< Chivumbulutso 13 >

1 Kenaka ndinaona chinjokacho chitayima mʼmbali mwa nyanja. Ndipo ndinaona chirombo chikutuluka mʼnyanja. Chinali ndi nyanga khumi ndi mitu isanu ndi iwiri. Pa nyanga iliyonse chinavala chipewa chaufumu, ndipo pa mutu uliwonse panali dzina lonyoza Mulungu.
Andin, déngizdin on münggüzlük, yette bashliq bir diwining chiqiwatqanliqini kördüm. Uning herbir münggüzide birdin taj bar idi, herbir béshida kupurluq namliri yéziqliq idi.
2 Chirombo chimene ndinachionacho chinali ngati kambuku, mapazi ake ngati chimbalangondo, kukamwa kwake ngati kwa mkango. Chinjoka chija chinapatsa chirombocho mphamvu zake, mpando wake waufumu ndiponso ulamuliro waukulu.
Men körgen bu diwe yilpizgha oxshaytti, putliri éyiqning putlirigha, aghzi bolsa shirning aghzigha oxshaytti. Ejdiha uninggha öz qudriti, texti we zor hoquqini berdi.
3 Umodzi wa mitu wa chirombocho unkaoneka ngati uli ndi bala losati nʼkupola, koma nʼkuti balalo litapola. Dziko lonse linadabwa ndipo linatsatira chirombocho.
Diwining bashliridin biri ejellik yarilan’ghandek turatti. Lékin, bu ejellik yara saqayghanidi. Pütkül dunya diwige heyranuhes bolup uninggha [egeshti].
4 Anthu anapembedza chinjoka chija chifukwa chinapereka ulamuliro wake kwa chirombocho. Nachonso chirombo chija anachipembedza nʼkumafunsa kuti, “Ndani angafanane ndi chirombochi? Ndani angachite nacho nkhondo?”
Ejdiha diwige [seltenetlik] hoquq bergechke ular ejdihagha choqunushti. Ular yene diwigimu choqunup: — Diwining tengdishi barmu? Uning bilen kimmu élishalisun? — dédi.
5 Chirombo chija chinaloledwa kuyankhula mawu onyada ndi achipongwe kwa Mulungu. Chinapatsidwa mphamvu zolamulira pa miyezi 42.
Diwige tekebburluq we kupurluq qilidighan éghiz bérildi; uninggha qiriq ikki ay ish körüshke hoquq bérildi.
6 Ndipo chinayamba kuyankhula mawu achipongwe onyoza Mulungu, dzina lake, malo okhalamo ndi onse amene amakhala kumwamba.
U Xudagha kupurluq qilghili — Uning namigha we Uning dergahigha, shundaqla ershni makan qilghanlargha kupurluq qilghili aghzini achti.
7 Chinaloledwa kuchita nkhondo ndi oyera mtima ndi kuwagonjetsa. Ndipo chinapatsidwanso mphamvu zolamulira anthu a fuko lililonse, mtundu uliwonse ndi chiyankhulo chilichonse.
Uning muqeddes bendilerge qarshi jeng qilip, ularning üstidin ghalib kélishige yol qoyuldi; her qebile, her millet, her xil tilda sözlishidighan ellerge hökümranliq qilish hoquqi uninggha bérildi.
8 Anthu onse okhala pa dziko lapansi adzapembedza chirombocho, aliyense amene chilengedwere cha dziko lapansi dzina lake silinalembedwe mʼbuku la amoyo la Mwana Wankhosa anaphedwa uja.
Yer yüzidikilerning hemmisi — alem apiride bolghandin buyan boghuzlinip bolghan Qozining hayatliq deptirige nami yézilmighanlar bolsa, uninggha sejde qilidu.
9 Iye amene ali ndi makutu, amve.
Quliqi barlar, buni anglisun!
