< Chivumbulutso 13 >
1 Kenaka ndinaona chinjokacho chitayima mʼmbali mwa nyanja. Ndipo ndinaona chirombo chikutuluka mʼnyanja. Chinali ndi nyanga khumi ndi mitu isanu ndi iwiri. Pa nyanga iliyonse chinavala chipewa chaufumu, ndipo pa mutu uliwonse panali dzina lonyoza Mulungu.
Amola hanome da hano wayabo bagade bega: lelu. Amalalu, na da ohe fi liligi wayabo hano hagududili manebe ba: i. Amo ohe fi da hono nabuane gala amola dialuma fesuale gala. Ea hono afae afae amo da: iya habuga ba: i amola ea dialuma afae afae, dio amo da Godema gadesu dio amo dedei ba: i.
2 Chirombo chimene ndinachionacho chinali ngati kambuku, mapazi ake ngati chimbalangondo, kukamwa kwake ngati kwa mkango. Chinjoka chija chinapatsa chirombocho mphamvu zake, mpando wake waufumu ndiponso ulamuliro waukulu.
Amo ohe fi da lebade agoai ba: i. Ea emo da bea ohe ea emo agoane ba: i amola ea lafi da laione wa: me amo ea lafi agoane ba: i. Hanome da amo ohe fi liligima, hi gasa amola hi ouligisu hou amola hi fisu ema i.
3 Umodzi wa mitu wa chirombocho unkaoneka ngati uli ndi bala losati nʼkupola, koma nʼkuti balalo litapola. Dziko lonse linadabwa ndipo linatsatira chirombocho.
Ohe fi liligi amo ea dialuma afadafa da fa: gi agoai ba: i, be amo da bahoi dagoi ba: i. Osobo bagade fifi asi gala dunu huluane da fofogadigiba: le, ohe fi liligi amoma fa: no bobogei.
4 Anthu anapembedza chinjoka chija chifukwa chinapereka ulamuliro wake kwa chirombocho. Nachonso chirombo chija anachipembedza nʼkumafunsa kuti, “Ndani angafanane ndi chirombochi? Ndani angachite nacho nkhondo?”
Hanome da ea ouligisu hou ohe fi liligi ema ia dagoiba: le, dunu huluane da hanome amoma nodone sia: ne gadosu. Ilia da ohe fi liligi, ema nodone sia: ne gadole, amane sia: i, “Ohe fi liligi da eno huluane ilia hou baligi dagoi. Nowa da ema gegemu defelela: ?”
5 Chirombo chija chinaloledwa kuyankhula mawu onyada ndi achipongwe kwa Mulungu. Chinapatsidwa mphamvu zolamulira pa miyezi 42.
Amo ohe fi liligi oubi 42 amoga osobo bagadega ouligisuwane esalumusa: , Gode da ea logo hame hedofai. E da gasa fi hou hamone, Godema gadesu.
6 Ndipo chinayamba kuyankhula mawu achipongwe onyoza Mulungu, dzina lake, malo okhalamo ndi onse amene amakhala kumwamba.
Ohe fi liligi da Gode amola Ea dio, Ea esalebe soge amola dunu huluane Hebene ganodini esala, amo huluanema gadesu.
7 Chinaloledwa kuchita nkhondo ndi oyera mtima ndi kuwagonjetsa. Ndipo chinapatsidwanso mphamvu zolamulira anthu a fuko lililonse, mtundu uliwonse ndi chiyankhulo chilichonse.
Ohe fi liligi da Gode Ea fi ilima gegene, fane legei. E da fifi asi gala, fi hisu amola sia: hisu, huluane ilima ouligisu esaloma: ne, Gode da amo logo hame hedofai.
8 Anthu onse okhala pa dziko lapansi adzapembedza chirombocho, aliyense amene chilengedwere cha dziko lapansi dzina lake silinalembedwe mʼbuku la amoyo la Mwana Wankhosa anaphedwa uja.
Dunu huluane osobo bagade ganodini da ema nodone sia: ne gadomu. Be dunu, amo Gode da osobo bagade hame hahamoi eso amoga ilia dio Esalusu Buga amo Sibi Mano medole legei Ea buga, amo ganodini dedei dunu ilia da ohe fi liligi amoma hame sia: ne gadoi.
9 Iye amene ali ndi makutu, amve.
‘Defea! Ge galea, nabima!’
10 “Woyenera kupita ku ukapolo, adzapita ku ukapolo. Woyenera kufa ndi lupanga, adzafa ndi lupanga.” Pamenepa kwa anthu a Mulungu pakufunika kupirira ndi kukhulupirika.
