< Chivumbulutso 12 >

1 Chizindikiro chachikulu chinaoneka kuthambo; mayi atavala dzuwa, mapazi ake ataponda mwezi, pamutu pake pali chipewa chaufumu chokhala ndi nyenyezi khumi ndi ziwiri.
And there appeared a great sign in heaven, a woman clothed with the sun, and the moon under her feet, and upon her head a crown of twelve stars.
2 Mayiyo anali woyembekezera ndipo pa nthawi yake yochira analira mokuwa chifukwa cha ululu wakubala.
And being with child, she cried out in travail, labouring to be delivered.
3 Kenaka ku thambo kunaonekanso chizindikiro china; chinjoka chachikulu kwambiri, chofiira chomwe chinali ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi; pamutu uliwonse chitavala chipewa chaufumu.
And there appeared another sign in heaven, and behold, a great red dragon, having seven heads and ten horns; and upon his heads seven crowns.
4 Mchira wake unakokolola gawo limodzi la magawo atatu a nyenyezi kuzichotsa ku thambo ndi kuziponya pa dziko lapansi. Chinjoka chija chinadzayima patsogolo pa mayi uja amene anali pafupi kuberekayu kuti mwanayo akangobadwa chimudye.
And his tail drew a third part of the stars of heaven, and cast them to the earth: and the dragon stood before the woman, who was ready to bring forth, that when she was delivered, he might devour her child.
5 Mayiyo anabereka mwana wamwamuna amene adzalamulira anthu a mitundu ina yonse ndi ndodo yachitsulo. Ndipo mwanayo analandidwa ku dzanja la mayiyo ndi kupita naye kwa Mulungu ku mpando wake waufumu.
And she brought forth a male child, who was to rule all nations with a rod of iron: and her child was caught up unto God, and to his throne.
6 Mayiyo anathawira ku chipululu ku malo kumene Mulungu anamukonzera, kumene akasamalidweko masiku 1,260.
And the woman fled into the wilderness, where she hath a place prepared of God, that they might nourish her there a thousand two hundred and sixty days.
7 Zitatero, kumwamba kunayambika nkhondo. Mikayeli ndi angelo ake kumenyana ndi chinjoka chija. Chinjokacho ndi angelo ake anabwezeranso.
And there was war in heaven, Michael and his angels fought against the dragon: and the dragon fought, and his angels;
8 Koma analibe mphamvu ndipo anagonjetsedwa nathamangitsidwa kumwambako.
but these prevailed not, neither was their place found any more in heaven.
9 Chinjoka chachikulu chija chinagwetsedwa pansi. Ichocho ndiye njoka yakalekale ija yotchedwa Mdierekezi kapena Satana, amene amasocheretsa anthu a pa dziko lonse lapansi. Chinaponyedwa pa dziko la pansi pamodzi ndi angelo ake.
And the great dragon was cast out, that old serpent, called the devil and Satan, who deceiveth the whole world: he was cast down to the earth, and his angels were cast down with him.
10 Kenaka ndinamva mawu ofuwula kumwamba akunena kuti, “Tsopano chipulumutso, mphamvu, ufumu wa Mulungu wathu ndi ulamuliro wa Khristu wake zabwera. Pakuti woneneza abale athu uja, amene amangokhalira kuwaneneza pamaso pa Mulungu usana ndi usiku, wagwetsedwa pansi.
And I heard a loud voice saying in heaven, Now is come the salvation, and the power, and the kingdom of our God, and the authority of his Christ: for the accuser of our brethren is cast down, who accused them before our God day and night.
11 Abale athuwo anamugonjetsa ndi magazi a Mwana Wankhosa ndiponso mawu a umboni wawo. Iwo anadzipereka kwathunthu, moti sanakonde miyoyo yawo.
And they have overcome him by the blood of the Lamb, and by the word of their testimony, and they loved not their life unto the death.
12 Choncho, kondwerani, inu dziko lakumwamba ndi onse okhala kumeneko! Koma tsoka dziko lapansi ndi nyanja chifukwa Mdierekezi wagwetsedwa kwa inu! Iye wadzazidwa ndi ukali chifukwa akudziwa kuti nthawi yake ndi yochepa.”
Therefore rejoice, ye heavens, and ye that dwell in them: but wo to the inhabitants of the earth and of the sea; for the devil is come down to you, in great rage, knowing that he hath but a short time.
13 Pamene chinjokacho chinaona kuti chagwetsedwa pa dziko lapansi, chinayamba kuthamangitsa mayi uja amene anali atabala mwana wamwamunayu.
Now when the dragon saw that he was cast down to the earth, he persecuted the woman that brought forth the male-child:
14 Mayiyo anapatsidwa mapiko awiri a chiwombankhanga chachikulu kuti athawire ku malo ake aja a ku chipululu. Kumeneko adzasamalidwako zaka zitatu ndi theka kuti chinjoka chija chisamupeze.
and there were given to the woman two wings of a great eagle, that she might fly into the wilderness to her place, where she is to be nourished for a time, and times, and half a time, from the face of the serpent.
15 Kenaka chinjoka chija chinalavulira mayiyo madzi ambiri ngati mtsinje, kuti madziwo amukokolole.
And the serpent threw water out of his mouth, like a river, after the woman, that he might cause her to be carried away by the flood.
16 Koma dziko lapansi linamuthandiza mayiyo. Nthaka inatsekuka ndi kumeza mtsinje uja unachokera mʼkamwa mwa chinjokacho.
But the earth helped the woman, and opened it's mouth, and swallowed up the flood, which the dragon threw out of his mouth.
17 Pamenepo chinjokacho chinamupsera mtima mayiyo ndipo chinachoka kupita kukachita nkhondo ndi ana ena onse a mayiyo, ndiye kuti anthu amene anasunga malamulo a Mulungu ndi kuchitira umboni za Yesu.
Then the dragon was enraged against the woman, and went away to make war with the rest of her seed, who keep the commandments of God, and who have the testimony of Jesus Christ.

< Chivumbulutso 12 >