< Chivumbulutso 18 >

1 Zitatha izi ndinaona mngelo wina akutsika kuchokera kumwamba. Iye anali ndi ulamuliro waukulu, ndipo dziko lapansi linawala ndi ulemerero.
Amalalu, na da a: igele dunu Hebene soge yolesili, osoboga manebe ba: i. E da hina bagade agoane ba: i. Ea hadigi da osobo bagade huluane hadigi hamoi.
2 Mngeloyo anafuwula ndi mawu amphamvu kuti: “‘Wagwa! Wagwa Babuloni Wamkulu!’ Wasandulika mokhalamo ziwanda ndi kofikako mizimu yonse yoyipa ndi mbalame zonse zonyansa ndi zodetsedwa.
E da ha: giwane wele sia: i, “Uda da dafai dagoi. Ba: bilone Bagade da dafai dagoi. Fio liligi amola nigima: a:silibu, amo fawane amo moilai bai bagade ganodini esala. Wadela: i ledo bagade sio fi hisu hisu da amo moilai bai bagade ganodini esala.
3 Pakuti mayiko onse amwa vinyo ozunguza mutu wazigololo zake. Mafumu a dziko lapansi achita naye chigololo, ndipo amalonda a dziko lapansi analemera kuchokera pa zolakalaka zake zosefukira.”
Bai dunu fifi asi gala huluane da fedege agoane amo ea wadela: i hanai hou gasa bagade waini hano mai dagoi. Osobo bagade ouligisu dunu da ema wadela: i uda lasu hou hamosu amola osobo bagade bidi lasu dunu da e gasa bagade wadela: i hou hanaiwane hamobeba: le, muni bagade lai.”
4 Ndiponso ndinamva mawu ena kuchokera kumwamba akuti: “‘Anthu anga tulukani, mwa iye,’ mungachimwe naye kuti musadzalandire nawo gawo lililonse la miliri yake;
Amalalu, na da sia: eno muagadodi misi amane nabi, “Na fi dunu! Ba: bilone moilai bai bagade yolesili, misa! Dilia da ea wadela: i hou gilisili mae hamoma! Dilia da ea se dabe iasu gilisili ba: mu da defea hame.
5 pakuti machimo ake awunjikana mpaka kumwamba, ndipo Mulungu wakumbukira milandu yake.
Bai ea wadela: i hou da gilisibiba: le, afae da afae da: iya ligisiba: le, Hebene sogega doaga: i. Gode da ea wadela: i hou hame gogolei.
6 Bwezerani Iye monga momwe iye anakuchitirani. Mubwezereni mowirikiza pa zimene anachita. Mumusakanizire magawo awiri kuchokera mʼchikho chake.
Ema dabema amola ea afadafa wadela: i hou hamoi galea, ema se dabe iasu amo defele aduna ima. E da se nabasu bagade iabeba: le, ema gasa bagadedafa baligiliwane dabe ima.
7 Mumuzunze, kumumvetsa chisoni kwambiri monga mwaulemerero ndi zolakalaka zimene anadzaza mu mtima mwake. Iye anadzikuza nʼkumati, ‘Ndinakhala monga mfumu yayikazi, ine sindine wamasiye ndipo sindidzalira maliro.’
E da hadigi amola liligi ida: iwane hi hanai liligi labeba: le, ema se nabasu amola da: i dioi, amo defele imunu da defea. Bai e da wali udigili amane sia: sa, “Na da didalo hame! Na da hina bagade uda agoane fi esala. Na da se nabasu hamedafa ba: mu!”
8 Chifukwa chake miliri yake idzamugonjetsa tsiku limodzi; imfa, kulira maliro ndi njala. Iye adzanyeka ndi moto pakuti wamphamvu ndi Mulungu Ambuye amene wamuweruza.
Amaiba: le, eso afadafa ganodini e da se bagade nabimu. Olosu, da: i dioi amola ha: su da ema doaga: mu. E da laluga nemu.
9 “Mafumu a dziko lapansi, amene anachita naye chigololo nachita naye pamodzi zosangalatsa moyo uno, akadzaona utsi wa kunyeka kwake, adzalira nakhuza maliro ake.