10 “Woyenera kupita ku ukapolo, adzapita ku ukapolo. Woyenera kufa ndi lupanga, adzafa ndi lupanga.” Pamenepa kwa anthu a Mulungu pakufunika kupirira ndi kukhulupirika.
««Tutqun bolidu» dep békitilgenler choqum tutqun bolidu, «qilichlinidu» dep békitilgenler choqum qilichlinip ölidu». Muqeddes bendilirining sewri-taqiti we étiqadi mana shu ishlarda melum bolidu.
11 Kenaka ndinaona chirombo china chikutuluka mʼnthaka. Chinali ndi nyanga ziwiri ngati mwana wankhosa koma kuyankhula kwake ngati chinjoka.
Men yerdin chiqiwatqan yene bir diwini kördüm. Uning qoziningkidek kichik ikki münggüzi bar idi, lékin awazi ejdihaningkidek chiqatti.
12 Chinalamulira ndi mphamvu zonse za chirombo choyamba chija, ndipo chinachititsa kuti dziko lapansi ndi anthu okhalamo alambire chirombo choyamba chija, chimene bala lake losati nʼkupola linali litapola.
U awwalqi diwige wakaliten uning pütün hoquqini yürgüzüp, yer yüzini we uningda turuwatqanlarni ejellik yarisi saqayghan awwalqi diwige choqunduridu.
13 Ndipo chinachita zizindikiro zazikulu zodabwitsa, mpaka kumagwetsa moto pa dziko lapansi kuchokera kumwamba anthu akuona.
U zor möjizilik alametlerni körsitetti, hetta kishilerning köz aldida asmandin yer yüzige ot yaghduratti.
14 Chifukwa cha zizindikiro zimene chinaloledwa kuchita mʼmalo mwa chirombo choyamba chija, chimene bala lake linapola, chinanyenga anthu okhala pa dziko lapansi. Chinalamula anthu kuti apange fano mopereka ulemu kwa chirombo chimene chinavulazidwa ndi lupanga, koma nʼkukhalabe ndi moyo.
U awwalqi diwige wakaliten körsitishke hoquqlandurulghan alametler bilen yer yüzide turuwatqanlarni azdurup, ulargha «qilich bilen yarilan’ghan, lékin tirik qalghan» dégen awwalqi diwige atap bir but-heykel yasap tikleshni tapilidi.
15 Chirombo cha chiwirichi chinapatsidwa mphamvu zakupereka mpweya kwa fano la chirombo choyamba chija kuti liyankhule ndi kuphetsa aliyense wokana kupembedza fanolo.
Diwining but-heykilige nepes kirgüzüp, uninggha uni sözliyeleydighan qilish we uninggha choqunmighanlarning hemmisini öltürgüzüsh qudriti bérildi.
16 Chinakakamiza aliyense, wamngʼono, wamkulu, wolemera, wosauka, mfulu ndi kapolo kuti alembedwe chizindikiro pa dzanja lamanja kapena pa mphumi.
U töwen we katta, bay we kembeghel, hör we qullarning hemmisini ong qoli yaki péshanisige tamgha basturushqa mejburlidi.
17 Chinkachita zimenezi kuti wina aliyense asaloledwe kugula kapena kugulitsa kanthu ngati alibe chizindikiro chimenechi, chimene ndi dzina la chirombocho kapena nambala yotanthauza dzina lake.
U yene bu tamgha, yeni diwining nami yaki uning namidiki reqem bésilghanlardin bashqa héchkim bir nerse sétiwalalmaydu yaki satalmaydu, dep békitti.
18 Pano pafunika nzeru. Munthu amene ali ndi nzeru atanthauze nambala ya chirombocho, pakuti nambalayo ikutanthauza munthu. Nambala yake ndi 666.
Mana bu yerde hékmet bar. Eqil-parasiti barliki kishiler diwining reqimini hésablap baqsun; chünki bu reqem bir ademning reqimi bolidu. Uning reqimi 666dur.

< Chivumbulutso 13 >