< Masalimo 1 >

1 Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Błogosławiony mąż, który nie chodzi w radzie niepobożnych, a na drodze grzesznych nie stoi, i na stolicy naśniewców nie siedzi;
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
Ale w zakonie Pańskim jest kochanie jego, a w zakonie jego rozmyśla we dnie i w nocy.
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
Albowiem będzie jako drzewo nad strumieniem wód w sadzone, które owoc swój wydaje czasu swego, a liść jego nie opada; i wszystko, cokolwiek czynić będzie, poszczęści się.
4 Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
Lecz nie tak niepobożni; ale są jako plewa, którą wiatr rozmiata.
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
Przetoż się niepobożni na sądzie nie ostoją, ani grzesznicy w zgromadzeniu sprawiedliwych.
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
Albowiem zna Pan drogę sprawiedliwych; ale droga niepobożnych zginie.

< Masalimo 1 >