< Chivumbulutso 15 >
1 Kumwamba ndinaona chizindikiro china chachikulu ndi chodabwitsa: angelo asanu ndi awiri ali ndi miliri isanu ndi iwiri yomaliza chifukwa Mulungu anakwiya kotheratu.
És láttam a mennyben egy másik nagy és csodálatos jelet: hét angyalt, akiknél az utolsó hét csapás volt, mert ezekkel teljesedett be Isten haragja.
2 Ndipo ndinaona chimene chinaoneka ngati nyanja yonyezimira yosakaniza ndi moto, ndipo pambali pa nyanjayo panayima amene anagonjetsa chirombo chija ndi fano lake, ndi nambala yotanthauza dzina lake. Anthuwo ananyamula azeze amene Mulungu anawapatsa.
És láttam, mint egy üvegtengert, amely tűzzel volt elegyítve, és azokat, akik diadalmaskodtak a fenevadon és az ő képén és bélyegén és nevének számán, láttam az üvegtenger mellett állni azokat, akiknek kezében voltak Isten hárfái.
3 Iwo ankayimba nyimbo ya Mose, mtumiki wa Mulungu, ndi nyimbo ya Mwana Wankhosa. Nyimbo yake inkati, “Zochita zanu ndi zazikulu ndi zodabwitsa, Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse Njira zanu ndi zachilungamo ndi zoona, Mfumu ya mitundu yonse.
És énekelték Mózesnek, Isten szolgájának énekét és a Bárány énekét: „Nagyok és csodálatosak a te dolgaid, mindenható Úristen, igazságosak és igazak a te utaid, ó, szentek Királya.
4 Inu Ambuye, ndani angapande kukuopani, ndi kulemekeza dzina lanu? Pakuti Inu nokha ndiye woyera. Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzapembedza pamaso panu, pakuti ntchito zanu zolungama zaonekera poyera.”
Ki ne félne téged, Uram! És ki ne dicsőítené a te nevedet? Mert csak egyedül te vagy szent. Mert eljönnek mind a pogányok és leborulnak előtted, mert ítéleteid nyilvánvalókká lettek.“
5 Zitatha izi, ndinaona kumwamba Nyumba ya Mulungu imene ndi Tenti ya Umboni, atatsekula.
És ezek után láttam, és íme megnyílt a mennyben a bizonyságtétel sátorának temploma,
6 Mʼnyumbamo munatuluka angelo asanu ndi awiri ndi miliri isanu ndi iwiri. Angelowo anavala nsalu zoyera bwino zonyezimira ndi malamba agolide pa zifuwa zawo.
és kijött a templomból a hét angyal, akiknél a hét csapás volt, tiszta fehér gyolcsba öltözve és mellük arany övvel övezve.
7 Ndipo kenaka chimodzi cha zamoyo zinayi zija chinapereka kwa angelo asanu ndi awiri mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi ukali wa Mulungu amene ali ndi moyo mpaka muyaya. (aiōn )
És egy a négy élőlény közül adott a hét angyalnak hét arany poharat, amely az örökkön örökké élő haragjával volt tele. (aiōn )
8 Ndipo Nyumba ya Mulungu inadzaza ndi utsi wochokera ku ulemerero wa Mulungu ndi ku mphamvu zake, ndipo panalibe yemwe akanalowa mʼNyumbayo mpaka miliri isanu ndi iwiri ya angelo asanu ndi awiri aja itatha.
És megtelt a templom füsttel Isten dicsőségétől és erejétől, és senki sem mehetett be a templomba, míg a hét angyal hét csapása be nem teljesedik.