< Chivumbulutso 17 >
1 Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja amene anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri anadza nati kwa ine, “Bwera ndikuonetse chilango cha mkazi wadama wotchuka uja amene akukhala pambali pa madzi ambiri.
tadanantaraṁ teṣāṁ saptakaṁsadhāriṇāṁ saptadūtānām eka āgatya māṁ sambhāṣyāvadat, atrāgaccha, medinyā narapatayo yayā veśyayā sārddhaṁ vyabhicārakarmma kṛtavantaḥ,
2 Mafumu a dziko lapansi amachita naye chigololo ndipo okhala pa dziko lapansi analedzera ndi vinyo wa zigololo zake.”
yasyā vyabhicāramadena ca pṛthivīnivāsino mattā abhavan tasyā bahutoyeṣūpaviṣṭāyā mahāveśyāyā daṇḍam ahaṁ tvāṁ darśayāmi|
3 Kenaka mngeloyo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku chipululu. Kumeneko ndinaona mkazi atakhala pa chirombo chofiira chokutidwa ndi mayina a chipongwe ndipo chinali ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi.
tato 'ham ātmanāviṣṭastena dūtena prāntaraṁ nītastatra nindānāmabhiḥ paripūrṇaṁ saptaśirobhi rdaśaśṛṅgaiśca viśiṣṭaṁ sindūravarṇaṁ paśumupaviṣṭā yoṣidekā mayā dṛṣṭā|
4 Mkaziyo anavala zovala za pepo ndi zofiira nadzikongoletsa ndi golide, miyala yapamwamba ndi ngale. Ananyamula chikho chagolide mʼdzanja lake, chodzaza ndi zinthu zonyansa ndi fungo loyipa la zigololo zake.
sā nārī kṛṣṇalohitavarṇaṁ sindūravarṇañca paricchadaṁ dhārayati svarṇamaṇimuktābhiśca vibhūṣitāsti tasyāḥ kare ghṛṇārhadravyaiḥ svavyabhicārajātamalaiśca paripūrṇa ekaḥ suvarṇamayaḥ kaṁso vidyate|
5 Pa mphumi pake panalembedwa dzina lodabwitsa: BABULONI WAMKULU MAYI WA AKAZI ADAMA NDI WAZOYIPITSA ZA DZIKO LAPANSI.
tasyā bhāle nigūḍhavākyamidaṁ pṛthivīsthaveśyānāṁ ghṛṇyakriyāṇāñca mātā mahābābiliti nāma likhitam āste|
6 Ndinaona kuti mkaziyo anali ataledzera ndi magazi a oyera mtima, magazi a amene anachitira umboni Yesu. Nditamuona mkaziyo ndinadabwa kwambiri.
mama dṛṣṭigocarasthā sā nārī pavitralokānāṁ rudhireṇa yīśoḥ sākṣiṇāṁ rudhireṇa ca mattāsīt tasyā darśanāt mamātiśayam āścaryyajñānaṁ jātaṁ|
7 Kenaka mngelo uja anati kwa ine, “Bwanji ukudabwa? Ndikufotokozera chinsinsi cha mkaziyu ndi chinsinsi cha chirombo chimene wakwerapochi chokhala ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi.
tataḥ sa dūto mām avadat kutastavāścaryyajñānaṁ jāyate? asyā yoṣitastadvāhanasya saptaśirobhi rdaśaśṛṅgaiśca yuktasya paśośca nigūḍhabhāvam ahaṁ tvāṁ jñāpayāmi|
8 Chirombo chimene wachionachi chinalipo kale koma tsopano kulibe ndipo chidzatuluka ku chidzenje chakuya ndi kupita kukawonongedwa. Anthu okhala pa dziko lapansi amene mayina awo sanalembedwe mʼbuku lamoyo kuyambira pa kulengedwa kwa dziko lapansi adzadabwa pamene adzaona chirombocho, chifukwa chinalipo kale, tsopano kulibe, komabe chidzabwera. (Abyssos )
tvayā dṛṣṭo 'sau paśurāsīt nedānīṁ varttate kintu rasātalāt tenodetavyaṁ vināśaśca gantavyaḥ| tato yeṣāṁ nāmāni jagataḥ sṛṣṭikālam ārabhya jīvanapustake likhitāni na vidyante te pṛthivīnivāsino bhūtam avarttamānamupasthāsyantañca taṁ paśuṁ dṛṣṭvāścaryyaṁ maṁsyante| (Abyssos )
9 “Zimenezi zikufunika kuganizira mwanzeru. Mitu isanu ndi iwiriyo ndi mapiri asanu ndi awiri pomwe mkazi uja amakhalirapo. Yomweyonso ndi mafumu asanu ndi awiri.
