< Masalimo 1 >

1 Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Blessed is the man who has not followed the counsel of the impious, and has not remained in the way of sinners, and has not sat in the chair of pestilence.
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
But his will is with the law of the Lord, and he will meditate on his law, day and night.
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
And he will be like a tree that has been planted beside running waters, which will provide its fruit in its time, and its leaf will not fall away, and all things whatsoever that he does will prosper.
4 Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
Not so the impious, not so. For they are like the dust that the wind casts along the face of the earth.
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
Therefore, the impious will not prevail again in judgment, nor sinners in the council of the just.
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
For the Lord knows the way of the just. And the path of the impious will pass away.

< Masalimo 1 >