Osobo bagade hina bagade dunu amo da e amola gilisili wadela: le hamosu, ilia da amo moilai bai bagade laluga nenanebe ba: sea, bagadewane dimu.
10 Iwo adzayima kutali nalira chifukwa choopsedwa ndi mazunzo ake. “‘Tsoka! Tsoka mzinda waukulu iwe, Babuloni mzinda wamphamvu! Mu ora limodzi chiwonongeko chako chafika!’
Ilia da gilisili e se nabasu lasa: besa: le, sedagawane ba: lalawane lelumu. Ilia da amane sia: mu, “Ameia: ! Ameia: ! Ba: bilone bagade, moilai bai bagade ida: iwane galu. Eso afadafa ganodini di da se dabe iasu lai dagoiba: le dafai!”
11 “Amalonda a dziko lapansi adzalira nakhuza maliro ake chifukwa palibenso amene akugula katundu wawo,
Osobo bagade bidi lasu dunu amola da e dawa: le, dimu amola didiga: mu. Bai wali eno dunu da ilia liligi bu hame bidi laha.
12 katundu wagolide, siliva, miyala yamtengo wapamwamba ndi ngale; nsalu zoyera kwambiri zapamwamba ndi zofiira; nsalu zasilika ndi zapepo; mitengo iliyonse yonunkhira ndi zinthu zilizonse zopangidwa ndi mnyanga, kapena matabwa ogulidwa ndi ndalama zambiri kapena mkuwa kapena chitsulo ndi mwala wonyezimira;
Liligi huluane amo gouli, silifa, igi ida: iwane, su amola abula ida: iwane, liligi ida: iwane ifa, igi, ouli amola balase, amoga hamoi liligi,
13 zokometsera zakudya, mure, lubani ndi zofukiza zina, vinyo ndi mafuta a olivi, ufa wosalala ndi tirigu; ngʼombe ndi nkhosa; akavalo ndi ngolo; ndi anthu adzagulitsidwa ukapolo.
sinamone, hedama: ne fodole nasu liligi, gabusiga: manoma, fala: gisenese, waini hano, falaua, widi, bulamagau, sibi, hosi, sa: liode amola udigili hawa: hamosu dunu, amo huluane dunu eno da bu hame bidi lamuba: le, ilia da disa.
14 “Iwo adzanena kuti, ‘Chipatso chimene unachilakalaka chakuchokera. Chuma chako chonse ndi ulemerero zatha, sizidzapezekanso.’
Bidi lasu dunu da Ba: bilone amoma amane sia: sa, “Liligi ida: iwane gala di da lalegagumu hanai galu, amo da mugululi asi. Dia gagui amola ida: iwane ba: su da asi dagoi. Di da amo bu hamedafa ba: mu!”
15 Amalonda amene anagulitsa zinthu izi napeza chuma kuchokera kwa iye adzayima patali potero ataopsedwa ndi mazunzo ake. Adzalira ndi kukhuza maliro
Bidi lasu dunu, (amo da amo moilai bai bagadega bidi lasu hawa: hamobeba: le bagade gagui), ilia da ea se nabasu gilisili ba: sa: besa: le, sedagawane lelumu. Ilia da dimu amola didiga: mu.
16 ndipo adzalira mokuwa kuti, “‘Tsoka! Tsoka! Mzinda waukulu, iwe wovala nsalu zoyera kwambiri, zapepo ndi zofiira, ndi wonyezimira ndi golide, miyala yamtengo wapamwamba ndi ngale!
Ilia da amane sia: mu, “Ameia: ! Ameia: ! Moilai bai bagade da se bagade nabi. E da musa: abula ida: iwane amo yoi, oga: iyei amola gouli liligi amo lasu amola gifalo amoga sali.
17 Chuma chambiri choterechi chafika powonongeka mu ora limodzi!’ “Oyendetsa sitima ndi onse oyenda pa sitima ya pamadzi, ogwira ntchito mʼsitima ndi onse amene amadalira nyanja pamoyo wa tsiku ndi tsiku adzayima patali potero.
