces my servants to commit sexual immorality, and to eat things sacrificed to idols.
21 Ndamupatsa nthawi kuti aleke zachigololo zake koma sakufuna.
I gave her time to repent, but she refuses to repent of her sexual immorality.
22 Tsono ndidzamugwetsa mʼmasautso ndipo amene amachita naye zadama zakezo ndidzawasautsa kwambiri akapanda kulapa ndi kuleka njira za mkaziyo.
Look, I will throw her into a sickbed, and those who commit adultery with her into great oppression, unless they repent of her works.
23 Ana ake ndidzawakantha ndi kuwapheratu. Kotero mipingo yonse idzadziwa kuti Ine ndine uja amene ndimafufuza mʼmitima mwa anthu ndi mʼmaganizo mwawo. Aliyense wa inu ndidzachita naye monga mwa ntchito zake.
I will kill her children with Death, and all the churches will know that I am he who searches the minds and hearts. I will give to each one of you according to your deeds.
24 Tsopano ndikunena kwa enanu a ku Tiyatira, kwa inu amene simunatsate chiphunzitso cha mkaziyo ndipo simunaphunzire zimene iwo amati ndi ‘zinsinsi zonama’ za Satana. Kwa inu mawu anga ndi akuti sindikuwunjikirani malamulo ena.
But to you I say, to the rest who are in Thyatira, as many as do not have this teaching, who do not know what some call 'the deep things of Satan,' to you I say, I am not putting any other burden on you.
25 Inu mungogwiritsa zimene munaphunzira basi, mpaka Ine ndidzabwere.
Nevertheless, hold that which you have firmly until I come.
26 Amene adzapambana ndi kuchita chifuniro changa mpaka kumapeto, ndidzamupatsa ulamuliro pa mitundu yonse ya anthu.
He who overcomes, and he who keeps my works to the end, to him I will give authority over the nations.
27 Adzayilamulira ndi ndodo yachitsulo ndipo nadzayiphwanyaphwanya ngati mbiya. Ulamuliro umenewu ndi omwe ndinalandira kwa Atate anga.
He will rule them with an iron scepter, shattering them like clay pots; as I also have received of my Father:
28 Ine ndidzamupatsanso nthanda, nyenyezi yowala mʼmamawa ija.
and I will give him the morning star.
29 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.
He who has an ear, let him hear what the Spirit says to the churches.

< Chivumbulutso 2 >