< Chivumbulutso 16 >

1 Kenaka ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Nyumba ya Mulungu ija kuwuza angelo asanu ndi awiri kuti, “Pitani, katsanulireni pa dziko lapansi ukali wa Mulungu umene uli mʼmbale zisanu ndi ziwirizi!”
J'entendis du temple une voix forte qui disait aux sept anges: « Allez, versez sur la terre les sept coupes de la colère de Dieu. »
2 Mngelo woyamba anapita natsanula mbale yake pa dziko lapansi ndipo zilonda zoyipa ndi zowawa zinabuka pa anthu amene anali ndi chizindikiro cha chirombo chija, napembedza fano lake.
La première alla répandre sa coupe sur la terre, et elle devint un ulcère douloureux pour les gens qui avaient la marque de la bête et qui adoraient son image.
3 Mngelo wachiwiri anapita natsanula mbale yake pa nyanja ndipo madzi ake anasanduka magazi, magazi ake ngati a munthu wakufa. Chamoyo chilichonse cha mʼnyanjamo chinafa.
Le second ange versa sa coupe dans la mer, qui devint du sang comme celui d'un mort. Tous les êtres vivants de la mer moururent.
4 Mngelo wachitatu anapita natsanula mbale yake pa mitsinje ndi akasupe amadzi ndipo zinasanduka magazi.
Le troisième versa sa coupe dans les fleuves et les sources d'eau, et ils devinrent du sang.
5 Kenaka ndinamva mngelo wolamulira madzi uja akuti, “Inu mwachita chilungamo, Inu Woyerayo, amene mulipo ndipo munalipo;
J'entendis l'ange des eaux qui disait: « Tu es juste, toi qui es et qui étais, ô Saint, car tu as jugé ces choses.
6 pakuti iwo anakhetsa magazi a oyera anu ndi aneneri anu, nʼchifukwa chake mwawapatsa magazi kuti amwe, zomwe zikuwayenera.”
Car ils ont répandu le sang des saints et des prophètes, et tu leur as donné du sang à boire. Ils méritent cela. »
7 Kenaka ndinamva mawu ochokera ku guwa lansembe akuti, “Inde, Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse, chiweruzo chanu ndi choona ndi cholungama.”
J'ai entendu l'autel dire: « Oui, Seigneur Dieu, le Tout-Puissant, tes jugements sont vrais et justes. »
8 Mngelo wachinayi anapita natsanula mbale yake pa dzuwa ndipo dzuwa linapatsidwa mphamvu yopsereza anthu ndi moto.
Le quatrième versa sa coupe sur le soleil, et il lui fut donné de brûler les hommes par le feu.
9 Anapserera nako kutentha kwakukuluko ndipo anatukwana Mulungu, amene anali ndi ulamuliro pa miliri imeneyi, koma anakana kulapa ndi kumulemekeza.
Les gens furent brûlés par une grande chaleur, et les gens blasphémèrent le nom de Dieu qui a le pouvoir sur ces fléaux. Ils ne se sont pas repentis et ne lui ont pas rendu gloire.
10 Mngelo wachisanu anapita natsanula mbale yake pa mpando waufumu wa chirombo chija ndipo mdima unagwa ponse pamene panali ufumu wake. Anthu analuma malilime awo chifukwa cha ululu.
Le cinquième versa sa coupe sur le trône de la bête, et son royaume fut obscurci. Ils se rongeaient la langue à cause de la douleur,
11 Ndipo anatukwana Mulungu wakumwamba chifukwa cha maululu awo ndi zilonda zawo koma anakana kulapa pa zimene anachita.
et ils blasphémaient le Dieu du ciel à cause de leurs douleurs et de leurs ulcères. Ils ne se sont toujours pas repentis de leurs œuvres.
12 Mngelo wachisanu ndi chimodzi anapita natsanula mbale yake pa mtsinje waukulu wa Yufurate, ndipo madzi ake anaphwa kuti pakhale njira yodzera mafumu ochokera kummawa.
Le sixième versa sa coupe sur le grand fleuve, l'Euphrate. Ses eaux tarirent, afin que le chemin fût préparé pour les rois qui viendront du soleil levant.
13 Kenaka ndinaona mizimu yoyipa itatu imene inkaoneka ngati achule; inatuluka mʼkamwa mwa chinjoka chija, mʼkamwa mwa chirombo chija ndi mʼkamwa mwa mneneri wonyenga uja.
Je vis sortir de la bouche du dragon, de la bouche de la bête et de la bouche du faux prophète, trois esprits impurs, semblables à des grenouilles;
14 Imeneyi ndiyo mizimu ya ziwanda imene imachita zizindikiro zodabwitsa ndipo imatuluka kupita kwa mafumu a dziko lonse, kukawasonkhanitsa ku nkhondo ya pa tsiku lalikulu la Mulungu Wamphamvuzonse.
car ce sont des esprits de démons, qui font des prodiges, et qui vont vers les rois de toute la terre habitée, afin de les rassembler pour le combat du grand jour de Dieu le Tout-Puissant.
15 “Taonani, ndikubwera ngati mbala! Wodala munthu amene ali maso, nasunga zovala zake, kuti asayende maliseche kuti angaonetse maliseche ake.”
« Voici, je viens comme un voleur. Heureux celui qui veille et qui garde ses vêtements, afin qu'il ne marche pas nu, et qu'on ne voie pas sa honte. »
16 Kenaka mizimu ija inasonkhanitsa pamodzi mafumu ku malo amene mʼChihebri amatchedwa Armagedo.
Il les rassembla dans le lieu qui s'appelle en hébreu « Harmagedon ».
17 Mngelo wachisanu ndi chiwiri anatsanulira mbale yake mu mlengalenga ndipo ku Nyumba ya Mulungu kunamveka mawu ofuwula kuchokera ku mpando waufumu kuti, “Kwatha!”
Le septième versa sa coupe dans l'air. Et une voix forte sortit du temple du ciel, du trône, en disant: « C'est fait! ».
18 Kenaka kunachitika mphenzi, phokoso, mabingu ndi chivomerezi choopsa. Chivomerezi ngati ichi sichinachitikepo chikhalire cha munthu pa dziko lapansi. Chinali chivomerezi choopsa kwambiri.
Il y eut des éclairs, des sons, des tonnerres, et un grand tremblement de terre, tel qu'il n'y en a jamais eu depuis qu'il y a des hommes sur la terre, un tremblement de terre si grand et si puissant.
19 Mzinda waukuluwo unagawika magawo atatu ndipo mizinda ya mitundu ya anthu inagwa. Mulungu anakumbukira Babuloni Wamkulu namupatsa chikho chake chodzaza ndi vinyo wa ukali wa mkwiyo wake.
La grande ville fut divisée en trois parties, et les villes des nations tombèrent. On se souvint de Babylone la grande aux yeux de Dieu, pour lui donner la coupe du vin de l'ardeur de sa colère.
20 Chilumba chilichonse chinathawa ndipo mapiri sanaonekenso.
Toutes les îles s'enfuirent, et les montagnes ne furent pas retrouvées.
21 Matalala akuluakulu olemera pafupifupi makilogalamu makumi asanu anagwa kuchokera kumwamba kugwera pa anthu. Ndipo anthu anatukwana Mulungu chifukwa cha mliri wa matalala popeza unali mliri woopsa kwambiri.
De gros grêlons, du poids d'un talent, tombaient du ciel sur les gens. On blasphémait Dieu à cause du fléau de la grêle, car ce fléau était extrêmement violent.

< Chivumbulutso 16 >