Nowa da udigili hawa: hamomusa: gagulaligili ilegei galea, e da gagulaligi dagoi ba: mu. Nowa da enoga gegesu gobiheiga medole legemusa: ilegei galea, e da gobiheiga medole legei dagoi ba: mu. Amaiba: le, Gode Ea fi dunu ilia mae yolesili, dafawaneyale dawa: iwane esalumu da defea.”
11 Kenaka ndinaona chirombo china chikutuluka mʼnthaka. Chinali ndi nyanga ziwiri ngati mwana wankhosa koma kuyankhula kwake ngati chinjoka.
Amalalu, na da ohe fi liligi eno osobo hagududili heda: lebe ba: i. E da hono aduna amo sibi mano ea hono defele gala. Ea sia: da hanome agoane liligi ea sia: defele nabi.
12 Chinalamulira ndi mphamvu zonse za chirombo choyamba chija, ndipo chinachititsa kuti dziko lapansi ndi anthu okhalamo alambire chirombo choyamba chija, chimene bala lake losati nʼkupola linali litapola.
E da musa: ohe fi liligi amo ea ouligisu hou lai dagoi. E da dunu huluane osobo bagadega esalebe, amo huluane musa: ohe fi (amo da ea fa: gi bahoi ba: i) ema sia: ne gadoma: ne, gasawane logei.
13 Ndipo chinachita zizindikiro zazikulu zodabwitsa, mpaka kumagwetsa moto pa dziko lapansi kuchokera kumwamba anthu akuona.
Amo ohe fi liligi ageyadu da musa: hame ba: su gasa bagade hou hamosu. E da dunu huluane ba: ma: ne, lalu bagade muagadodi misa: ne, osobo bagadega doaga: ma: ne, ea sia: ga hamoi dagoi.
14 Chifukwa cha zizindikiro zimene chinaloledwa kuchita mʼmalo mwa chirombo choyamba chija, chimene bala lake linapola, chinanyenga anthu okhala pa dziko lapansi. Chinalamula anthu kuti apange fano mopereka ulemu kwa chirombo chimene chinavulazidwa ndi lupanga, koma nʼkukhalabe ndi moyo.
Gode da ea logo hame hedofaiba: le, e da musa: ohe fi liligi ba: ma: ne, musa: hame ba: i gasa bagade hou hamonanu. Amaiba: le, e da osobo bagade dunu huluanedafa ilima ogogoi. E da ilima amane sia: i, “Dilia ohe fi liligi amo da gegesu gobiheiga fa: gi be uhi, ema sia: ne gadoma: ne, ea ba: su agoaila defele loboga hamoma!”
15 Chirombo cha chiwirichi chinapatsidwa mphamvu zakupereka mpweya kwa fano la chirombo choyamba chija kuti liyankhule ndi kuphetsa aliyense wokana kupembedza fanolo.
Gode da logo hame hedofaiba: le, ohe fi liligi ageyadu da amo musa: ohe fi agoaila loboga hamoi liligi amoma mifo i. Amalalu, amo loboga hamoi liligi da uhini sia: baoui. Amola nowa da loboga hamoi agoaila liligi ema hame nodone sia: ne gadoloba, e da amo dunu medole legesu.
16 Chinakakamiza aliyense, wamngʼono, wamkulu, wolemera, wosauka, mfulu ndi kapolo kuti alembedwe chizindikiro pa dzanja lamanja kapena pa mphumi.
Ohe fi liligi da dunu huluane amo fonobahadi, bagade, hame gagui, bagade gagui, udigili hawa: hamosu dunu amola halegale lalebe dunu, amo huluane da dawa: digima: ne ilegei dedesu ilia lobodafa o ilia odagiga ilegele dedema: ne logei.
17 Chinkachita zimenezi kuti wina aliyense asaloledwe kugula kapena kugulitsa kanthu ngati alibe chizindikiro chimenechi, chimene ndi dzina la chirombocho kapena nambala yotanthauza dzina lake.
Amo dedei da ohe fi liligi ea dio o idi amo ea dio olelesu. Amai dawa: digima: ne dedesu hame dedei ba: loba, dunu da liligi bidi lamu da ema sema bagade gala.
18 Pano pafunika nzeru. Munthu amene ali ndi nzeru atanthauze nambala ya chirombocho, pakuti nambalayo ikutanthauza munthu. Nambala yake ndi 666.
Amo bagade dawa: ma. Nowa dunu da bagade dawa: su galea e da ohe fi liligi idi amo ea dawa: loma: ne dawa: mu. Amo idi da dunu ea dio olelesa. Idi da 666.