< Chivumbulutso 2 >
1 “Lembera mngelo wa mpingo wa ku Efeso kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri zija mʼdzanja lake lamanja amene akuyenda pakati pa zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide.
Andělu Efezské církve piš: Totoť praví ten, kterýž drží těch sedm hvězd v pravici své, jenž se prochází uprostřed těch sedmi svícnů zlatých:
2 Ine ndimadziwa zochita zako, ntchito yako yowawa ndi kupirira kwako. Ine ndimadziwa kuti sungalekerere anthu oyipa amene amadzitcha atumwi pamene sichoncho, unawayesa, ndipo unawapeza kuti ndi abodza.
Známť skutky tvé, a práci tvou, i trpělivost tvou, a že nemůžeš trpěti zlých; a zkusil jsi těch, kteříž se praví býti apoštolé, ale nejsou, a shledals je, že jsou lháři.
3 Iwe wapirira ndipo wakumana ndi zovuta chifukwa cha dzina langa, ndipo sunatope.
A snášel jsi, a trpělivost máš, a pro jméno mé pracovals a neustal.
4 Komabe ndili ndi chotsutsana nawe: Wataya chikondi chako chapoyamba.
Ale mámť něco proti tobě, totiž že jsi tu první lásku svou opustil.
5 Kumbukirani kuti munagwa kuchokera patali. Lapa ndikuchita zinthu zimene unkachita poyamba. Ngati sulapa ndidzabwera ndikukuchotsera choyikapo nyale chako pamalo pake.
Protož pomni, odkud jsi vypadl, a čiň pokání a první skutky čiň. Pakliť toho nebude, přijdu na tebe rychle a pohnuť svícnem tvým z místa jeho, nebudeš-li pokání činiti.
6 Komabe chokomera chako ndi chakuti umadana ndi zochita za Anikolai, zimene Inenso ndimadana nazo.
Ale toto dobré do sebe máš, že nenávidíš skutků Mikulášenské roty, kterýchž i já nenávidím.
7 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wakudya zipatso za mtengo wopatsa moyo umene uli ku paradizo wa Mulungu.
Kdo má uši, slyš, co Duch praví církvím: Tomu, kdož zvítězí, dám jísti z dřeva života, kteréž jest uprostřed ráje Božího.
8 “Lembera mngelo wa mpingo wa ku Simurna kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi Woyamba ndi Wotsiriza, amene anafa nʼkukhalanso ndi moyo.
Andělu pak Smyrnenské církve piš: Toto praví ten první i poslední, kterýž byl mrtvý, a ožil:
9 Ine ndimadziwa masautso ako ndi umphawi wako, chonsecho ndiwe wolemera! Ndikudziwa zimene amakusinjirira anthu amene amati ndi Ayuda pamene sizili choncho, koma ndi a mpingo wa Satana.
Vím o skutcích tvých, i o soužení, a chudobě tvé, (ale bohatý jsi), i o rouhání těch, kteříž se praví býti Židé, a nejsou, ale jsou sběř satanova.
10 Musachite mantha ndi zimene muti musauke nazo posachedwapa. Ndithu, Satana adzayika ena a inu mʼndende pofuna kukuyesani, ndipo mudzazunzika kwa masiku khumi. Khalani okhulupirika ngakhale zitafika pa imfa, ndipo Ine ndidzakupatsani chipewa cha ulemerero wamoyo.
Nebojž se nic toho, co trpěti máš. Aj, uvržeť ďábel některé z vás do vězení, abyste zkušeni byli, a budete míti úzkost za deset dní. Budiž věrný až do smrti, a dámť korunu života.
11 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Amene adzapambana sadzapwetekedwa ndi pangʼono pomwe ndi imfa yachiwiri.
Kdo má uši, slyš, co Duch praví církvím: Kdo zvítězí, nebude uražen od smrti druhé.
12 “Lembera mngelo wa mpingo wa ku Pergamo kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ali ndi lupanga lakuthwa konsekonse.
Andělu pak Pergamenské církve piš: Totoť praví ten, kterýž má ten meč s obou stran ostrý:
13 Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa kumene mumakhala, kumene kuli mpando waufumu wa Satana. Komabe inu ndinu okhulupirika kwa Ine. Simunataye chikhulupiriro chanu pa Ine, ngakhale mʼmasiku a Antipa, mboni yanga yokhulupirika, amene anaphedwa mu mzinda wanu, kumene amakhala Satana.
Vím skutky tvé, i kde bydlíš, totiž tu, kdež jest stolice satanova, a že držíš se jména mého, a nezapřel jsi víry mé, ani v těch dnech, když Antipas, svědek můj věrný, zamordován jest u vás, tu, kdež bydlí satan.
14 Komabe, ndili ndi zinthu zingapo zotsutsana nanu. Kumeneko muli ndi anthu ena amene amatsata ziphunzitso za Balaamu, uja amene anaphunzitsa Baraki kukopa Aisraeli kuti azidya nsembe zoperekedwa ku mafano ndi kumachita chigololo.