atra jñānayuktayā buddhyā prakāśitavyaṁ| tāni saptaśirāṁsi tasyā yoṣita upaveśanasthānasvarūpāḥ saptagirayaḥ sapta rājānaśca santi|
10 Mafumu asanu anagwa, imodzi ilipo ndipo ina sinabwere; koma pamene idzafika, idzayenera kukhala kwa kanthawi kochepa.
teṣāṁ pañca patitā ekaśca varttamānaḥ śeṣaścādyāpyanupasthitaḥ sa yadopasthāsyati tadāpi tenālpakālaṁ sthātavyaṁ|
11 Chirombo chomwe chinalipo kale ndipo tsopano kulibe ndiyo mfumu yachisanu ndi chitatu. Iyo ndi ya mʼgulu la asanu ndi awiriwo ndipo ikupita kukawonongedwa.
yaḥ paśurāsīt kintvidānīṁ na varttate sa evāṣṭamaḥ, sa saptānām eko 'sti vināśaṁ gamiṣyati ca|
12 “Nyanga khumi unaziona zija ndi mafumu khumi amene sanapatsidwe ulamuliro, koma adzapatsidwa ulamuliro pamodzi ndi chirombo kwa ora limodzi.
tvayā dṛṣṭāni daśaśṛṅgāṇyapi daśa rājānaḥ santiḥ, adyāpi tai rājyaṁ na prāptaṁ kintu muhūrttamekaṁ yāvat paśunā sārddhaṁ te rājāna iva prabhutvaṁ prāpsyanti|
13 Mafumuwo ali ndi cholinga chimodzi ndipo adzapereka mphamvu ndi ulamuliro wawo kwa chirombocho.
ta ekamantraṇā bhaviṣyanti svakīyaśaktiprabhāvau paśave dāsyanti ca|
14 Iwo adzachita nkhondo ndi Mwana Wankhosa, koma Mwana Wankhosayo adzawagonjetsa chifukwa Iye ndi Mbuye wa ambuye ndi Mfumu ya mafumu, ndipo amene adzakhala ndi Iye ndi oyitanidwa ake, osankhidwa ndi otsatira ake okhulupirika.”
te meṣaśāvakena sārddhaṁ yotsyanti, kintu meṣaśāvakastān jeṣyati yataḥ sa prabhūnāṁ prabhū rājñāṁ rājā cāsti tasya saṅgino 'pyāhūtā abhirucitā viśvāsyāśca|
15 Kenaka mngeloyo anati kwa ine, “Madzi amene unawaona pamene mkazi wadamayo anakhalapo ndiwo anthu ochuluka, mitundu ndi ziyankhulo.
aparaṁ sa mām avadat sā veśyā yatropaviśati tāni toyāni lokā janatā jātayo nānābhāṣāvādinaśca santi|
16 Nyanga khumi ndi chirombo unazionazo zidzadya mkazi wadamayo. Zidzamufwifwitsa ndi kumusiya wamaliseche; zidzadya nyama yake ndi kumutentha ndi moto.
tvayā dṛṣṭāni daśa śṛṅgāṇi paśuśceme tāṁ veśyām ṛtīyiṣyante dīnāṁ nagnāñca kariṣyanti tasyā māṁsāni bhokṣyante vahninā tāṁ dāhayiṣyanti ca|
17 Pakuti Mulungu wayika ichi mʼmitima mwawo kuti akwaniritse cholinga chake povomerezana kupereka mphamvu zawo zolamulira kwa chirombo, kufikira Mawu a Mulungu atakwaniritsidwa.
yata īśvarasya vākyāni yāvat siddhiṁ na gamiṣyanti tāvad īśvarasya manogataṁ sādhayitum ekāṁ mantraṇāṁ kṛtvā tasmai paśave sveṣāṁ rājyaṁ dātuñca teṣāṁ manāṁsīśvareṇa pravarttitāni|
18 Mkazi unamuonayo ndi mzinda waukulu umene ulamulira mafumu a dziko lapansi.”
aparaṁ tvayā dṛṣṭā yoṣit sā mahānagarī yā pṛthivyā rājñām upari rājatvaṁ kurute|