< Chivumbulutso 1 >

1 Vumbulutso lochokera kwa Yesu Khristu, limene Mulungu anamupatsa kuti aonetse atumiki ake zimene zinayenera kuchitika posachedwa. Iye anatuma mngelo wake kuti adziwitse mtumiki wake Yohane,
مکاشفه عیسی مسیح که خدا به او داد تا اموری را که می‌باید زود واقع شود، برغلامان خود ظاهر سازد و بوسیله فرشته خودفرستاده، آن را ظاهر نمود بر غلام خود یوحنا،۱
2 amene akuchitira umboni chilichonse chimene anachiona. Awa ndi Mawu a Mulungu ndi umboni wa Yesu Khristu.
که گواهی داد به کلام خدا و به شهادت عیسی مسیح در اموری که دیده بود.۲
3 Ngodala munthu amene awerenga mawu oneneratu zamʼtsogolo ndi iwo amene amamva ndi kusunga zolembedwa mʼbukuli pakuti nthawi yayandikira.
خوشابحال کسی‌که می‌خواند و آنانی که می‌شنوند کلام این نبوت را، و آنچه در این مکتوب است نگاه می‌دارند، چونکه وقت نزدیک است.۳
4 Ndine Yohane, Kupita ku mipingo isanu ndi iwiri ya mʼchigawo cha Asiya. Chisomo ndi mtendere kwa inu, kuchokera kwa Iye amene ali, amene analipo ndi amene akubwera ndi kwa mizimu isanu ndi iwiri yokhala patsogolo pa mpando wake waufumu,
یوحنا، به هفت کلیسایی که در آسیا هستند.۴
5 ndiponso kuchokera kwa Yesu Khristu mboni yokhulupirika, woyamba kuukitsidwa, ndi wolamulira mafumu a dziko lapansi. Kwa Iye amene amatikonda ndipo watimasula ku machimo athu ndi magazi ake,
و از عیسی مسیح که شاهد امین ونخست زاده از مردگان و رئیس پادشاهان جهان است. مر او را که ما را محبت می‌نماید و ما را ازگناهان ما به خون خود شست،۵
6 ndipo watisandutsa mafumu ndi ansembe kuti tizitumikira Mulungu ndi Atate ake. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu ku nthawi zosatha, Ameni. (aiōn g165)
و ما را نزد خدا وپدر خود پادشاهان و کهنه ساخت، او را جلال وتوانایی باد تا ابدالاباد. آمین. (aiōn g165)۶
7 “Onani akubwera ndi mitambo,” ndipo “Aliyense adzamuona, ndi amene anamubaya omwe.” Ndipo anthu a mitundu yonse ya pa dziko lapansi “adzalira chingʼangʼadza chifukwa cha Iye.”
اینک با ابرها می‌آید و هر چشمی او راخواهد دید و آنانی که او را نیزه زدند و تمامی امت های جهان برای وی خواهند نالید. بلی!۷
8 “Ine ndine Alefa ndi Omega,” akutero Ambuye Mulungu Wamphamvuzonseyo “amene muli, amene munalipo, ndi amene mudzakhalapo.”
«من هستم الف و یا، اول و آخر، » می‌گویدآن خداوند خدا که هست و بود و می‌آید، قادرعلی الاطلاق.۸
9 Ine Yohane mʼbale wanu ndi mnzanu mʼmasautso ndi mu ufumu ndi mukupirira kwambiri, zomwe ndi zathu mwa Yesu, ndinali pa chilumba cha Patimo chifukwa cha Mawu a Mulungu ndi umboni wa Yesu.
من یوحنا که برادر شما و شریک در مصیبت و ملکوت و صبر در عیسی مسیح هستم، بجهت کلام خدا و شهادت عیسی مسیح در جزیره‌ای مسمی به پطمس شدم.۹
10 Pa tsiku la Ambuye ndinanyamulidwa ndi Mzimu ndipo ndinamva kumbuyo kwanga mawu ofuwula ngati lipenga,
و در روز خداوند درروح شدم و از عقب خود آوازی بلند چون صدای صور شنیدم،۱۰
11 amene anati, “Lemba mʼbuku zimene ukuziona ndipo uzitumize ku mipingo isanu ndi iwiri ya ku Efeso, Simurna, Pergamo, Tiyatira, Sarde, Filadefiya ndi ku Laodikaya.”
