< Masalimo 99 >
1 Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
Господь царює – нехай тремтять народи! Він сидить на херувимах – нехай здригнеться земля!
2 Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
Господь великий на Сіоні, Він піднесений над усіма народами.
3 Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
Нехай прославлять вони ім’я Твоє велике й грізне: воно святе!
4 Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
Могутнє правління Царя любить правосуддя. Ти утвердив справедливість, здійснив суд і правду у Якова.
5 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
Піднесено славте Господа, Бога нашого, і вклоняйтеся біля підніжжя Його: Він святий!
6 Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
Мойсей і Аарон серед священників Його, і Самуїл серед тих, хто кличе Його ім’я; кликали вони до Господа, і Він відповідав їм.
7 Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
У хмарному стовпі говорив до них; вони ж дотримувалися Його одкровень і постанов, які Він дав їм.
8 Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
Господи, Боже наш, Ти відповідав їм! Ти був для них Богом, Який прощає, але й карав їх за провини їхні.
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
Піднесено славте Господа, Бога нашого, і вклоняйтеся на горі Його святій, бо святий Господь, Бог наш.