< Chivumbulutso 15 >

1 Kumwamba ndinaona chizindikiro china chachikulu ndi chodabwitsa: angelo asanu ndi awiri ali ndi miliri isanu ndi iwiri yomaliza chifukwa Mulungu anakwiya kotheratu.
Eka ne aneno ranyisi machielo malich ahinya ei polo: Ne aneno Malaike abiriyo, motingʼo masiche abiriyo, mago ne masiche mogik nikech ka girumo to mirimb Nyasaye chopo kare.
2 Ndipo ndinaona chimene chinaoneka ngati nyanja yonyezimira yosakaniza ndi moto, ndipo pambali pa nyanjayo panayima amene anagonjetsa chirombo chija ndi fano lake, ndi nambala yotanthauza dzina lake. Anthuwo ananyamula azeze amene Mulungu anawapatsa.
Ne aneno gima chalo gi nam mar kio mar rangʼi moruwore gi mach to e bathe kanyo ne aneno joma oseloyo ondiek malichno kod kido machalo kode to gi namba mar nyinge kochungʼ. Negitingʼo nyatiti mane omigi gi Nyasaye,
3 Iwo ankayimba nyimbo ya Mose, mtumiki wa Mulungu, ndi nyimbo ya Mwana Wankhosa. Nyimbo yake inkati, “Zochita zanu ndi zazikulu ndi zodabwitsa, Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse Njira zanu ndi zachilungamo ndi zoona, Mfumu ya mitundu yonse.
ka giwero wend Musa jatich Nyasaye gi wend Nyarombo kama: “Yaye Ruoth Nyasaye Maratego, mano kaka tijeni dongo kendo lich. Yaye Ruodh Nyasaye ogendini, yoreni nikare kendo gin adiera.
4 Inu Ambuye, ndani angapande kukuopani, ndi kulemekeza dzina lanu? Pakuti Inu nokha ndiye woyera. Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzapembedza pamaso panu, pakuti ntchito zanu zolungama zaonekera poyera.”
En ngʼa, ma ok nyal luori aa Ruoth, ma ok nyal miyo nyingi duongʼ? Nikech in kendi ema iler, ogendini duto nobi e nyimi mondo olami, nimar timbeni makare osefwenyore ratiro.”
5 Zitatha izi, ndinaona kumwamba Nyumba ya Mulungu imene ndi Tenti ya Umboni, atatsekula.
Eka ne angʼiyo mi aneno ka hekalu mar Hemb Rapar oyawore e polo.
6 Mʼnyumbamo munatuluka angelo asanu ndi awiri ndi miliri isanu ndi iwiri. Angelowo anavala nsalu zoyera bwino zonyezimira ndi malamba agolide pa zifuwa zawo.
Malaike abiriyo motingʼo masiche abiriyo nowuok e hekalu. Ne girwakore gi lewni maler mapakni kendo manyilni to negitweyo okanda mar dhahabu e korgi.
7 Ndipo kenaka chimodzi cha zamoyo zinayi zija chinapereka kwa angelo asanu ndi awiri mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi ukali wa Mulungu amene ali ndi moyo mpaka muyaya. (aiōn g165)
Achiel kuom gik mangima angʼwen ka ne omiyo malaike abiriyogo tewni abiriyo mag dhahabu mopongʼ gi mirimb Nyasaye mosiko nyaka chiengʼ. (aiōn g165)
8 Ndipo Nyumba ya Mulungu inadzaza ndi utsi wochokera ku ulemerero wa Mulungu ndi ku mphamvu zake, ndipo panalibe yemwe akanalowa mʼNyumbayo mpaka miliri isanu ndi iwiri ya angelo asanu ndi awiri aja itatha.
Hekalu ne iye opongʼ gi iro moa e duongʼ maler mar Nyasaye kod tekone. To onge ngʼama ne nyalo donjo ei hekalu kapok masiche abiriyo mag malaike abiriyogo orumo.

< Chivumbulutso 15 >