< Masalimo 1 >

1 Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
[God] is pleased with those who do not do what [MET] wicked people advise them to do, and who do not imitate the behavior of [MET] sinful people, and who do not join in with people who (ridicule/sneer at) [God].
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
Those whom God is pleased with delight in doing the things that he has instructed/taught us to do. They read and think about Yahweh’s requirements, day and night.
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
They [constantly produce/do things that please God] just like fruit trees that have been planted along the banks of a stream produce fruit at the right time every year. [Like] trees that never wither, they succeed in everything that they do.
4 Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
But wicked people are not like that! Wicked people are [as worthless as] chaff that is blown away by the wind.
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
Therefore, wicked people (will not be acquitted/will be condemned) [LIT] when [God] judges people, and furthermore, sinful people will not even be present when [God] gathers righteous people together,
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
because he guides and protects righteous people, but the path that the wicked walk on leads them to where they will be destroyed/punished [by God forever].

< Masalimo 1 >