< Chivumbulutso 19 >
1 Zitatha izi, ndinamva chimene chinamveka ngati phokoso la gulu lalikulu mmwamba likufuwula kuti, “Haleluya! Chipulumutso ndi ulemerero ndi mphamvu ndi za Mulungu wathu,
Pamekakila nanso nikija luli anga mulilo ukulu niiumbe nikulu laantu kilunde ekalunga ilumbi, Uuguni ukulu, ningulu inge yang'wi Tunda witu.
2 pakuti chiweruzo chake ndi choona ndi cha chilungamo. Iye waweruza mkazi wadama wotchuka uja amene anayipitsa dziko lonse lapansi ndi zigololo zake. Iye wabwezera pa mkaziyo magazi a atumiki ake.”
Ulamuli wakwe watai lukulu, kunsoko wamulamula umukosi numukulu numubipiye ihe kugooli wakwe. Witumile kilipo kusakami aitumi akwe, naeumihunue ung'wenso.
3 Ndipo anafuwulanso kuti, “Haleluya! Utsi wochokera kwa mkazi wadamayo udzakwera kumwamba mpaka muyaya.” (aiōn )
Kunkua akabiile, ikalunga “Ilumbi! Ulyoki lepuma kung'wake ikale na kale.” (aiōn )
4 Akuluakulu 24 aja ndi zamoyo zinayi zija anadzigwetsa pansi kupembedza Mulungu amene anakhala pa mpando waufumu. Ndipo anafuwula kuti, “Ameni, Haleluya!”
Ianyampala ao makumi abiile nuunne nimaintu anne nuupanga ikaluma nukukulya Itunda nuikie mituntunlautemi. Aeakulunga, Hueli, Ilumbi!
5 Kenaka mawu anachoka ku mpando waufumu kuti, “Lemekezani Mulungu wathu inu nonse atumiki ake, inu amene mumamuopa, nonse angʼono ndi akulu!”
Papo ululi likapuma mituntu lautemi, ikalunga “Mukulye Itunda witu unye itumi akwe mihe, unye nimuze mekua, ihe niagila umuhimu naaniagila ingulu.”
6 Kenaka ndinamva chimene chinamveka ngati gulu lalikulu, ngati mkokomo wamadzi othamanga ndipo ngati kugunda kwakukulu kwa bingu, ndipo anati, “Haleluya! Pakuti Ambuye Mulungu wathu Wamphamvuzonse akulamulira.
Papo nikija ululi anga luli liumbe nikulu nilaantu, anga loli lamugugumo nuamaze nedu, hangi anga mugugumo walupito ikalunga, “Ilumbi!” Mkulu Itunda witu, mutemi waawa ehi, nuezutemile.
7 Tiyeni tisangalale ndi kukondwera ndi kumutamanda! Pakuti nthawi ya ukwati wa Mwana Wankhosa yafika, ndipo Mkwatibwi wakonzekeratu.
Nukulumbiye nukuolowa nukumupa ukulu kunsoko awinga nuuli wang'wankolo wazaa, nubibi wawinga ukondile.
8 Wapatsidwa nsalu yoyera kwambiri, yowala ndi yosada kuti avale.” (Nsalu yoyera kwambiri ikuyimira ntchito zolungama za oyera mtima).
Wikagombigwa kutugalwa kitani nikiza nikekumetameta kitani nikiza igebge ntendo niyatai lukulu niyauhueli.
9 Kenaka mngelo anandiwuza kuti, “Lemba kuti, Odala amene ayitanidwa ku phwando la ukwati wa Mwana Wankhosa.” Ndipo anatinso, “Awa ndiwo mawu woona a Mulungu.”
Umalaika wikatambula unene, “Maandike aya: Akembetilwe nianilwe kuwenga wang'wa nkolo.” Kuu uwu wikambila, “Izi nkani yatai nang'wi Tunda.
10 Pamenepo ndinadzigwetsa pa mapazi ake kumupembedza. Koma anandiwuza kuti, “Usatero ayi, ine ndine mtumiki mnzako ngati iwe yemwe, ndiponso ngati abale ako amene asunga umboni wa Yesu. Pembedza Mulungu. Pakuti umboni wa Yesu ndiye mzimu wa uneneri.”
Aentunile ntongeela amigulu akwe nikakulya. Kuite wikambila, “Uleke kutenda ite! Une numitumi miako nualuna ako nuambile uwihengi nuang'wa Yesu mukulye Itunda, kunsoko uwihengi nuang'wa Yesu nkolo akinyakidagu.”