Ale mámť proti tobě něco málo, že tam máš ty, kteříž drží učení Balámovo, jenž učil Baláka pohoršení klásti před obličejem synů Izraelských, aby jedli modlám obětované a smilnili.
15 Chimodzimodzinso inuyo muli ndi ena amene amatsatira ziphunzitso za Anikolai.
Tak i ty máš některé, kteříž drží učení Mikulášenců, což já v nenávisti mám.
16 Tsono tembenukani mtima. Mukapanda kutero, ndidzabwera kwanuko posachedwa ndipo ndidzachita nanu nkhondo ndi lupanga lotuluka mʼkamwa mwanga lija.
Èiniž pokání. Pakli nebudeš, přijdu na tebe brzy, a bojovatiť budu s nimi mečem úst svých.
17 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo. Kwa amene adzapambane ndidzamupatsa chakudya chobisika cha mana. Ndidzamupatsanso mwala woyera wolembedwapo dzina latsopano, lodziwa iye yekha amene walandirayo.’”
Kdo má uši, slyšiž, co Duch praví církvím: Tomu, jenž vítězí, dám jísti mannu skrytou a dám jemu kamének bílý, a na tom kaménku jméno nové napsané, kteréhož žádný neví, než ten, kdož je přijímá.
18 “Lembera mngelo wampingo wa ku Tiyatira kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa Mwana wa Mulungu, amene maso ake ali ngati moto woyaka ndi mapazi ake ngati chitsulo chonyezimira.
Andělu pak Tyatirské církve piš: Totoť praví Syn Boží, jenž má oči jako plamen ohně, a nohy jeho podobné jsou mosazi:
19 Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zanu, chikondi chanu ndi chikhulupiriro chanu, kutumikira kwanu ndi kupirira kwanu. Ndikudziwa tsopano kuti ntchito zanu ndi zabwino kuposa zoyamba zija.
Známť skutky tvé, i lásku, i přisluhování, i věrnost, i trpělivost tvou, a skutky tvé, i ty poslední, kteříž větší jsou nežli první.
20 Komabe ndili ndi chinthu chokudzudzula nacho. Umamulekerera mkazi uja Yezebeli amene amadzitcha yekha kuti ndi mneneri. Iye amaphunzitsa atumiki anga kuti azichita zadama ndi kumadya zansembe zoperekedwa ku mafano.
Ale mámť proti tobě něco málo, že dopouštíš ženě Jezábel, kteráž se býti praví prorokyní, učiti a v blud uvoditi služebníky mé, aby smilnili a jedli modlám obětované.
21 Ndamupatsa nthawi kuti aleke zachigololo zake koma sakufuna.
Ale dalť jsem jí čas, aby pokání činila z smilstva svého, avšak nečinila pokání.
22 Tsono ndidzamugwetsa mʼmasautso ndipo amene amachita naye zadama zakezo ndidzawasautsa kwambiri akapanda kulapa ndi kuleka njira za mkaziyo.
Aj, já uvrhu ji na lože, i ty, kteříž cizoloží s ní, v soužení převeliké, jestliže nebudou činiti pokání z skutků svých.
23 Ana ake ndidzawakantha ndi kuwapheratu. Kotero mipingo yonse idzadziwa kuti Ine ndine uja amene ndimafufuza mʼmitima mwa anthu ndi mʼmaganizo mwawo. Aliyense wa inu ndidzachita naye monga mwa ntchito zake.
A syny její zmorduji smrtí; i zvědíť všecky církve, žeť jsem já ten, kterýž zpytuji ledví a srdce, a odplatím jednomu každému z vás podle skutků vašich.
24 Tsopano ndikunena kwa enanu a ku Tiyatira, kwa inu amene simunatsate chiphunzitso cha mkaziyo ndipo simunaphunzire zimene iwo amati ndi ‘zinsinsi zonama’ za Satana. Kwa inu mawu anga ndi akuti sindikuwunjikirani malamulo ena.
Vámť pak pravím i jiným Tyatirským, kteřížkoli nemají učení tohoto, a kteříž nepoznali hlubokosti satanovy, jakž oni říkají: Nevzložímť na vás jiného břemene.
25 Inu mungogwiritsa zimene munaphunzira basi, mpaka Ine ndidzabwere.
Avšak to, což máte, držte, dokavadž nepřijdu.
26 Amene adzapambana ndi kuchita chifuniro changa mpaka kumapeto, ndidzamupatsa ulamuliro pa mitundu yonse ya anthu.
Kdož by pak vítězil a ostříhal až do konce skutků mých, dám jemu moc nad pohany.
27 Adzayilamulira ndi ndodo yachitsulo ndipo nadzayiphwanyaphwanya ngati mbiya. Ulamuliro umenewu ndi omwe ndinalandira kwa Atate anga.
I budeť je spravovati prutem železným, a jako nádoba hrnčířova střískáni budou, jakž i já vzal jsem od Otce svého.
28 Ine ndidzamupatsanso nthanda, nyenyezi yowala mʼmamawa ija.
A dám jemu hvězdu jitřní.
29 Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.
Kdo má uši, slyš, co Duch praví církvím.