< Masalimo 1 >

1 Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Ubusisiwe umuntu ongahambi ngezeluleko zababi; ongemiyo endleleni yezoni; ongahlaliyo esihlalweni sabaklolodayo.
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
Kodwa ukuthokoza kwakhe kusemthethweni kaThixo, futhi unakana ngomthetho wakhe imini lobusuku.
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
Unjengesihlahla esihlanyelwe emifuleni yamanzi, esithela izithelo zaso ngesikhathi saso, ohlamvu laso kalibuni. Konke akwenzayo kuyaphumelela.
4 Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
Ababi kabanjalo! Banjengamakhoba aphetshulwa ngumoya.
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
Ngakho ababi kabayikuma ekwahlulelweni, noma izoni enkundleni yabalungileyo.
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
Ngoba uThixo uyayilinda indlela yabalungileyo, kodwa indlela yababi iya ekubhujisweni.

< Masalimo 1 >