Be hedolodafa (aua afae agoane) e da amo liligi huluane yolesi dagoi. Dusagai ouligisu dunu, genonesisu dunu, dunu ilia amo ganodini ahoa amola dunu huluane ilia hano wayabo bagade amoga hawa: hamonanebeba: le esaloma: ne liligi laha, amo da sedagawane lelu,
18 Akadzaona utsi wa kunyeka kwake, adzakuwa kuti, ‘Kodi panalinso mzinda wina ngati mzinda waukuluwu?’
Ba: bilone nenanebeba: le lalu amola mobi, heda: lebe ba: loba, ilia amane wele sia: i, “Moilai bai bagade eno amo moilai bai bagade agoane da hamedafa ba: su.”
19 Adzathira fumbi pamitu pawo ndipo adzalira nakhuza maliro kuti, “Tsoka! Tsoka mzinda waukulu iwe, kumene onse anali ndi sitima pa nyanja analemera kudzera mʼchuma chake! Mu ora limodzi wawonongedwa.
Ilia da osobo gasa: le, ilisu dialuma da: iya ligisili, amane wele sia: i, “Ameia: ! Ba: bilone da se bagade nabi. Amo moilai bai bagade ganodini, dusagai hawa: hamosu dunu da muni bagade ba: i. Be hedolodafa (aua afae amoga) e da ea gagui huluane fisi dagoi!”
20 “Kondwerani chifukwa cha iye inu kumwamba! Kondwerani oyera mtima ndi atumwi ndi aneneri! Mulungu wamuweruza iye monga momwe anakuchitirani inu.”
Hebene ganodini fi! E da gugunufinisi dagoiba: le, hahawane nodoma! Gode Ea fi dunu, asunasi dunu amola balofede dunu! Dilia nodoma! Bai Ba: bilone da dilima wadela: le hamobeba: le, Gode da ema dabe i dagoi.
21 Kenaka mngelo wamphamvu ananyamula mwala waukulu ngati mphero yayikulu nawuponya mʼnyanja nanena kuti, “Mwa mphamvu chonchi mzinda waukulu wa Babuloni udzaponyedwa pansi, sudzapezekanso.
Amalalu, a:igele gasa bagade amo da igi bagade gaguia gadole, hano wayabo bagade amoga sanasi. E amane sia: i, “Ba: bilone da amaiwane sanasili, bu hamedafa ba: mu.
22 Mwa iwe simudzamvekanso liwu la woyimba zeze, ndi akatswiri a zoyimbayimba, oyimba zitoliro, ndi lipenga. Mwa iwe simudzapezekanso mʼmisiri wina aliyense. Mwa iwe simudzapezekanso phokoso la mphero.
Amo moilai bai bagade ganodini, sani baidama dubi, dunu ilia gesami, faludi amola dalabede fulaboi, amo da bu hamedafa nabimu. Hawa: hamosu dunu da di ganodini bidi lasu hawa: bu hame hamomu. Widi goudasu igi da udigili dialebeba: le, bu hame nabimu galebe.
23 Kuwala kwa nyale sikudzawunikanso mwa inu. Mawu a mkwati ndi mkwatibwi sadzamvekanso mwa iwe. Amalonda anu anali akuluakulu a dziko lapansi. Mitundu yonse inasokonezedwa ndi zamatsenga zako.
Di ganodini gamali nenanebe bu hame ba: mu. Udalai dunu amola uda, ela gilisili sia: dabe bu hame nabimu. Dia bidi lasu hawa: hamosu dunu ilia da gasa bagadeba: le, eno osobo bagade bidi lasu hawa: hamosu dunu ili baligi dagoi. Dia ogogosu sema nabi hou amoga di da osobo bagade fifi asi gala dunu huluane ogogoi.
24 Mwa iye munapezeka magazi a aneneri ndi a oyera mtima, ndi onse amene anaphedwa pa dziko lapansi.”
Gode da Ea fi dunu amola balofede dunu, amo ilia maga: me Ba: bilone moilai bai bagade ganodini dialebe ba: beba: le, Ba: bilone da se dabe iasu lai. Dafawane! Dunu huluane osobo bagadega enoga medole legei, amo ilia maga: me da Ba: bilone moilai bai bagade ganodini dialebe ba: i.”

< Chivumbulutso 18 >