11 Ndinaona kumwamba kutatsekuka ndipo patsogolo panga panali kavalo woyera, amene anakwerapo dzina lake linali Wokhulupirika ndiponso Woona. Poweruza ndi kuchita nkhondo, amachita molungama.
Hangi nikaona ilunde lakaluguka, hange goza yekatula ukoli farasi nzelu! Nuyu nai umunankie aeukitangwa muhueli hange watai. Lamula itai nukituma embita.
12 Maso ake anali ngati malawi amoto, ndipo pamutu pake panali zipewa zaufumu zambiri. Anali ndi dzina lolembedwa, lodziwika ndi Iye yekha, osati wina aliyense.
Imiho akwe anga ululeme lamoto, numigulya itwe lakwe ukete ngala yedu. Ukete lina nilaandekilwe migulya akwe nusholimanyile muntu wehi inge ung'wenso duu.
13 Iye anavala mkanjo woviyika mʼmagazi, ndipo dzina lake ndi Mawu a Mulungu.
Utugae ng'wenda nunimikilwe musakami nilina lakwe aaukitangwa lukani lang'wi Tunda.
14 Magulu ankhondo akumwamba ankamutsatira atakwera pa akavalo oyera, ndipo iwowo atavala nsalu zoyera kwambiri ndi zosada.
Imajeshi akilunde ae amutyatie migulya afarasi ninzelu, aeatugawe kitani ninza, nzelu hange nza.
15 Mʼkamwa mwake munatuluka lupanga lakuthwa limene anati akaphe nalo mitundu ya anthu. Iye adzalamulira ndi ndodo yachitsulo. Iye anaponda choponderamo mphesa cha ukali wa Mulungu Wamphamvuzonse.
Mumulomo wakwe kepuma shege nikitaki nikelima nsilya imahe, nung'wenso wikamusunga kumulanga, kekuo nitaki kung'wi Tunda, wizutemile migulya nihe.
16 Pa chovala ndi pa ntchafu pake panalembedwa dzina ili: MFUMU YA MAFUMU NDI MBUYE WA AMBUYE.
Nung'wenso uandekilwe migulya lang'wenda wakwe numukinama kakwe lina. MUTEMI WA ATEMI HANGI MUKULU WAAKULU.
17 Ndipo ndinaona mngelo atayimirira pa dzuwa amene anafuwula ndi mawu okweza kwa mbalame zonse zowuluka mlengalenga kuti, “Bwerani, sonkhanani pamodzi ku phwando lalikulu la Mulungu.
Aemine malaeka akeze wimekile mulyoa. Auitangile kululi nulukulu inyonyi yehi niyeluma migulya, “Nzii ilingeeli mehi palung'we paludya nulukulu nulang'wi Tunda.
18 Kuti mudye mnofu wa mafumu, wa akulu a ankhondo, ndi wa anthu amphamvu, wa akavalo ndi okwerapo awo, ndi wa anthu onse, mfulu ndi akapolo, angʼono ndi aakulu.”
Nzii muliye inyama amutemi, nyama ajemedali, nyama aantu niakulu, nyama afalasi nianankila falasi hange nyama aantu ehi, neidesile niatugwa, niagila umuhimu nawaniagila ingulu.”
19 Kenaka ndinaona chirombo chija ndi mafumu a dziko lapansi ndi magulu ankhondo atasonkhana pamodzi kuti achite nkhondo ndi wokwera pa kavalo ndi ankhondo ake.
Ainekeine ikekale niatemi ihe palungwi nimajeshi ao. Aeipangile kunsoko ambita hange ung'wi naunankie efalasi nijeshi lakwe.
20 Koma chirombocho chinagwidwa pamodzi ndi mneneri wonyenga uja amene anachita zizindikiro zodabwitsa pamaso pake. Ndi zizindikirozi anasocheretsa amene analembedwa chizindikiro cha chirombocho napembedza fano lake. Onse awiri anaponyedwa amoyo mʼnyanja yamoto yasulufule wotentha. (Limnē Pyr )
Ikekale kekaambwa numunya kidagu wakwe nuauteele naiwigeeye ilingasilyo muugole wakwe kuilingasilya auakongee awa niasigeeye ugomola wakikali nawa naiakuiye ududu wakwe. Ehi muubiile akagung'wa akizeapanga milule la moto nuakiigwe nikibiliti. (Limnē Pyr )
21 Ena onse anaphedwa ndi lupanga lija linatuluka mʼkamwa mwa wokwera pa kavalo uja, ndipo mbalame zonse zinadya mokwanira mnofu wa anthu akufawo.
Awa naeasigile akabulagwa neshege naikipumile kumulomo wang'wa ung'wi wao naunankie migulya la falasi. Inyunyi yehi aiilie imeimba namiile ao.