که می‌گفت: «من الف و یاو اول و آخر هستم. آنچه می‌بینی در کتابی بنویس و آن را به هفت کلیسایی که در آسیاهستند، یعنی به افسس و اسمیرنا و پرغامس وطیاتیرا و ساردس و فیلادلفیه و لائودکیه بفرست.»۱۱
12 Nditatembenuka kuti ndione amene amandiyankhulayo, ndinaona zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide.
پس رو برگردانیدم تا آن آوازی را که با من تکلم می‌نمود بنگرم؛ و چون رو گردانیدم، هفت چراغدان طلا دیدم،۱۲
13 Pakati pa zoyikapo nyalezo ndinaona wina wooneka ngati Mwana wa Munthu atavala mkanjo wofika kumapazi ake ndipo anamangirira lamba wagolide pa chifuwa pake.
و در میان هفت چراغدان، شبیه پسر انسان را که ردای بلند در بر داشت و برسینه وی کمربندی طلا بسته بود،۱۳
14 Tsitsi lake linali loyera ngati thonje, kuyera ngati matalala, ndipo maso ake amawala ngati malawi amoto.
و سر و موی او سفید چون پشم، مثل برف سفید بود و چشمان او مثل شعله آتش،۱۴
15 Mapazi ake anali ngati chitsulo choti chili mʼngʼanjo yamoto, ndipo mawu ake anali ngati mkokomo wamadzi othamanga.
و پایهایش مانند برنج صیقلی که در کوره تابیده شود، و آواز او مثل صدای آبهای بسیار؛۱۵
16 Mʼdzanja lake lamanja ananyamula nyenyezi zisanu ndi ziwiri, ndipo mʼkamwa mwake munali lupanga lakuthwa konsekonse. Nkhope yake imawala ngati dzuwa lowala kwambiri.
و در دست راست خود هفت ستاره داشت و از دهانش شمشیری دودمه تیز بیرون می‌آمد و چهره‌اش چون آفتاب بود که در قوتش می‌تابد.۱۶
17 Nditamuona ndinagwa pa mapazi ake ngati wakufa. Kenaka Iye anasanjika dzanja lake lamanja pa ine nati, “Usachite mantha. Ndine Woyamba ndi Wotsiriza.
و چون او را دیدم، مثل مرده پیش پایهایش افتادم و دست راست خود را بر من نهاده، گفت: «ترسان مباش! من هستم اول و آخر و زنده؛۱۷
18 Ine ndine Wamoyo; ndinali wakufa ndipo taona ndine wamoyo mpaka muyaya! Ndipo ndili ndi makiyi a imfa ndi Hade. (aiōn g165, Hadēs g86)
ومرده شدم و اینک تا ابدالاباد زنده هستم وکلیدهای موت و عالم اموات نزد من است. (aiōn g165, Hadēs g86)۱۸
19 “Chomwecho, lemba zimene waona, zimene zilipo panopa ndi zimene zidzachitike mʼtsogolo.
پس بنویس چیزهایی را که دیدی و چیزهایی که هستند و چیزهایی را که بعد از این خواهند شد،۱۹
20 Tanthauzo la nyenyezi zisanu ndi ziwiri zimene waziona mʼdzanja langa lamanja ndi la zoyikapo nyale zagolide zisanu ndi ziwiri ndi ili: Nyenyezi zisanu ndi ziwiri ndi angelo a mipingo isanu ndi iwiri ija, ndipo zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zija ndi mipingo isanu ndi iwiri ija.”
سر هفت ستاره‌ای را که در دست راست من دیدی و هفت چراغدان طلا را. اما هفت ستاره، فرشتگان هفت کلیسا هستند و هفت چراغدان، هفت کلیسا می‌باشند.۲۰

< Chivumbulutso 1 >