< Chivumbulutso 12 >
1 Chizindikiro chachikulu chinaoneka kuthambo; mayi atavala dzuwa, mapazi ake ataponda mwezi, pamutu pake pali chipewa chaufumu chokhala ndi nyenyezi khumi ndi ziwiri.
And a great sign was seen in the heaven, a woman arrayed with the sun, and the moon under her feet, and upon her head a crown of twelve stars,
2 Mayiyo anali woyembekezera ndipo pa nthawi yake yochira analira mokuwa chifukwa cha ululu wakubala.
and being with child she doth cry out, travailing and pained to bring forth.
3 Kenaka ku thambo kunaonekanso chizindikiro china; chinjoka chachikulu kwambiri, chofiira chomwe chinali ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi; pamutu uliwonse chitavala chipewa chaufumu.
And there was seen another sign in the heaven, and, lo, a great red dragon, having seven heads and ten horns, and upon his head seven diadems,
4 Mchira wake unakokolola gawo limodzi la magawo atatu a nyenyezi kuzichotsa ku thambo ndi kuziponya pa dziko lapansi. Chinjoka chija chinadzayima patsogolo pa mayi uja amene anali pafupi kuberekayu kuti mwanayo akangobadwa chimudye.
and his tail doth draw the third of the stars of the heaven, and he did cast them to the earth; and the dragon did stand before the woman who is about to bring forth, that when she may bring forth, her child he may devour;
5 Mayiyo anabereka mwana wamwamuna amene adzalamulira anthu a mitundu ina yonse ndi ndodo yachitsulo. Ndipo mwanayo analandidwa ku dzanja la mayiyo ndi kupita naye kwa Mulungu ku mpando wake waufumu.
and she brought forth a male child, who is about to rule all the nations with a rod of iron, and caught away was her child unto God and His throne,
6 Mayiyo anathawira ku chipululu ku malo kumene Mulungu anamukonzera, kumene akasamalidweko masiku 1,260.
and the woman did flee to the wilderness, where she hath a place made ready from God, that there they may nourish her — days a thousand, two hundred, sixty.
7 Zitatero, kumwamba kunayambika nkhondo. Mikayeli ndi angelo ake kumenyana ndi chinjoka chija. Chinjokacho ndi angelo ake anabwezeranso.
And there came war in the heaven; Michael and his messengers did war against the dragon, and the dragon did war, and his messengers,
8 Koma analibe mphamvu ndipo anagonjetsedwa nathamangitsidwa kumwambako.
and they did not prevail, nor was their place found any more in the heaven;
9 Chinjoka chachikulu chija chinagwetsedwa pansi. Ichocho ndiye njoka yakalekale ija yotchedwa Mdierekezi kapena Satana, amene amasocheretsa anthu a pa dziko lonse lapansi. Chinaponyedwa pa dziko la pansi pamodzi ndi angelo ake.
and the great dragon was cast forth — the old serpent, who is called 'Devil,' and 'the Adversary,' who is leading astray the whole world — he was cast forth to the earth, and his messengers were cast forth with him.
10 Kenaka ndinamva mawu ofuwula kumwamba akunena kuti, “Tsopano chipulumutso, mphamvu, ufumu wa Mulungu wathu ndi ulamuliro wa Khristu wake zabwera. Pakuti woneneza abale athu uja, amene amangokhalira kuwaneneza pamaso pa Mulungu usana ndi usiku, wagwetsedwa pansi.
And I heard a great voice saying in the heaven, 'Now did come the salvation, and the power, and the reign, of our God, and the authority of His Christ, because cast down was the accuser of our brethren, who is accusing them before our God day and night;
11 Abale athuwo anamugonjetsa ndi magazi a Mwana Wankhosa ndiponso mawu a umboni wawo. Iwo anadzipereka kwathunthu, moti sanakonde miyoyo yawo.
and they did overcome him because of the blood of the Lamb, and because of the word of their testimony, and they did not love their life — unto death;
12 Choncho, kondwerani, inu dziko lakumwamba ndi onse okhala kumeneko! Koma tsoka dziko lapansi ndi nyanja chifukwa Mdierekezi wagwetsedwa kwa inu! Iye wadzazidwa ndi ukali chifukwa akudziwa kuti nthawi yake ndi yochepa.”
because of this be glad, ye heavens, and those in them who do tabernacle; woe to those inhabiting the land and the sea, because the Devil did go down unto you, having great wrath, having known that he hath little time.'
13 Pamene chinjokacho chinaona kuti chagwetsedwa pa dziko lapansi, chinayamba kuthamangitsa mayi uja amene anali atabala mwana wamwamunayu.
And when the dragon saw that he was cast forth to the earth, he pursued the woman who did bring forth the male,
14 Mayiyo anapatsidwa mapiko awiri a chiwombankhanga chachikulu kuti athawire ku malo ake aja a ku chipululu. Kumeneko adzasamalidwako zaka zitatu ndi theka kuti chinjoka chija chisamupeze.
and there were given to the woman two wings of the great eagle, that she may fly to the wilderness, to her place, where she is nourished a time, and times, and half a time, from the face of the serpent;
15 Kenaka chinjoka chija chinalavulira mayiyo madzi ambiri ngati mtsinje, kuti madziwo amukokolole.
and the serpent did cast forth after the woman, out of his mouth, water as a river, that he may cause her to be carried away by the river,
16 Koma dziko lapansi linamuthandiza mayiyo. Nthaka inatsekuka ndi kumeza mtsinje uja unachokera mʼkamwa mwa chinjokacho.
and the land did help the woman, and the land did open its mouth and did swallow up the river, that the dragon did cast forth out of his mouth;
17 Pamenepo chinjokacho chinamupsera mtima mayiyo ndipo chinachoka kupita kukachita nkhondo ndi ana ena onse a mayiyo, ndiye kuti anthu amene anasunga malamulo a Mulungu ndi kuchitira umboni za Yesu.
and the dragon was angry against the woman, and went away to make war with the rest of her seed, those keeping the commands of God, and having the testimony of Jesus Christ.