< Masalimo 1 >

1 Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Блаженна та людина, що не ходить на раду нечестивих, не стоїть на дорозі грішників і не сидить на зборищі глумливих!
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
Але в Законі Господнім її насолода і про Закон Його роздумує вдень та вночі.
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
І буде вона як дерево, посаджене над водними потоками, що плід свій дає вчасно, і листя його не зів’яне. Що б вона не робила, щаститиме їй.
4 Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
Не так нечестиві! [Вони] – як полова, що вітер розносить [усюди].
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
Тому не встоять нечестиві на суді ані грішники – на зборах праведних.
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
Адже знає Господь[життєвий] шлях праведних, а шлях нечестивих загине.

< Masalimo 1 >